Yeremiya 32:1-44

  • Yeremiya anagula munda (1-15)

  • Pemphero la Yeremiya (16-25)

  • Zimene Yehova anayankha (26-44)

32  Awa ndi mawu amene Yehova anauza Yeremiya mʼchaka cha 10 cha ulamuliro wa Zedekiya mfumu ya Yuda. Chimenechi chinali chaka cha 18 cha Nebukadinezara.*+  Pa nthawi imeneyo, asilikali a mfumu ya Babulo anali atazungulira Yerusalemu. Ndipo mneneri Yeremiya anali atamutsekera mʼnyumba imene inali mʼBwalo la Alonda,+ limene linali pafupi ndi nyumba ya mfumu ya Yuda.  Mfumu Zedekiya ya Yuda inamutsekera+ kumeneko nʼkunena kuti: “Nʼchifukwa chiyani ukulosera zimenezi? Ukunena kuti, ‘Yehova wanena kuti: “Mzindawu ndidzaupereka mʼmanja mwa mfumu ya Babulo ndipo idzaulanda,+  ndipo Zedekiya mfumu ya Yuda sadzapulumuka mʼmanja mwa Akasidi, chifukwa adzaperekedwa ndithu mʼmanja mwa mfumu ya Babulo ndipo idzalankhulana ndi kuonana naye maso ndi maso.”’+  ‘Mfumuyo idzatenga Zedekiya kupita naye ku Babulo ndipo adzakhala komweko mpaka nditasankha zoti ndimuchite,’ akutero Yehova. ‘Ngakhale kuti mukupitiriza kumenyana ndi Akasidi simudzapambana.’”+  Ndiyeno Yeremiya anati: “Yehova wandiuza kuti,  ‘Kukubwera Hanameli mwana wa Salumu mʼbale wawo wa bambo ako, kudzakuuza kuti: “Ugule munda wanga wa ku Anatoti+ chifukwa munthu woyamba amene ali ndi ufulu wogula mundawo ndi iweyo.”’”+  Ndiyeno Hanameli mwana wa mʼbale wawo wa bambo anga anandipeza mʼBwalo la Alonda mogwirizana ndi zimene Yehova ananena. Iye anandiuza kuti: “Gula munda wanga wa ku Anatoti, umene uli mʼdziko la Benjamini, chifukwa iweyo ndi amene uli ndi ufulu wouwombola nʼkuutenga kuti ukhale cholowa chako. Uugule kuti ukhale wako.” Atatero ndinazindikira kuti mawu amenewa anali a Yehova.  Choncho ndinagula munda wa Hanameli mwana wa mʼbale wawo wa bambo anga umene unali ku Anatoti. Ndinamuyezera ndalama+ zake ndipo zinakwana masekeli* 7 ndi ndalama zina 10 zasiliva. 10  Kenako ndinalemba kalata ya pangano+ nʼkuikapo chidindo ndipo ndinaitana mboni+ kuti zidzasainire kalatayo. Ndiyeno ndinamuyezera ndalamazo pasikelo. 11  Ndiye mogwirizana ndi malamulo ndinatenga makalata onse a pangano, yomata ndi yosamata yomwe. 12  Kenako ndinapereka makalata a pangano ogulira mundawo kwa Baruki+ mwana wa Neriya,+ mwana wa Maseya. Ndinapereka makalatawo pamaso pa Hanameli mwana wa mʼbale wawo wa bambo anga, pamaso pa mboni zimene zinasaina makalatawo ndi pamaso pa Ayuda onse amene anali mʼBwalo la Alonda.+ 13  Ndiyeno ndinalamula Baruki anthu onsewo akumva kuti: 14  “Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli wanena kuti, ‘Tenga makalata awa, makalata a pangano ogulira mundawa, kalata yomata ndi kalata yosamatayo ndipo uwaike mʼmbiya kuti akhale kwa nthawi yaitali.’ 15  Chifukwa Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli wanena kuti, ‘Mʼdziko lino anthu adzagulanso nyumba, minda ndi minda ya mpesa.’”