Yeremiya 16:1-21

  • Yeremiya anauzidwa kuti asakwatire, kulira kapena kusala kudya (1-9)

  • Anapatsidwa chilango kenako nʼkubwezeretsedwa mwakale (10-21)

16  Ndiyeno Yehova anandiuzanso kuti:  “Usakwatire ndipo usakhale ndi ana aamuna kapena ana aakazi mʼmalo ano.  Ponena za ana aamuna ndi ana aakazi amene adzabadwe mʼmalo ano, komanso ponena za amayi ndi abambo amene adzabereke anawo mʼdzikoli, Yehova akuti:  ‘Iwo adzafa ndi matenda oopsa+ koma palibe amene adzalire maliro awo kapena kuwaika mʼmanda. Iwo adzakhala ngati manyowa panthaka.+ Adzafa ndi lupanga ndiponso njala.+ Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamumlengalenga ndi zilombo zakutchire.’   Yehova wanena kuti,‘Usalowe mʼnyumba imene olira maliro akuchitiramo phwando,Ndipo usapite kukalira nawo maliro kapena kukapepesa.+ Chifukwa anthu awa ndawachotsera mtendere wanga,Komanso chikondi changa chokhulupirika ndi chifundo changa,’ akutero Yehova.+   ‘Anthu amʼdzikoli adzafa, kaya ndi olemekezeka kapena onyozeka. Sadzaikidwa mʼmanda,Palibe aliyense amene adzalire maliro awo,Kapena kudzichekacheka komanso kumeta mpala chifukwa cha iwo.*   Palibe amene adzapereke chakudya kwa anthu amene akulira maliro,Kuti awatonthoze chifukwa cha maliro amene awagwera,Komanso palibe amene adzawapatse kapu ya vinyo kuti awatonthozeKuti amwe chifukwa cha imfa ya bambo awo kapena mayi awo.   Ndipo usadzalowe mʼnyumba yaphwandoKuti ukhale nawo pansi nʼkumadya ndi kumwa.’  Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti, ‘Mʼmasiku anu, ndidzathetsa phokoso lachikondwerero, phokoso lachisangalalo, mawu a mkwati ndi mawu a mkwatibwi mʼmalo ano, inuyo mukuona.’+ 10  Ukadzauza anthu awa mawu onsewa, iwo adzakufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wanena kuti adzatigwetsera tsoka lalikulu limeneli? Kodi talakwa chiyani ndipo tamuchimwira chiyani Yehova Mulungu wathu?’+ 11  Udzawayankhe kuti, ‘“Chifukwa chakuti makolo anu anandisiya,”+ akutero Yehova, “ndipo anapitiriza kutsatira milungu ina, kuitumikira ndi kuigwadira.+ Koma ine anandisiya ndipo sanasunge malamulo anga.+ 12  Ndipo inu mwachita zinthu zoipa kwambiri kuposa makolo anu.+ Aliyense wa inu akupitiriza kuumitsa khosi nʼkumatsatira mtima wake woipawo mʼmalo mondimvera.+ 13  Choncho ndidzakuchotsani mʼdziko lino nʼkukupititsani kudziko limene inu kapena makolo anu sankalidziwa.+ Kumeneko mukatumikira milungu ina masana ndi usiku+ chifukwa sindidzakuchitirani chifundo.”’ 14  ‘Komabe masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene sadzalumbiranso kuti: “Pali Yehova Mulungu wamoyo amene anatulutsa Aisiraeli mʼdziko la Iguputo!”+ 15  Koma adzalumbira kuti: “Pali Yehova Mulungu wamoyo amene anatulutsa Aisiraeli mʼdziko lakumpoto komanso kuchokera mʼmayiko onse kumene anawabalalitsira!” Ineyo ndidzawabwezera kudziko lawo limene ndinapatsa makolo awo.’+ 16  ‘Ine ndikuitana asodzi ambiri,’ akutero Yehova,‘Ndipo adzawawedza. Kenako ndidzaitana anthu ambiri osaka nyama,Ndipo adzawasaka mʼphiri lililonse, pachitunda chilichonse,Komanso mʼmapanga a mʼmatanthwe. 17  Chifukwa maso anga akuona chilichonse chimene akuchita.* Anthuwo sanabisike kwa ine,Ndipo zolakwa zawo sizinabisike pamaso panga. 18  Choyamba ndidzawabwezera zolakwa zawo zonse ndi machimo awo onse,+Chifukwa aipitsa dziko langa ndi zifaniziro zopanda moyo za mafano* awo onyansaNdipo adzaza cholowa changa ndi zinthu zawo zonyansa.’”+ 19  Inu Yehova, ndinu mphamvu yanga komanso malo anga achitetezo,Malo anga othawirako pa tsiku lamavuto,+Mitundu ya anthu idzabwera kwa inu kuchokera kumalekezero a dziko lapansi,Ndipo idzati: “Makolo athu analandira mafano monga cholowa chawo,Analandira zinthu zachabechabe komanso zosapindulitsa.”+ 20  Kodi munthu angapange milungu?Zimene munthu amapangazo si milungu ayi.+ 21  “Choncho ine ndiwaphunzitsa.Pa nthawi ino ndiwachititsa kuti adziwe mphamvu ndi nyonga zanga,Ndipo adziwa kuti dzina langa ndine Yehova.”

Mawu a M'munsi

Zikuoneka kuti imeneyi inali miyambo ya maliro imene Aisiraeli opanduka ankachita.
Mʼchilankhulo choyambirira, “maso anga ali pa njira zawo zonse.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mitembo ya mafano.”