Yeremiya 15:1-21

  • Yehova sadzasintha chiweruzo chake (1-9)

  • Kudandaula kwa Yeremiya (10)

  • Zimene Yehova anayankha (11-14)

  • Pemphero la Yeremiya (15-18)

    • Ankasangalala ndi kudya mawu a Mulungu (16)

  • Yeremiya analimbikitsidwa ndi Yehova (19-21)

15  Kenako Yehova anandiuza kuti: “Ngakhale Mose ndi Samueli akanaima pamaso panga,+ anthu awa sindikanawakomera mtima. Achotse pamaso panga. Asiye apite.  Ndiyeno akakufunsa kuti, ‘Tipite kuti?’ uwayankhe kuti, ‘Yehova wanena kuti: “Amene akuyenera kufa ndi mliri afe ndi mliri! Amene akuyenera kufa ndi lupanga afe ndi lupanga!+ Amene akuyenera kufa ndi njala yaikulu afe ndi njala yaikulu! Amene akuyenera kutengedwa kupita ku ukapolo atengedwe kupita ku ukapolo!”’+  “‘Ndidzawabweretsera masoka okwanira 4,’*+ akutero Yehova. ‘Ndidzawatumizira lupanga kuti liwaphe, agalu kuti akoke mitembo yawo, mbalame zamumlengalenga komanso zilombo zakutchire kuti ziwadye ndi kuwawononga.+  Ndidzawasandutsa chinthu chochititsa mantha kwa maufumu onse apadziko lapansi,+ chifukwa cha zimene Manase mwana wa Hezekiya, mfumu ya Yuda, anachita mu Yerusalemu.+   Ndi ndani adzakusonyeze chifundo, iwe Yerusalemu?Ndi ndani adzakumvere chisoni,Ndipo ndi ndani adzapatuke kuti afunse za moyo wako?’   ‘Iwe wandisiya,’ akutero Yehova.+ ‘Ukupitiriza kubwerera nʼkundisiya.*+ Choncho ndidzakutambasulira dzanja langa nʼkukuwononga.+ Ndatopa ndi kukumvera chisoni.*   Ndidzawapeta kuti auluzike ndi mphepo pamageti amʼdzikoli. Ndidzawaphera ana awo.+ Ndidzawononga anthu anga,Chifukwa akukana kusiya kuyenda mʼnjira zawo.+   Akazi awo amasiye adzachuluka kwambiri pamaso panga kuposa mchenga wakunyanja. Ndidzawabweretsera wowononga masana, adzawononga amayi ndi anyamata. Ndidzawachititsa kuti asokonezeke komanso kugwidwa ndi mantha mwadzidzidzi.   Mkazi amene wabereka ana 7 wafooka,Ndipo akupuma movutikira. Kwa iye dzuwa lalowa masanasana,Iye wachita manyazi ndipo wathedwa nzeru.’* Ndipo anthu awo otsala omwe ndi ochepaNdidzawapereka kwa adani awo kuti awaphe ndi lupanga,’ akutero Yehova.”+ 10  Tsoka ine, chifukwa inu mayi anga munabereka ine,+Munthu amene nthawi zonse ndimakangana ndi dziko lonse komanso kulimbana nalo. Sindinakongole kanthu kapena kukongoza wina aliyense,Koma anthu onse akunditemberera. 11  Yehova anandiuza kuti: “Ndithu ndidzakuchitira zinthu zabwino.Ndithu ndidzakuthandiza pa nthawi ya tsoka,Ndidzakuthandiza pa nthawi yamavuto. 12  Kodi munthu angathe kuthyolathyola chitsulo?Kodi angathe kuthyolathyola chitsulo chakumpoto ndi kopa?* 13  Chuma chanu komanso zinthu zanu zamtengo wapatali ndidzazipereka kwa adani anu kuti azitenge.+Adzazitenga popanda malipiro chifukwa cha machimo anu onse amene munachita mʼdziko lanu lonse. 14  Ndidzazipereka kwa adani anuKuti azitenge nʼkupita nazo kudziko limene simukulidziwa.+ Chifukwa mkwiyo wanga wayatsa moto,Ndipo motowo ukukuyakirani.”+ 15  Inu Yehova mukudziwa bwino mavuto anga.Ndikumbukireni ndi kundiyangʼana. Mundibwezerere anthu amene akundizunza.+ Musalole kuti ndiwonongeke chifukwa chakuti mukuwalezera mtima. Dziwani kuti ndikunyozedwa chifukwa cha inu.+ 16  Mawu anu anandipeza ndipo ndinawadya.+Mawu anu anakondweretsa komanso kusangalatsa mtima wanga,Chifukwa ine ndimatchedwa ndi dzina lanu, inu Yehova Mulungu wa magulu ankhondo akumwamba. 17  Sindikhala pansi ndi gulu la anthu okonda zosangalatsa nʼkumasangalala nawo.+ Ndimakhala ndekha chifukwa dzanja lanu lili pa ine,Popeza mwandidzaza ndi mkwiyo.*+ 18  Nʼchifukwa chiyani ululu wanga sukutha ndiponso bala langa silikupola? Balali silikumva mankhwala. Kodi mukhala ngati chitsime chosathandizaChimene munthu sangachidalire? 19  Choncho Yehova wanena kuti: “Ukabwerera, ine ndidzakukonda,Ndipo udzapitiriza kunditumikira.* Ukasiyanitsa zinthu zamtengo wapatali ndi zinthu zopanda phindu,Udzakhala ngati pakamwa panga.* Anthuwo adzayenera kubwera kwa iwe,Koma iwe sudzapita kwa iwo.” 20  “Ndakuchititsa kuti ukhale ngati mpanda wakopa wolimba kwambiri kwa anthu awa.+ Iwo adzamenyana nawe ndithu,Koma sadzakugonjetsa,+Chifukwa ine ndili ndi iwe kuti ndikupulumutse komanso kukulanditsa,” akutero Yehova. 21  “Ndidzakulanditsa mʼmanja mwa anthu oipaNdipo ndidzakuwombola mʼmanja mwa anthu ankhanza.”

Mawu a M'munsi

Mabaibulo ena amati, “ziweruzo zamitundu 4.” Mʼchilankhulo choyambirira, “mabanja 4.”
Mabaibulo ena amati, “Ukupitiriza kuyenda chafutambuyo.”
Kapena kuti, “Ndatopa ndi kusintha maganizo.”
Mabaibulo ena amati, “Dzuwa lachita manyazi ndipo lathedwa nzeru.”
Kapena kuti, “mkuwa.”
Kapena kuti, “uthenga wachiweruzo.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndipo udzaima pamaso panga.”
Kapena kuti, “Udzakhala wondilankhulira.”