+ 16  Nditapereka makalata amenewa kwa Baruki mwana wa Neriya, ndinapemphera kwa Yehova kuti: 17  “Inu Yehova Ambuye Wamkulu Koposa. Inuyo ndi amene munapanga kumwamba ndi dziko lapansi pogwiritsa ntchito mphamvu zanu zazikulu+ ndi dzanja lanu lotambasula. Palibe chimene chingakuvuteni. 18  Inu amene mumasonyeza anthu masauzande ambiri chikondi chokhulupirika koma mumabwezera kwa ana,* zolakwa za abambo awo.+ Inu ndinu Mulungu woona, wamkulu ndi wamphamvu ndipo dzina lanu ndinu Yehova wa magulu ankhondo akumwamba. 19  Zolinga zanu ndi zazikulu ndipo zochita zanu ndi zamphamvu.+ Maso anu amaona zonse zimene anthu amachita,+ kuti munthu aliyense mumuchitire zinthu mogwirizana ndi njira zake komanso zochita zake.+ 20  Inu munachita zizindikiro ndi zodabwitsa mʼdziko la Iguputo zimene zikudziwikabe mpaka lero. Ndipo zimenezo zinachititsa kuti dzina lanu lidziwike mu Isiraeli komanso pakati pa anthu onse+ ngati mmene likudziwikira lero. 21  Inu munatulutsa anthu anu Aisiraeli mʼdziko la Iguputo pogwiritsa ntchito zizindikiro, zodabwitsa, dzanja lamphamvu, mkono wotambasula ndi zinthu zochititsa mantha kwambiri.+ 22  Patapita nthawi munawapatsa dziko lino limene munalumbira kuti mudzalipereka kwa makolo awo,+ lomwe ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi.+ 23  Iwo analowa mʼdzikoli nʼkulitenga kuti likhale lawo, koma sanamvere mawu anu kapena kuyenda motsatira malamulo anu. Iwo sanachite zinthu zonse zimene munawalamula kuti achite, nʼchifukwa chake munawagwetsera masoka onsewa.+ 24  Taonani! Anthu abwera kumzinda uno ndipo amanga malo okwera omenyerapo nkhondo kuti aulande,+ moti uperekedwa mʼmanja mwa Akasidi amene akumenyana ndi anthu amumzindawu. Anthu adzafa ndi lupanga,+ njala ndi mliri.*+ Zinthu zonse zimene munanena zachitika ndipo ndi izi mukuzionazi. 25  Koma inu Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, mwandiuza kuti, ‘Gula mundawu ndi ndalama pamaso pa mboni,’ ngakhale kuti mzindawu uperekedwa ndithu mʼmanja mwa Akasidi.” 26  Zitatero Yehova anauza Yeremiya kuti: 27  “Ine ndine Yehova, Mulungu wa anthu onse. Kodi pali chinthu chovuta kwa ine? 28  Choncho Yehova wanena kuti, ‘Tsopano ndikupereka mzindawu mʼmanja mwa Akasidi ndi mʼmanja mwa Nebukadinezara* mfumu ya Babulo, ndipo aulanda.+ 29  Akasidi amene akumenyana ndi anthu amumzindawu adzabwera nʼkuyatsa mzindawu moti udzapseratu.+ Adzawotchanso nyumba zimene pamadenga ake anthu ankaperekerapo nsembe kwa Baala komanso nsembe zachakumwa kwa milungu ina kuti andikhumudwitse.’+ 30  ‘Aisiraeli ndi Ayuda akhala akuchita zoipa zokhazokha pamaso panga kuyambira ali ana.+ Aisiraeli akhala akundikhumudwitsa ndi ntchito za manja awo,’ akutero Yehova. 31  ‘Mzinda uwu wakhala chinthu chimene chimandikwiyitsa komanso kundipsetsa mtima kungoyambira pamene unamangidwa mpaka lero.+ Choncho ukuyenera kuchotsedwa pamaso panga+ 32  chifukwa cha zoipa zonse zimene Aisiraeli ndi Ayuda achita nʼkundikhumudwitsa nazo. Achita zimenezi pamodzi ndi mafumu awo,+ akalonga awo,+ ansembe awo, aneneri awo,+ anthu a ku Yuda ndi anthu onse amene akukhala mu Yerusalemu. 