Kalata ya Yakobo 1:1-27

  • Moni (1)

  • Kupirira kumachititsa kuti tikhale osangalala (2-15)

    • Chikhulupiriro chimakhala cholimba tikamayesedwa (3)

    • Tizipempha ndi chikhulupiriro (5-8)

    • Chilakolako chimabweretsa uchimo ndi imfa (14, 15)

  • Mphatso iliyonse yabwino imachokera kumwamba (16-18)

  • Kumva ndi kuchita zimene mawu akunena (19-25)

    • Munthu amene akudziyangʼanira pagalasi (23, 24)

  • Kulambira koyera komanso kosadetsedwa (26, 27)

1  Ine Yakobo,+ kapolo wa Mulungu ndi wa Ambuye Yesu Khristu, ndikulembera mafuko 12 amene anamwazikana mʼmadera osiyanasiyana. Landirani moni!  Abale anga, muzisangalala kwambiri pamene mukukumana ndi mayesero osiyanasiyana,+  chifukwa monga mukudziwira, chikhulupiriro chanu chikakhalabe cholimba pamene mukuyesedwa, mumaphunzira kukhala opirira.+  Koma lolani kuti kupirirako kumalize kugwira ntchito yake, kuti mukhale okwanira ndi opanda cholakwa pa mbali iliyonse, kapena kuti mukhale ndi makhalidwe onse abwino.+  Choncho ngati wina akusowa nzeru, azipempha kwa Mulungu+ ndipo adzamupatsa,+ chifukwa iye amapereka mowolowa manja kwa onse ndiponso amapereka mosatonza.*+  Koma azipempha ndi chikhulupiriro,+ asamakayikire ngakhale pangʼono,+ chifukwa amene akukayikira ali ngati funde lapanyanja limene limatengeka ndi mphepo nʼkumawindukawinduka.  Munthu wotero asayembekezere kuti adzalandira kanthu kuchokera kwa Yehova.*  Iye ndi wokayikakayika+ ndipo zochita zake zonse zimasinthasintha.  Mʼbale wonyozeka asangalale* chifukwa walemekezedwa ndi Mulungu,+ 10  ndipo wachuma asangalale chifukwa waphunzira kukhala wodzichepetsa,+ chifukwa mofanana ndi duwa lakutchire, iye adzafota. 11  Dzuwa likatuluka limatentha kwambiri nʼkufotetsa zomera ndipo maluwa a zomerazo amathothoka moti kukongola kwake kumatha. Mofanana ndi zimenezi munthu wachumayo adzafa ali mkati mofunafuna chuma.+ 12  Wosangalala ndi munthu amene akupirira mayesero,+ chifukwa akadzavomerezedwa, adzalandira mphoto* ya moyo,+ imene Yehova* analonjeza onse amene akupitiriza kumukonda.+ 13  Munthu akakhala pa mayesero asamanene kuti: “Mulungu akundiyesa.” Chifukwa Mulungu sangayesedwe ndi zinthu zoipa ndipo iye sayesa munthu ndi zinthu zoipa. 14  Koma munthu aliyense amayesedwa ndi chilakolako chake chimene chimamukopa* ndi kumukola.+ 15  Ndiye chilakolako chikatenga pakati, chimabereka tchimo. Ndipo tchimo likachitika, limabweretsa imfa.+ 16  Abale anga okondedwa, musasocheretsedwe. 17  Mphatso iliyonse yabwino ndi yangwiro imachokera kumwamba.+ Imatsika kuchokera kwa Atate wa zounikira zakuthambo,+ amene sasintha ngati mthunzi umene umasunthasuntha.+ 18  Mwakufuna kwake, iye anatibereka pamene tinakhulupirira mawu ake omwe ndi choonadi.+ Anachita zimenezi kuti tikhale zipatso zoyambirira pa zolengedwa zake.+ 19  Abale anga okondedwa, dziwani izi: Munthu aliyense azikhala wokonzeka kumvetsera, aziganiza kaye asanalankhule+ komanso asamafulumire kukwiya,+ 20  chifukwa munthu amene wakwiya sachita zinthu mogwirizana ndi chilungamo cha Mulungu.+ 21  Choncho siyani khalidwe lililonse lonyansa ndipo chotsani zoipa zilizonse* zimene zatsalira mwa inu.+ Modzichepetsa vomerezani kuti mawu amene angathe kukupulumutsani adzalidwe mwa inu. 22  Komabe muzichita zimene mawu amanena,+ osati kungomva chabe, nʼkumadzipusitsa ndi maganizo abodza. 23  Chifukwa ngati munthu amangomva mawu koma osachita,+ amafanana ndi munthu amene akudziyangʼanira nkhope yake pagalasi. 24  Iye amadziyangʼana nʼkuchokapo ndipo nthawi yomweyo amaiwala kuti ndi munthu wotani. 25  Koma amene amayangʼanitsitsa mulamulo langwiro+ limene limabweretsa ufulu ndipo amapitiriza kuliyangʼanitsitsa, adzakhala wosangalala ndi zimene akuchita+ chifukwa chakuti si munthu amene amangomva nʼkuiwala, koma amene amachita zimene wamvazo. 26  Ngati munthu akuganiza kuti amalambira Mulungu,* koma satha kulamulira lilime lake,+ akudzipusitsa* ndipo kulambira kwake nʼkopanda phindu. 27  Kulambira* koyera komanso kosadetsedwa kwa Mulungu ndi Atate wathu ndi uku: Kusamalira ana amasiye+ ndi akazi amasiye+ amene akukumana ndi mavuto*+ komanso kupewa kuti dzikoli likuchititseni kukhala ndi banga.+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “amapereka popanda kupezera aliyense zifukwa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “adzitamandire.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “chisoti chachitsulo chooneka ngati nkhata.”
Kapena kuti, “chimamukopa ngati nyambo.”
Mabaibulo ena amati, “zoipa zambirimbiri.”
Kapena kuti, “ndi wopembedza.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “akupusitsa mtima wake.”
Kapena kuti, “Chipembedzo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼmasautso awo.”