Yeremiya 11:1-23

  • Yuda anaphwanya pangano limene anapanga ndi Mulungu (1-17)

    • Anali ndi milungu yochuluka mofanana ndi mizinda yawo (13)

  • Yeremiya anali ngati mwana wa nkhosa amene akupita kukaphedwa (18-20)

  • Yeremiya anatsutsidwa ndi anthu akwawo (21-23)

11  Mawu amene Yehova anauza Yeremiya ndi awa:  “Imvani mawu a pangano langa, anthu inu! Anthu a ku Yuda komanso okhala mu Yerusalemu ukawauze* mawu amenewa.  Ukawauze kuti, ‘Yehova Mulungu wa Isiraeli wanena kuti: “Munthu aliyense wosamvera mawu a mʼpangano limeneli ndi wotembereredwa.+  Makolo anu ndinawalamula kuti azimvera mawu amenewa pamene ndinkawatulutsa mʼdziko la Iguputo,+ pamene ndinkawatulutsa mʼngʼanjo yosungunulira zitsulo.+ Ndinawalamula kuti, ‘Muzimvera mawu anga, ndipo muzichita zinthu zonse zimene ndakulamulani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndipo ine ndidzakhala Mulungu wanu,+  kuti ndikwaniritse lumbiro limene ndinalumbirira makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,+ ngati mmene zilili lero.’”’” Pamenepo ine ndinayankha kuti: “Zikhale momwemo,* inu Yehova.”  Kenako Yehova anandiuza kuti: “Ulengeze mawu onsewa mʼmizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya Yerusalemu kuti: ‘Imvani mawu a pangano langa ndipo muchite zimene mawuwo akunena.  Inetu ndinkalangiza makolo anu pa tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Iguputo ndipo ndikupitiriza mpaka pano. Ndinkawalangiza mobwerezabwereza* kuti: “Muzimvera mawu anga.”+  Koma iwo sanamvere kapena kutchera khutu. Mʼmalomwake aliyense wa iwo anapitiriza kuumitsa mtima wake ndi kuchita zofuna za mtima wake woipawo.+ Choncho ndinawalanga mogwirizana ndi mawu onse a mʼpangano langa limene ndinawalamula kuti azilitsatira koma iwo anakana kulitsatira.’”  Kenako Yehova anandiuza kuti: “Anthu a mu Yuda komanso okhala mu Yerusalemu akonza chiwembu choti andipandukire. 10  Iwo abwerera ku zolakwa za makolo awo akale amene anakana kumvera mawu anga.+ Iwonso atsatira milungu ina ndipo akuitumikira.+ A mʼnyumba ya Isiraeli ndi a mʼnyumba ya Yuda aphwanya pangano langa limene ndinachita ndi makolo awo.+ 11  Choncho Yehova wanena kuti, ‘Ndiwagwetsera tsoka+ limene sadzatha kulithawa. Akadzandiitana kuti ndiwathandize, sindidzawamvetsera.+ 12  Ndiyeno mizinda ya Yuda komanso anthu okhala mu Yerusalemu adzapita kukapempha thandizo kwa milungu imene akuifukizira nsembe.+ Koma milungu imeneyo sidzawapulumutsa pa nthawi ya tsoka lawo. 13  Chifukwa milungu yako, iwe Yuda, yafanana ndi mizinda yako kuchuluka kwake. Ndipo chinthu chochititsa manyazi mwachimangira* maguwa ansembe ochuluka mofanana ndi misewu ya mu Yerusalemu, maguwa ansembe oti muziperekerapo nsembe kwa Baala.’+ 14  Koma iwe,* usawapempherere anthu awa. Usandilirire kuti ndiwathandize kapena kuwapempherera,+ chifukwa ine sindidzamvetsera pamene iwo akundiitana chifukwa cha tsoka limene lawagwera. 15  Nʼchifukwa chiyani anthu anga okondedwa akupezekabe mʼnyumba yangaPamene ambiri a iwo akuchita zinthu zoipa? Kodi nyama yopatulika* idzawapulumutsa tsoka likadzawagwera? Kodi iwo adzasangalala pa nthawi imeneyo? 16  Mʼmbuyomu Yehova ankakutchulani kuti mtengo wa maolivi wa masamba obiriwira,Wokongola komanso wobala zipatso. Koma pamveka phokoso lamphamvu ndipo mtengowo wauyatsa moto,Ndipo adani athyola nthambi zake. 17  “Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, amene anakudzalani,+ wanena kuti tsoka lidzakugwerani chifukwa cha zoipa zimene a mʼnyumba ya Isiraeli ndi a mʼnyumba ya Yuda achita. Iwo andikhumudwitsa popereka nsembe kwa Baala.”+ 18  Yehova anandiuza kuti ndidziwe,Pa nthawiyo, inu Mulungu, munandionetsa zimene ankachita. 19  Ndinali ngati mwana wa nkhosa wamphongo womvera amene akupita kukaphedwa. Sindinadziwe kuti andikonzera chiwembu nʼkunena kuti:+ “Tiyeni tiwononge mtengowu limodzi ndi zipatso zake,Ndipo tiyeni timuchotse mʼdziko la anthu amoyo,Kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.” 20  Koma Yehova wa magulu ankhondo akumwamba amaweruza mwachilungamo.Amafufuza maganizo* komanso mtima.+ Inu Mulungu, ndiloleni ndione mukuwapatsa chilango,Chifukwa mlandu wanga ndausiya mʼmanja mwanu. 21  Choncho izi ndi zimene Yehova wanena zokhudza anthu a ku Anatoti+ amene akufuna kuchotsa moyo wako, ndipo akunena kuti: “Usanenere mʼdzina la Yehova+ ngati ukufuna kuti tisakuphe.” 22  Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti: “Ine ndidzawapatsa chilango. Anyamata adzafa ndi lupanga+ ndipo ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.+ 23  Sipadzapezeka ngakhale munthu mmodzi wotsala pakati pawo chifukwa ndidzabweretsa tsoka pa anthu a ku Anatoti,+ mʼchaka chimene ndidzawapatse chilango.”

Mawu a M'munsi

Zikuoneka kuti apa amauza Yeremiya.
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ame.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndinkadzuka mʼmawa kwambiri nʼkuwalangiza.”
Kapena kuti, “Ndipo mulungu wochititsa manyazi mwamumangira.”
Apa akunena Yeremiya.
Zimenezi ndi nsembe zimene ankapereka kukachisi.
Kapena kuti, “Amafufuza mmene ndikumvera mumtima.” Mʼchilankhulo choyambirira, “impso.”