Yeremiya 22:1-30

  • Uthenga wachiweruzo wokhudza mafumu oipa (1-30)

    • Uthenga wokhudza Salumu (10-12)

    • Uthenga wokhudza Yehoyakimu (13-23)

    • Uthenga wokhudza Koniya (24-30)

22  Yehova wanena kuti: “Pita kunyumba ya mfumu ya Yuda ndipo ukanene mawu awa.  Ukanene kuti, ‘Tamverani mawu a Yehova, inu mfumu ya Yuda amene mwakhala pampando wachifumu wa Davide. Mumve mawu amenewa inuyo, atumiki anu komanso anthu anu amene amalowa pamageti awa.  Yehova wanena kuti: “Muzichita zinthu motsatira malamulo komanso mwachilungamo. Muzipulumutsa munthu amene akuberedwa mʼmanja mwa munthu wakuba mwachinyengo. Musamachitire nkhanza mlendo aliyense amene akukhala mʼdziko lanu ndipo musamavulaze mwana wamasiye kapena mkazi wamasiye.+ Musamakhetse magazi a munthu aliyense wosalakwa mumzinda uno.+  Mukamvera mawu amenewa mosamala, mafumu amene amakhala pampando wachifumu wa Davide+ adzalowa pamageti a nyumba iyi. Iwowo, atumiki awo komanso anthu awo adzalowa pamageti amenewa atakwera magaleta ndi mahatchi.”’+  ‘Koma mukapanda kumvera mawu amenewa, ndikulumbira pa dzina langa kuti nyumba iyi idzakhala bwinja,’ akutero Yehova.+  Ponena za nyumba ya mfumu ya Yuda, Yehova wanena kuti,‘Kwa ine, iwe uli ngati Giliyadi,Uli ngati nsonga ya phiri la ku Lebanoni. Koma ndidzakusandutsa chipululu,Ndipo mʼmizinda yako yonse simudzapezeka aliyense wokhalamo.+   Ndidzakutumizira anthu oti akuwononge,Aliyense adzabwera ndi zida zake.+ Iwo adzadula mitengo yako ya mkungudza yabwino kwambiriNdipo adzaigwetsera pamoto.+  Anthu ochokera mʼmitundu yambiri adzadutsa pafupi ndi mzindawu ndipo adzafunsana kuti: “Nʼchifukwa chiyani Yehova anachitira mzinda waukuluwu zinthu zimenezi?”+  Ndipo adzayankha kuti: “Chifukwa chakuti anthu amumzindawu anasiya pangano la Yehova Mulungu wawo nʼkuyamba kulambira milungu ina ndiponso kuitumikira.”’+ 10  Munthu wakufa musamulire,Ndipo musamumvere chisoni. Mʼmalomwake, mulirire kwambiri munthu amene watengedwa kupita kudziko lina,Chifukwa sadzabwereranso kudzaona dziko limene anabadwira. 11  Ponena za Salumu*+ mwana wa Yosiya, mfumu ya Yuda, amene akulamulira mʼmalo mwa bambo ake Yosiya,+ amene anachoka mʼdziko lino kupita ku ukapolo, Yehova wanena kuti: ‘Sadzabwereranso kwawo. 12  Chifukwa akafera kudziko laukapolo kumene amutengera ndipo dziko lino sadzalionanso.’+ 13  Tsoka kwa munthu amene amamanga nyumba yakeKomanso zipinda zake zamʼmwamba mopanda chilungamo.Amene amagwiritsa anthu ntchito kwaulere,Ndipo amakana kuwapatsa malipiro awo.+ 14  Amene amanena kuti, ‘Ndimanga nyumba yaikuluYokhala ndi zipinda zikuluzikulu zamʼmwamba. Ndidzaiikira mawindoNʼkuyala matabwa a mkungudza mʼmakoma ake ndipo ndidzaipaka penti wofiira.’ 15  Kodi ukuganiza kuti upitiriza kulamulira chifukwa chakuti ukugwiritsa ntchito kwambiri matabwa a mkungudzawa kuposa anthu ena? Bambo akonso ankadya komanso kumwaKoma ankachita zinthu motsatira malamulo komanso mwachilungamo,+Ndipo zinthu zinawayendera bwino. 