Kalata ya Yakobo 5:1-20

  • Anachenjeza anthu achuma (1-6)

  • Mulungu amadalitsa anthu amene amayembekezera moleza mtima (7-11)

  • Mukati “ayi,” azikhaladi ayi (12)

  • Pemphero lachikhulupiriro limagwira ntchito (13-18)

  • Kuthandiza munthu wochimwa kuti abwerere (19, 20)

5  Tamverani inu anthu achuma. Lirani mofuula chifukwa cha masautso amene akubwera kwa inu.+  Chuma chanu chawola ndipo zovala zanu zadyedwa ndi njenjete.*+  Golide ndi siliva wanu wawonongeka ndi dzimbiri. Dzimbiri limenelo lidzakhala umboni wokutsutsani ndipo lidzadya mnofu wanu. Zimene mwasunga zidzakhala ngati moto mʼmasiku otsiriza.+  Tamverani! Malipiro amene simunapereke kwa anthu amene anagwira ntchito yokolola mʼminda yanu akufuula ndipo Yehova* wa magulu ankhondo akumwamba wamva kufuula kopempha thandizo kwa anthu okololawo.+  Mwakhala moyo wa mwanaalirenji ndipo dziko lapansi mwalidyerera. Mwadya ndipo mwanenepa ngati nyama pa tsiku limene ikukaphedwa.+  Mwaweruza ndiponso kupha munthu wolungama. Iye akukutsutsani.  Choncho lezani mtima abale, mpaka kukhalapo kwa Ambuye.+ Ganizirani mmene mlimi amachitira. Iye amayembekezerabe zipatso zamtengo wapatali zochokera munthaka. Amayembekezera moleza mtima mpaka mvula yoyamba komanso mvula yomaliza itagwa.+  Inunso khalani oleza mtima.+ Limbitsani mitima yanu, chifukwa kukhalapo kwa Ambuye kwayandikira.+  Musamadandaule za ena* abale, kuti musaweruzidwe.+ Taonani, Woweruza waima pakhomo. 10  Abale, pa nkhani ya kumva zowawa+ ndi kuleza mtima,+ tengerani chitsanzo cha aneneri amene analankhula mʼdzina la Yehova.*+ 11  Monga mmene mukudziwira, anthu amene anapirira timawaona kuti ndi odala.*+ Munamva za kupirira kwa Yobu+ ndipo mukudziwa madalitso amene Yehova* anamupatsa.+ Mukuona nokha kuti Yehova* ndi wachikondi chachikulu komanso wachifundo.+ 12  Koma koposa zonse abale anga, siyani kulumbira, potchula kumwamba kapena dziko lapansi kapena lumbiro lina lililonse. Koma mukati “Inde,” azikhaladi inde ndipo mukati “Ayi,” azikhaladi ayi+ kuti musakhale oyenera kuweruzidwa. 13  Kodi pali aliyense amene akukumana ndi mavuto pakati panu? Apitirize kupemphera.+ Kodi pali aliyense amene akusangalala? Aimbe nyimbo zotamanda Mulungu.+ 14  Kodi pali aliyense amene akudwala pakati panu? Aitane akulu+ a mpingo, ndipo iwo amupempherere ndi kumupaka+ mafuta mʼdzina la Yehova.* 15  Pemphero lachikhulupiriro lidzachiritsa munthu amene akudwalayo* ndipo Yehova* adzamulimbitsa. Komanso ngati anachita machimo, adzakhululukidwa. 16  Choncho muululirane machimo anu poyera+ ndi kupemphererana, kuti muchiritsidwe. Pemphero lopembedzera la munthu wolungama limagwira ntchito mwamphamvu kwambiri.*+ 17  Eliya anali munthu ngati ife tomwe, komabe atapemphera kuchokera pansi pamtima kuti mvula isagwe, mvula sinagwedi mʼdzikolo kwa zaka zitatu ndi miyezi 6.+ 18  Kenako anapempheranso ndipo mvula inagwa kuchokera kumwamba moti nthaka inatulutsa zipatso zake.+ 19  Abale anga, ngati wina pakati panu wasiya choonadi chifukwa chosocheretsedwa, ndiye munthu wina nʼkumubweza, 20  dziwani kuti amene wabweza wochimwayo panjira yake yoipa,+ wamupulumutsa ku imfa ndipo Mulungu adzakhululukira wochimwayo machimo ambiri.+

Mawu a M'munsi

Mawu a Chigiriki amene amasuliridwa kuti “njenjete” amatanthauza mtundu winawake wa kadziwotche amene amadya zovala.
Kapena kuti, “Musamangʼungʼudze za ena.”
Kapena kuti, “osangalala.”
Mabaibulo ena amati, “amene watopayo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “limakhala lamphamvu kwambiri pamene likugwira ntchito.”