Yeremiya 31:1-40

  • Aisiraeli amene anatsala adzakhalanso mʼdziko lawo (1-30)

    • Rakele akulirira ana ake (15)

  • Pangano latsopano (31-40)

31  “Pa nthawi imeneyo ndidzakhala Mulungu wa mabanja onse a Isiraeli ndipo iwo adzakhala anthu anga,” akutero Yehova.+   Yehova wanena kuti: “Anthu amene anapulumuka ku lupanga, ndinawakomera mtima mʼchipululu,Pamene Isiraeli ankapita kumalo ake opumulirako.”   Yehova anaonekera kwa ine ali kutali ndipo anati: “Ine ndakukonda ndipo ndidzakukonda mpaka kalekale. Nʼchifukwa chake ndakukokera kwa ine ndi chikondi chokhulupirika.*+   Choncho ndidzakumanganso ndipo udzakhalanso mtundu,+ Iwe namwali wa Isiraeli, udzanyamulanso maseche akoNʼkupita kukavina mosangalala.*+   Udzadzalanso mpesa kumapiri a ku Samariya.+Anthu adzadzala mpesa nʼkudya zipatso zake.+   Chifukwa tsiku lidzafika limene alonda amene ali mʼmapiri a Efuraimu adzafuula kuti: ‘Nyamukani, tiyeni tipite ku Ziyoni kwa Yehova Mulungu wathu.’”+   Yehova wanena kuti: “Fuulirani Yakobo mosangalala, Fuulani mosangalala chifukwa muli patsogolo pa mitundu ina.+ Lengezani zimenezi. Tamandani Mulungu nʼkunena kuti,‘Inu Yehova pulumutsani anthu anu, otsalira a Isiraeli.’+   Ine ndikuwabweretsa kuchokera kudziko lakumpoto,+ Ndidzawasonkhanitsa pamodzi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi.+ Pakati pawo padzakhala anthu amene ali ndi vuto losaona, olumala,+Azimayi oyembekezera komanso amene atsala pangʼono kubereka, Onse pamodzi adzabwerera kuno ali chigulu.+   Iwo adzabwera akulira.+ Ndidzawatsogolera akadzandipempha kuti ndiwakomere mtima. Ndidzawatsogolera kumitsinje ya madzi,*+Ndipo ndidzawayendetsa mʼnjira yabwino imene sadzapunthwa. Chifukwa ine ndine Bambo ake a Isiraeli ndipo Efuraimu ndi mwana wanga woyamba kubadwa.”+ 10  Inu mitundu ya anthu, imvani mawu a Yehova,Ndipo mulengeze mawuwo kuzilumba zakutali kuti:+ “Amene anabalalitsa Aisiraeli ndi amene adzawasonkhanitse. Adzawayangʼanira ngati mmene mʼbusa amachitira ndi nkhosa zake.+ 11  Chifukwa Yehova adzawombola Yakobo+Ndipo adzamupulumutsa mʼmanja mwa munthu wamphamvu kuposa iyeyo.+ 12  Iwo adzabwera nʼkufuula mosangalala pamwamba pa phiri la Ziyoni.+Nkhope zawo zidzawala chifukwa cha ubwino wa* Yehova.Chifukwa cha mbewu, vinyo watsopano+ ndi mafuta,Ndiponso chifukwa cha ana a nkhosa ndi ana a ngʼombe.+ Iwo adzakhala ngati dimba lothiriridwa bwino+Ndipo sadzakhalanso ofooka.”+ 13  “Pa nthawi imeneyo, anamwali,Anyamata ndiponso amuna achikulire, adzavina pamodzi mosangalala.+ Kulira kwawo ndidzakusandutsa chisangalalo.+ Ndidzawatonthoza ndipo ndidzachititsa kuti akhale osangalala mʼmalo mokhala achisoni.+ 14  Ansembe ndidzawapatsa chakudya chochuluka,*Ndipo anthu anga adzakhutira ndi zinthu zabwino zimene ndidzawapatse,”+ akutero Yehova. 15  “Yehova wanena kuti: ‘Mawu amveka ku Rama.+ Kwamveka kulira mofuula ndiponso komvetsa chisoni. Rakele akulirira ana ake.+ Iye wakana kutonthozedwa pamene akulirira ana ake,Chifukwa ana akewo kulibenso.’”+ 16  Yehova wanena kuti: “‘Tonthola, usalire ndipo usagwetsenso misozi,Chifukwa ulandira mphoto pa ntchito yako,’ akutero Yehova. ‘Ana ako adzabwerera kuchokera kudziko la mdani.’+ 17  ‘Uli ndi tsogolo labwino,+ Ndipo ana ako adzabwerera kudziko lawo,’ akutero Yehova.”+ 18  “Ndamva Efuraimu akulira kuti,‘Ndinali ngati mwana wa ngʼombe wosaphunzitsidwa,Mwandidzudzula ndipo ndaphunzirapo kanthu. Ndithandizeni kuti ndibwerere ndipo ndidzabwereradi,Chifukwa inu ndinu Yehova Mulungu wanga. 19  Nditabwerera kwa inu ndinadzimvera chisoni.+Mutandithandiza kuzindikira, ndinadzimenya pantchafu chifukwa cha chisoni. Ndinachita manyazi ndipo ndinaoneka wonyozeka,+Chifukwa cha zinthu zimene ndinachita ndili wachinyamata.’” 20  “Kodi Efuraimu si mwana wanga wamtengo wapatali, amene ndimamukonda?+ Ngakhale kuti nthawi zambiri ndimamudzudzula, ndimamukonda ndipo ndimamukumbukirabe. Nʼchifukwa chake ndakhudzika naye* kwambiri.+ Ndipo sindidzalephera kumumvera chisoni,” akutero Yehova.+ 21  “Udziikire zizindikiro zamumsewu,Ndipo udziikire zikwangwani.+ Maganizo ako akhale panjirayo, njira imene ukuyenera kuyendamo.