16  Ankateteza anthu ovutika komanso osauka pa mlandu,Moti zinthu zinkayenda bwino. ‘Kodi kumeneku sindiye kundidziwa?’ akutero Yehova. 17  ‘Koma maso ako ndi mtima wako zili pa kupeza phindu mwachinyengo,Kukhetsa magazi a anthu osalakwa,Komanso kuba mwachinyengo ndi kulanda anthu zinthu zawo basi.’ 18  Choncho ponena za Yehoyakimu+ mwana wa Yosiya, mfumu ya Yuda, Yehova wanena kuti,‘Sadzamulira ngati mmene anthu amachitira kuti: “Mayo ine mchimwene wanga! Mayo ine mchemwali wanga!” Sadzamulira kuti: “Mayo ine mbuye wanga! Mayo ine a mfumu aja!” 19  Adzaikidwa mʼmanda ngati mmene amaikira bulu,+Adzamukoka kudutsa naye pamageti a YerusalemuNʼkukamutaya kunja.’+ 20  Pita ku Lebanoni ndipo ukalire,Ukalire mofuula ku BasanaNdipo ukalirenso ku Abarimu,+Chifukwa onse amene ankakukonda kwambiri agonjetsedwa.+ 21  Ndinalankhula nawe pamene unkaona kuti ndiwe wotetezeka. Koma iwe unanena kuti, ‘Sindimvera.’+ Wakhala ukuchita zimenezi kuyambira uli wachinyamata,Chifukwa wakhala usakumvera mawu anga.+ 22  Mphepo idzaweta abusa ako onse+Ndipo anthu amene akukukonda kwambiri adzatengedwa kupita ku ukapolo. Pa nthawi imeneyo udzachititsidwa manyazi ndipo udzanyozeka chifukwa cha masoka onse amene adzakugwere. 23  Inu amene mumakhala mu Lebanoni,+Amene mukukhala mʼnyumba zamitengo ya mkungudza,+Mudzabuula kwambiri mukadzayamba kumva zowawa,Mukadzayamba kumva ululu* ngati wa mkazi amene akubereka.+ 24  ‘Pali ine, Mulungu wamoyo,’ akutero Yehova, ‘ngakhale iwe Koniya*+ mwana wa Yehoyakimu,+ mfumu ya Yuda, utakhala mphete yodindira kudzanja langa lamanja, ndingakuvule! 25  Ndidzakupereka mʼmanja mwa anthu amene akufuna kuchotsa moyo wako, mʼmanja mwa anthu amene umawaopa, mʼmanja mwa Mfumu Nebukadinezara* ya ku Babulo ndiponso mʼmanja mwa Akasidi.+ 26  Iwe ndi mayi ako amene anakubereka, ndidzakuponyerani kudziko lina limene simunabadwireko ndipo mudzafera kumeneko. 27  Ndipo iwo sadzabwereranso kudziko limene akulilakalaka.+ 28  Kodi munthu uyu Koniya, wangokhala chiwiya chonyozeka komanso chophwanyika,Chiwiya chimene palibe amene akuchifuna? Nʼchifukwa chiyani iyeyu ndi ana ake agwetsedwa pansiNʼkuponyedwa mʼdziko limene sakulidziwa?’+ 29  Iwe dziko lapansi, dziko lapansi, dziko lapansi, tamvera mawu a Yehova. 30  Yehova wanena kuti: ‘Lembani kuti munthu uyu alibe ana,Munthu amene zinthu sizidzamuyendera bwino pa moyo wake.*Chifukwa palibe mwana wake aliyense, amene adzakwanitseKukhala pampando wachifumu wa Davide nʼkuyambiranso kulamulira mu Yuda.’”+

Mawu a M'munsi

Amadziwikanso ndi dzina lakuti Yehoahazi.
Mʼchilankhulo choyambirira, “zowawa za pobereka.”
Amadziwikanso ndi dzina lakuti Yehoyakini ndi Yekoniya.
Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼmasiku a moyo wake.”