Oweruza 12:1-15

  • Anakangana ndi amuna a ku Efuraimu (1-7)

    • Anawayesa ndi mawu akuti “Shiboleti” (6)

  • Oweruza Ibizani, Eloni ndi Abidoni (8-15)

12  Ndiyeno amuna a ku Efuraimu anasonkhana pamodzi nʼkuwoloka kupita ku Zafoni,* ndipo anauza Yefita kuti: “Nʼchifukwa chiyani unapita kukamenyana ndi Aamoni osatiitana kuti tipite limodzi?+ Tiwotcha nyumba yako iwe uli momwemo.”  Koma Yefita anawauza kuti: “Ineyo ndi anthu anga tinalimbana koopsa ndi Aamoni. Ndinakuitanani kuti mudzandithandize koma simunandipulumutse mʼmanja mwawo.  Nditaona kuti inu simukubwera kudzandipulumutsa, ndinalolera kufa,* moti ndinapita kukamenyana ndi Aamoni,+ ndipo Yehova anawapereka mʼmanja mwanga. Ndiye nʼchifukwa chiyani lero mwabwera kudzamenyana nane?”  Kenako Yefita anasonkhanitsa amuna onse a ku Giliyadi+ nʼkumenyana ndi anthu a ku Efuraimu. Amuna a ku Giliyadi anagonjetsa anthu a ku Efuraimu, amene mʼmbuyomo ankati: “Ngakhale kuti inu anthu a ku Giliyadi mukukhala mʼdera la Efuraimu ndi la Manase, ndinu anthu othawa ku Efuraimu.”  Amuna a ku Giliyadi anakatchinga powolokera Yorodano+ anthu a ku Efuraimu asanafike. Ndiyeno munthu aliyense wa ku Efuraimu amene ankathawa akanena kuti: “Ndiloleni ndiwoloke,” amuna a ku Giliyadi ankamufunsa kuti: “Kodi ndiwe wa ku Efuraimu?” Akayankha kuti: “Ayi!”  ankamuuza kuti: “Nena kuti Shiboleti.” Koma iye ankanena kuti: “Siboleti,” chifukwa sankatha kutchula mawuwa molondola. Akatero ankamugwira nʼkumuphera powolokera Yorodano pomwepo. Anthu a ku Efuraimu amene anaphedwa pa nthawiyi anali okwana 42,000.  Yefita wa ku Giliyadi anaweruza Isiraeli zaka 6. Kenako anamwalira ndipo anaikidwa mʼmanda mumzinda wakwawo ku Giliyadi.  Yefita atamwalira, Ibizani wa ku Betelehemu anayamba kuweruza Isiraeli.+  Ibizani anali ndi ana aamuna 30 ndi ana aakazi 30. Iye anakonza zoti ana ake aakazi akwatiwe ndi amuna a mafuko ena komanso anatuma anthu kukatenga atsikana 30 kuchokera kwina kuti akhale akazi a ana ake aamuna. Ibizani anaweruza Isiraeli kwa zaka 7. 10  Kenako Ibizani anamwalira ndipo anaikidwa mʼmanda ku Betelehemu. 11  Ibizani atamwalira, Eloni wa fuko la Zebuloni anayamba kuweruza Isiraeli ndipo anaweruza Isiraeli zaka 10. 12  Kenako Eloni wa fuko la Zebuloni anamwalira, ndipo anaikidwa mʼmanda ku Aijaloni mʼdera la Zebuloni. 13  Eloni atamwalira, Abidoni mwana wa Hilele wa ku Piratoni, anayamba kuweruza Isiraeli. 14  Iye anali ndi ana aamuna 40 ndi zidzukulu 30. Onsewa ankayenda pa abulu 70. Abidoni anaweruza Isiraeli zaka 8. 15  Kenako Abidoni mwana wa Hilele wa ku Piratoni anamwalira, ndipo anaikidwa mʼmanda ku Piratoni, mʼdera la Efuraimu, mʼphiri la Aamaleki.+

Mawu a M'munsi

Mabaibulo ena amati, “nʼkuwoloka ndipo analowera chakumpoto.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “ndinaika moyo wanga mʼdzanja langa.”