33  Iwo anapitiriza kundifulatira ndipo sanandiyangʼane.+ Ngakhale kuti ndinayesetsa kuwaphunzitsa mobwerezabwereza,* palibe ngakhale mmodzi wa iwo amene anamvetsera kuti alandire malangizo.+ 34  Iwo anaika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imatchedwa ndi dzina langa kuti aiipitse.+ 35  Kuwonjezera pamenepo, anamangira Baala malo okwera mʼChigwa cha Mwana wa Hinomu*+ kuti aziwotcha* ana awo aamuna ndi ana awo aakazi pamoto ngati nsembe kwa Moleki.+ Ine sindinawalamule+ kuti azichita zimenezi. Ndipo sindinaganizirepo mumtima mwanga* zowauza kuti achite chinthu chonyansa chimenechi, chimene chachititsa kuti Yuda achimwe.’ 36  Choncho ponena za mzinda uwu umene mukunena kuti uperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya Babulo kuti uwonongedwe ndi lupanga, njala ndi mliri, Yehova Mulungu wa Isiraeli wanena kuti, 37  ‘Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi kuchokera kumayiko onse kumene ndinawabalalitsira nditakwiya, kupsa mtima ndiponso ndili ndi ukali waukulu.+ Ndidzawabwezeretsa mʼdziko lino nʼkuwachititsa kuti azikhala motetezeka.+ 38  Iwo adzakhala anthu anga ndipo ine ndidzakhala Mulungu wawo.+ 39  Ndidzawapatsa mtima umodzi+ komanso kuwachititsa kuti aziyenda mʼnjira imodzi kuti azindiopa nthawi zonse. Ndidzachita zimenezi kuti iwo limodzi ndi ana awo zinthu ziziwayendera bwino.+ 40  Ndidzachita nawo pangano+ lomwe lidzakhalapo mpaka kalekale. Panganoli lidzakhala lakuti sindidzasiya kuwachitira zinthu zabwino+ ndipo ndidzawapatsa mtima woti azindiopa kuti asachoke kwa ine.+ 41  Ndidzasangalala nawo ndipo ndidzawachitira zabwino.+ Ndidzawachititsa kuti azikhala mʼdziko lino+ mpaka kalekale. Ndidzachita zimenezi ndi mtima wanga wonse komanso moyo wanga wonse.’” 42  “Yehova wanena kuti, ‘Mofanana ndi mmene ndabweretsera anthu awa masoka aakulu onsewa, ndidzawabweretseranso zinthu zabwino zonse zimene ndikuwalonjezazi.+ 43  Anthu adzagulanso minda mʼdziko lino,+ ngakhale mukunena kuti: “Dziko ili ndi bwinja, lopanda munthu wokhalamo kapena nyama yakutchire ndipo laperekedwa kwa Akasidi.”’ 44  ‘Anthu adzagula minda ndi ndalama ndipo adzalemberana makalata a pangano pamaso pa mboni ndi kumata makalatawo. Zimenezi zidzachitika mʼdziko la Benjamini,+ mʼmadera ozungulira Yerusalemu, mʼmizinda ya Yuda,+ mʼmizinda yamʼmadera amapiri, mʼmizinda yamʼchigwa ndi mʼmizinda yakumʼmwera.+ Zidzakhala choncho chifukwa ndidzabwezeretsa anthu ake amene anatengedwa kupita kudziko lina,’+ akutero Yehova.”

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
Sekeli imodzi inali yofanana ndi magalamu 11.4. Onani Zakumapeto B14.
Mʼchilankhulo choyambirira, “mumabwezera pachifuwa cha ana.”
Kapena kuti, “matenda.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ngakhale kuti ndinkadzuka mʼmamawa nʼkumawaphunzitsa.”
Kapena kuti, “azidutsitsa.”
Kapena kuti, “Ndipo mʼmaganizo mwangamu simunabwerepo.”
Onani Matanthauzo a Mawu Ena, “Gehena.”