Kalata Yopita kwa Tito 3:1-15

  • Kugonjera koyenera (1-3)

  • Kukonzekera ntchito zabwino (4-8)

  • Kupewa mpatuko komanso kutsutsana pa zinthu zopusa (9-11)

  • Malangizo ena komanso moni (12-15)

3  Pitiriza kuwakumbutsa kuti azigonjera ndiponso kumvera maboma ndi olamulira.+ Akhalenso okonzeka kugwira ntchito iliyonse yabwino.  Asamanenere zoipa munthu aliyense ndiponso asamakonde kukangana. Koma akhale ololera+ ndipo azikhala ofatsa kwa anthu onse.+  Paja nafenso poyamba tinali opanda nzeru, osamvera, osocheretsedwa, akapolo a zilakolako zosiyanasiyana ndiponso a zinthu zosangalatsa, ochita zoipa, akaduka, onyansa komanso tinkadana.  Koma Mpulumutsi wathu Mulungu+ atasonyeza kukoma mtima ndi kukonda anthu,  (osati chifukwa cha ntchito zolungama zimene tinachita,+ koma chifukwa cha chifundo chake),+ anatipulumutsa potisambitsa kuti tifike ku moyo watsopano.+ Komanso anatipulumutsa potithandiza ndi mzimu woyera kuti tikhale atsopano.+  Iye anatikhuthulira mzimu umenewu kudzera mwa Yesu Khristu Mpulumutsi wathu,+  kuti titayesedwa olungama chifukwa cha kukoma mtima kwake kwakukulu,+ tingakhale olandira cholowa+ mogwirizana ndi chiyembekezo cha moyo wosatha.+  Mawu amenewa ndi oona, ndipo ndikufuna kuti upitirize kutsindika zinthu zimenezi, kuti amene akhulupirira Mulungu aziganizira kwambiri mmene angapitirizire kuchita ntchito zabwino. Zimenezi nʼzabwino ndiponso zothandiza kwa anthu.  Koma iwe uzipewa kutsutsana pa zinthu zopusa komanso zokhudza mibadwo ya makolo. Uzipewanso kukangana ndi kulimbana ndi anthu pa nkhani zokhudza Chilamulo, chifukwa zimenezi nʼzosathandiza ndiponso zopanda phindu.+ 10  Munthu wolimbikitsa mpatuko,+ ukamudzudzula* koyamba ndi kachiwiri,+ usagwirizane nayenso+ 11  podziwa kuti munthu woteroyo wasochera, akuchimwa ndipo akudziimba mlandu. 12  Ndikadzatuma Atema kapena Tukiko+ kwa iwe, udzayesetse kuti udzandipeze ku Nikopoli, chifukwa ndaganiza zokakhala kumeneko nyengo yozizirayi. 13  Zena, wodziwa Chilamulo uja, komanso Apolo, uwapatse zinthu zofunika pa ulendo zokwanira, kuti asasowe kanthu.+ 14  Koma abale athu aphunzire kugwira ntchito zabwino kuti azitha kuthandiza pakafunika kutero,+ kuti asakhale opanda phindu.+ 15  Onse amene ndili nawo kuno akupereka moni. Undiperekere moni kwa anthu amene amatikonda chifukwa tili ndi chikhulupiriro chofanana. Kukoma mtima kwakukulu kukhale ndi nonsenu.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “ukamuchenjeza.”