Rute 1:1-22

  • Banja la Elimeleki linasamukira ku Mowabu (1, 2)

  • Naomi, Olipa ndi Rute anakhala amasiye (3-6)

  • Rute anakhala wokhulupirika kwa Naomi ndi Mulungu wake (7-17)

  • Naomi anabwerera ku Betelehemu ndi Rute (18-22)

1  Tsopano, pa nthawi imene oweruza+ ankatsogolera* ku Isiraeli, mʼdzikomo munagwa njala. Ndiyeno munthu wina anasamuka ku Betelehemu+ wa ku Yuda nʼkukakhala ngati mlendo ku Mowabu.+ Anasamuka ndi mkazi wake ndi ana ake awiri aamuna.  Munthuyu dzina lake anali Elimeleki,* ndipo mkazi wake anali Naomi.* Mayina a ana akewo anali Maloni* ndi Kiliyoni.* Anthuwa anali a ku Betelehemu Efurata wa ku Yuda. Ndipo anafika ku Mowabu nʼkumakhala kumeneko.  Patapita nthawi, Elimeleki mwamuna wa Naomi anamwalira ndipo Naomi anatsala ndi ana ake aja.  Kenako anawo anakwatira akazi a Chimowabu. Wina dzina lake anali Olipa ndipo wina anali Rute.+ Iwo anakhalabe kumeneko zaka pafupifupi 10.  Patapita nthawi, ana awiriwo, Maloni ndi Kiliyoni, nawonso anamwalira, ndipo Naomi anatsala yekha wopanda ana komanso mwamuna.  Choncho iye ndi apongozi ake anayamba ulendo wochoka ku Mowabu kubwerera kwawo, chifukwa anamva kuti Yehova wakumbukira anthu ake powapatsa chakudya.  Choncho Naomi ndi apongozi ake awiri aja ananyamuka kumene ankakhala. Ali mʼnjira pa ulendo wobwerera ku Yuda,  Naomi anauza apongozi akewo kuti: “Basi bwererani, aliyense apite kunyumba kwa amayi ake. Yehova akusonyezeni chikondi chokhulupirika+ ngati mmenenso inuyo munasonyezera chikondichi kwa amuna anu amene anamwalira ndiponso kwa ine.  Yehova akudalitseni ndipo aliyense akapeze chitetezo* mʼnyumba ya mwamuna wake.”+ Kenako anawakisa ndipo iwo anayamba kulira mokweza. 10  Iwo ankanena kuti: “Ayi sitibwerera, ife tipita nanu kwanu.” 11  Koma Naomi anati: “Bwererani ana anga. Palibe chifukwa choti tipitire limodzi. Kodi ndingathe kuberekanso ana amene angadzakhale amuna anu?+ 12  Bwererani ana anga, pitani, chifukwa ndakalamba kwambiri moti sindingakwatiwenso. Ngakhale nditapeza mwamuna pofika usiku wa lero nʼkubereka ana aamuna, 13  kodi mungawadikire mpaka atakula? Kodi mungadzisungebe osakwatiwanso kuti mudzakwatiwe ndi iwowo? Ayi ndithu ana anga, zimene zinakuchitikirani zimandiwawa kwambiri, chifukwa dzanja la Yehova landiukira.”+ 14  Atatero iwo analiranso mokweza. Kenako Olipa anakisa apongozi akewo nʼkubwerera. Koma Rute sanalole kusiyana nawo. 15  Choncho Naomi anati: “Taona mchemwali wako wamasiye wabwerera kwa anthu a kwawo komanso kwa milungu yake. Iwenso bwerera.” 16  Koma Rute anati: “Musandichonderere kuti ndikusiyeni, kuti ndibwerere ndisakutsatireni, chifukwa kumene inu mupite inenso ndipita komweko ndipo kumene mugone inenso ndigona komweko. Anthu a mtundu wanu adzakhala anthu a mtundu wanga ndipo Mulungu wanu adzakhala Mulungu wanga.+ 17  Kumene inu mudzafere inenso ndidzafera komweko ndipo ndidzaikidwanso komweko. Yehova andilange kwambiri ngati chinachake kupatulapo imfa chingandisiyanitse ndi inu.” 18  Naomi ataona kuti Rute walimbikira zoti apite naye, anasiya kumuuza kuti abwerere. 19  Ndipo anapitiriza ulendo wawo mpaka anafika ku Betelehemu.+ Atangofika ku Betelehemu, mumzinda wonsewo anthu anayamba kulankhula za iwo. Azimayi ankafunsa kuti: “Kodi si Naomi uyu?” 20  Koma Naomi ankawayankha kuti: “Musanditchulenso kuti Naomi,* muzinditchula kuti Mara,* chifukwa Wamphamvuyonse wachititsa kuti moyo wanga ukhale wowawa kwambiri.+ 21  Ndinali ndi zonse pochoka kuno, koma Yehova wandibweza wopanda kanthu. Munditchula bwanji kuti Naomi, popeza Yehova ndi amene wandiukira ndipo Wamphamvuyonseyo ndi amene wandigwetsera tsokali?”+ 22  Izi ndi zomwe zinachitika pamene Naomi ankabwerera kwawo kuchokera ku Mowabu.+ Iye anabwerera ndi mpongozi wake Rute wa ku Mowabu. Iwo anafika ku Betelehemu kumayambiriro kwa nthawi yokolola balere.+

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “ankaweruza.”
Kutanthauza “Mulungu Wanga Ndi Mfumu.”
Kutanthauza “Wosangalatsa.”
Nʼkutheka kuti linachokera ku mawu a Chiheberi otanthauza, “kufooka kapena kudwala.”
Kutanthauza “Wolephera; Wotsirizika.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mpumulo.”
Kutanthauza “Wosangalatsa.”
Kutanthauza “Kuwawa.”