+ Bwerera iwe namwali wa Isiraeli. Bwerera kumizinda yakoyi. 22  Kodi udzapita uku ndi uku mpaka liti, iwe mwana wamkazi wosakhulupirika? Chifukwa Yehova walenga chinthu chatsopano padziko lapansi. Chinthucho nʼchakuti, mkazi adzafunafuna mwakhama mwamuna wake.” 23  Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti: “Ndikadzasonkhanitsa anthu a mtundu wawo amene anagwidwa nʼkutengedwa kupita kudziko lina, iwo adzanenanso mawu awa mʼdziko la Yuda ndi mʼmizinda yake kuti, ‘Yehova akudalitse iwe malo olungama okhalamo,+ iwe phiri lopatulika.’+ 24  Anthu okhala mʼmizinda, alimi komanso abusa a ziweto azidzakhala limodzi ku Yuda.+ 25  Chifukwa ndidzapereka mphamvu kwa munthu wotopa ndipo ndidzalimbikitsa aliyense amene wafooka.”+ 26  Kenako ndinadzidzimuka nʼkutsegula maso anga. Ndinali nditagona tulo tokoma. 27  “Taonani! Masiku akubwera, pamene ndidzachititsa kuti nyumba ya Isiraeli ndi nyumba ya Yuda ikhalenso ndi anthu ochuluka komanso ziweto zambiri,” akutero Yehova.+ 28  “Ndinkawayangʼanitsitsa kuti ndiwazule, ndiwagwetse, ndiwapasule, ndiwawononge komanso kuti ndiwasakaze.+ Mofanana ndi zimenezi, ndidzawayangʼanitsitsanso kuti ndiwamange komanso ndiwadzale,”+ akutero Yehova. 29  “Masiku amenewo sadzanenanso kuti, ‘Abambo anadya mphesa zosapsa koma mano a ana awo ndi amene anayezimira.’*+ 30  Komatu munthu aliyense adzafa chifukwa cha zolakwa zake. Mano a munthu aliyense amene wadya mphesa zosapsa ndi amene adzayezimire.” 31  “Taonani! Masiku akubwera, pamene ndidzachita pangano latsopano ndi nyumba ya Isiraeli komanso nyumba ya Yuda,” akutero Yehova.+ 32  “Koma silidzakhala pangano lofanana ndi limene ndinachita ndi makolo awo, pa tsiku limene ndinagwira dzanja lawo kuti ndiwatulutse mʼdziko la Iguputo.+ ‘Pangano langa limenelo analiphwanya+ ngakhale kuti ine ndinali mbuye wawo* weniweni,’ akutero Yehova.” 33  “Pangano limene ndidzapangane ndi nyumba ya Isiraeli pambuyo pa masiku amenewo ndi ili: Ndidzaika chilamulo changa mwa iwo+ ndipo ndidzachilemba mumtima mwawo.+ Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga,” akutero Yehova.+ 34  “Munthu sadzaphunzitsanso mnzake kapena mʼbale wake kuti, ‘Mumʼdziwe Yehova!’+ chifukwa aliyense adzandidziwa kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,”+ akutero Yehova. “Ine ndidzawakhululukira zolakwa zawo ndipo machimo awo sindidzawakumbukiranso.”+ 35  Yehova amene amapereka dzuwa kuti liziwala masana,Amene amaika malamulo oti mwezi ndi nyenyezi ziziwala usiku,Amene amavundula nyanjaKuti mafunde ake achite phokoso,Amene dzina lake ndi Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, wanena kuti:+ 36  “‘Ngati malamulo amenewa angalephere kugwira ntchito yake,Ndiye kutinso mbadwa za Isiraeli zingasiye kukhala mtundu, umene umakhala pamaso panga nthawi zonse,’ akutero Yehova.”+ 37  Yehova wanena kuti: “‘Ngati kumwamba kungayezedwe ndipo ngati maziko a dziko lapansi angafufuzidwe, ndiye kuti inenso ndingakane mbadwa zonse za Isiraeli chifukwa cha zonse zimene achita,’ akutero Yehova.”+ 38  “Taonani! Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene anthu adzamangira Yehova mzinda+ kuyambira pa Nsanja ya Hananeli+ mpaka ku Geti la Pakona.+ 39  Ndipo chingwe choyezera+ chidzachokera kumeneko nʼkukafika kuphiri la Garebi, kenako chidzakhotera ku Gowa. 40  Chigwa chonse cha mitembo ndi cha phulusa,* masitepe onse mpaka kukafika kuchigwa cha Kidironi,+ mpaka kukona ya Geti la Hatchi+ chakumʼmawa, zidzakhala zoyera kwa Yehova.+ Mzindawu sudzazulidwa ndipo sudzagwetsedwanso.”

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “Nʼchifukwa chake ndapitiriza kukusonyeza chikondi chokhulupirika.”
Kapena kuti, “kukavina pamodzi ndi anthu amene akuseka.”
Kapena kuti, “kumakhwawa a madzi.”
Kapena kuti, “chifukwa cha zinthu zabwino zochokera kwa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ansembe ndidzawanenepetsa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Nʼchifukwa chake mʼmimba mwanga mwabwadamuka.”
Ena amati kuyayamira.
Mabaibulo ena amati, “mwamuna wawo.”
Kapena kuti, “phulusa lamafuta,” kutanthauza phulusa losakanikirana ndi mafuta a nsembe.