Rute 2:1-23

  • Rute anakakunkha mʼmunda wa Boazi (1-3)

  • Rute anakumana ndi Boazi (4-16)

  • Rute anauza Naomi kuti Boazi anamukomera mtima (17-23)

2  Panali munthu wina wolemera kwambiri yemwe anali wachibale wa mwamuna wake wa Naomi. Dzina lake anali Boazi+ ndipo anali wa kubanja la Elimeleki.  Rute mkazi wa ku Mowabu uja anauza Naomi kuti: “Bwanji ndipite ndikakunkhe+ balere mʼmunda wa aliyense amene angandikomere mtima?” Ndipo Naomi anamuyankha kuti: “Pita mwana wanga.”  Zitatero Rute ananyamuka nʼkupita ndipo anakalowa mʼmunda wina nʼkuyamba kukunkha pambuyo pa anthu okolola. Ndiye zinangochitika kuti mundawo unali wa Boazi,+ wa kubanja la Elimeleki.+  Pasanapite nthawi, Boazi anafika kuchokera ku Betelehemu ndipo analonjera okololawo kuti: “Yehova akhale nanu.” Iwo anayankha kuti: “Yehova akudalitseni.”  Kenako Boazi anafunsa mnyamata amene ankayangʼanira okololawo kuti: “Kodi mtsikanayu ndi wakubanja liti?”  Mnyamatayo anayankha kuti: “Mtsikanayu ndi Mmowabu,+ anabwera limodzi ndi Naomi kuchokera ku Mowabu.+  Atafika anapempha kuti, ‘Ndimati ndikunkhe nawo.+ Ndizitola balere* wotsala pambuyo pa anthu amene akukololawa.’ Ndipo wakhala akukunkha kuyambira mʼmawa mpaka posachedwapa pamene anakhala pamthunzi kuti apume pangʼono.”  Kenako Boazi anauza Rute kuti: “Tamvera mwana wanga, usapitenso kumunda wina kukakunkha. Usachoke kupita kwina, uzikhala pafupi ndi atsikana anga antchitowa.+  Uzingoyangʼana mbali imene akukolola ndipo uziwatsatira. Anyamatawa ndawalamula kuti asakuvutitse.* Ukamva ludzu, uzipita kukamwa madzi amene ali mʼmitsukoyo, omwe anyamatawa atunga.” 10  Atamva zimenezi anagwada nʼkuwerama mpaka nkhope yake pansi, nʼkunena kuti: “Zatheka bwanji kuti mundiganizire ndi kundikomera mtima chonchi, ine wokhala mlendo?”+ 11  Boazi anamuyankha kuti: “Ndamva zonse zimene wachitira apongozi ako kuchokera pamene mwamuna wako anamwalira. Ndamvanso kuti unasiya bambo ako ndi mayi ako komanso dziko lakwanu, nʼkubwera kuno kwa anthu osawadziwa.+ 12  Yehova akupatse mphoto chifukwa cha zimene wachita,+ ndipo Yehova, Mulungu wa Isiraeli akulipire mokwanira* popeza wathawira mʼmapiko mwake kuti upeze chitetezo.”+ 13  Rute atamva zimenezi anati: “Mwandikomera mtima mbuyanga. Mwandilimbikitsa komanso mwalankhula mondilimbitsa mtima ngakhale kuti si ine mmodzi wa antchito anu.” 14  Pa nthawi ya chakudya Boazi anauza Rute kuti: “Bwera kuno udzadye mkate. Ukhozanso kumasunsa mu vinyo wowawasayu.” Choncho Rute anapita nʼkukakhala pansi limodzi ndi okololawo. Ndiyeno Boazi ankamupatsa balere wokazinga ndipo iye anadya nʼkukhuta mpaka wina kutsala. 15  Atatha kudya ananyamuka nʼkukayambanso kukunkha.+ Boazi analamula anyamata ake kuti: “Muzimulola kukunkha barele* ndipo musamʼvutitse.+ 16  Komanso, muzisolola balere wina pamitolopo nʼkumamusiya pansi kuti iye akunkhe ndipo musamuletse kukunkha.” 17  Choncho Rute anapitiriza kukunkha mʼmundamo mpaka madzulo.+ Atamaliza kumenya balere amene anakunkhayo anakwana pafupifupi muyezo umodzi wa efa.* 18  Atatero ananyamula balereyo nʼkubwerera kunyumba, ndipo apongozi ake anaona balere amene anakunkhayo. Kenako Rute anatenga chakudya chimene chinatsala+ chija nʼkuwapatsa apongozi akewo. 19  Tsopano apongozi ake anamʼfunsa kuti: “Kodi lero unakakunkha kuti? Adalitsike amene wakuganizirayo.”+ Ndiyeno iye anauza apongozi akewo za munda umene anakakunkhamo. Anawauza kuti: “Munda umene ndakunkhamo lero, eniake ndi a Boazi.” 20  Atatero Naomi anauza mpongozi wakeyo kuti: “Yehova amene sanaleke kusonyeza chikondi chokhulupirika kwa amoyo ndi akufa, amudalitse munthu ameneyu.”+ Ndipo Naomi anapitiriza kuti: “Munthuyutu ndi wachibale wathu.+ Ndi mmodzi wa otiwombola.”+ 21  Ndiyeno Rute mkazi wa Chimowabuyo anati: “Moti anandiuzanso kuti, ‘Usachoke, uzikhala pafupi ndi antchito angawa mpaka adzamalize kukolola.’”+ 22  Naomi anauza Rute mpongozi wakeyo kuti: “Zingakhale bwinodi mwana wanga, uzipita limodzi ndi atsikana akewo, kusiyana nʼkuti akakuchite chipongwe kumunda wina.” 23  Choncho Rute anapitiriza kukhala pafupi ndi atsikana antchito a Boazi, mpaka pamene anamaliza kukolola balere+ ndi tirigu. Ndipo ankakhalabe ndi apongozi ake.+

Mawu a M'munsi

Mabaibulo ena amati, “mitolo ya balere.”
Kapena kuti, “asakusokoneze.”
Kapena kuti, “akupatse mphoto yokwanira.”
Mabaibulo ena amati, “mitolo ya balere.”
Pafupifupi malita 22. Onani Zakumapeto B14.