Obadiya 1:1-21

  • Anthu onyada a ku Edomu anachititsidwa manyazi (1-9)

  • Anthu a ku Edomu anachitira nkhanza Yakobo (10-14)

  • Tsiku la Yehova loweruza mitundu yonse (15, 16)

  • Nyumba ya Yakobo idzabwezeretsedwa (17-21)

    • Edomu adzatenthedwa ndi moto wa Yakobo (18)

    • Yehova adzakhala Mfumu (21)

 Awa ndi masomphenya a Obadiya:* Zimene Yehova Ambuye Wamkulu Koposa akunena zokhudza Edomu+ ndi izi: “Ife tamva uthenga wochokera kwa Yehova,Ndipo nthumwi yatumidwa kwa anthu amitundu ina kukanena kuti: ‘Konzekani! Tiyeni tikamenyane naye.’”+   “Taona! Ndakuchititsa kukhala wosafunika pakati pa mitundu ina,Ndipo ikukuona kuti ndiwe wonyozeka kwambiri.+   Mtima wako wodzikuza wakupusitsa,+Iwe amene ukukhala mʼmalo obisika amʼthanthwe,Uli pamwamba pa phiri nʼkumanena mumtima mwako kuti,‘Ndani angandigwetsere pansi?’   Ngakhale utamakhala mʼmwamba* ngati chiwombankhanga,Kapena utamanga chisa chako pakati pa nyenyezi,Ine ndidzakugwetsapo pamenepo,” akutero Yehova.   “Akuba atabwera kwa iwe, kapena mbava zitabwera usiku,Kodi sangabe zokhazo zimene akufuna? (Koma ndiye udzawonongedwatu!)* Kapena okolola mphesa atabwera kwa iwe,Kodi sangasiyeko zina zoti munthu nʼkukunkha?+   Koma Esau ndiye wafufuzidwatu! Anthu asakasaka chuma chake chonse chobisika nʼkuchitenga.   Anthu amene unachita nawo mgwirizano* akuthamangitsira kumalire. Onsewo akupusitsa. Anthu amene unkakhala nawo mwamtendere akugonjetsa. Anthu amene ukudya nawo limodzi adzakutchera ukonde,Koma iwe sudzazindikira.”   Yehova akuti: “Kodi pa tsiku limenelo,Sindidzawononga anthu anzeru mu Edomu,+Komanso anthu ozindikira mʼdera lamapiri la Esau?   Iwe Temani,+ asilikali ako adzachita mantha,+Chifukwa aliyense mʼdera lamapiri la Esau adzaphedwa.+ 10  Popeza unachitira nkhanza mʼbale wako Yakobo,+Udzachititsidwa manyazi kwambiri.+Udzaphedwa ndipo sudzakhalaponso mpaka kalekale.+ 11  Pa tsiku limene unangoima nʼkumaonerera,Pa tsiku limene adani* anagwira gulu la asilikali a mʼbale wako nʼkupita nawo ku ukapolo,+Ndiponso pamene anthu akudziko lina analowa mumzinda* wake nʼkuchita maere+ pa Yerusalemu,Iwe unali ngati mmodzi wa adaniwo. 12  Iwe sumayenera kunyadira pa tsiku limene mʼbale wako anakumana ndi tsoka,+Sumayenera kusangalala pa tsiku limene anthu a ku Yuda ankawonongedwa,+Sumayeneranso kulankhula modzitama pa tsiku limene ankazunzika. 13  Iwe sumayenera kulowa mumzinda* wa anthu anga pa tsiku limene anakumana ndi tsoka.+Sumayenera kunyadira pamene mʼbale wako ankavutika pa tsiku limene anakumana ndi tsoka.Ndipo sumayeneranso kutenga chuma chake pa tsiku limene anakumana ndi tsoka.+ 14  Iwe sumayenera kuima panjira kuti uzipha anthu ake amene akuthawa.+Sumayeneranso kugwira anthu ake amene apulumuka nʼkuwapereka kwa adani awo pa tsiku limene ankazunzika.+ 15  Tsiku la Yehova limene adzalange mitundu yonse ya anthu lili pafupi.+ Zimene wachitira mʼbale wako, iwenso adzakuchitira zomwezo.+ Zimene unachitira anthu ena zidzakubwerera pamutu pako. 16  Mmene wamwera vinyo paphiri langa loyera,Ndi mmenenso mitundu ina yonse ya anthu izidzamwera mkwiyo wanga nthawi zonse.+ Iwo adzamwa ndi kugugudiza mkwiyo wanga,Ndipo zidzakhala ngati sanakhalepo nʼkomwe. 17  Anthu onse opulumuka adzakhala paphiri la Ziyoni+Ndipo phiri limeneli lidzakhala loyera.+Anthu a mʼbanja la Yakobo adzatenganso zinthu zimene zinali zawo.+ 18  A mʼbanja la Yakobo adzakhala ngati moto,A mʼbanja la Yosefe adzakhala ngati malawi a moto,Ndipo a mʼbanja la Esau adzakhala ngati mapesi.Moto wawo udzayatsa ndi kunyeketsa mapesiwo,Ndipo palibe aliyense wa mʼbanja la Esau amene adzapulumuke,+Chifukwa Yehova ndi amene wanena. 19  Iwo adzatenga dera la Negebu ndi dera lamapiri la Esau,+Komanso dera la Sefela ndi dera la Afilisiti.+ Adzatenganso madera a Efuraimu ndi Samariya,+Ndipo Benjamini adzatenga dera la Giliyadi. 20  Anthu amene anatengedwa pamalo okwera omenyerapo nkhondowa nʼkupita nawo kudziko lina,+Amene ndi Aisiraeli, adzatenga dziko la Akanani mpaka kukafika ku Zarefati.+ Anthu amene anatengedwa kuchokera ku Yerusalemu, amene anali ku Sefaradi, adzatenga mizinda ya Negebu.+ 21  Opulumutsa adzakwera paphiri la ZiyoniKuti aweruze dera lamapiri la Esau,+Ndipo Yehova adzakhala Mfumu.”+

Mawu a M'munsi

Kutanthauza “Mtumiki wa Yehova.”
Mabaibulo ena amati, “utaulukira mʼmwamba.”
Mabaibulo ena amati, “Kodi angawononge zambiri bwanji?”
Kapena kuti, “pangano.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “anthu achilendo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “pageti.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “pageti.”