Yeremiya 34:1-22

  • Uthenga wachiweruzo wopita kwa Zedekiya (1-7)

  • Anaphwanya pangano loti amasule akapolo (8-22)

34  Yehova analankhula ndi Yeremiya pamene Nebukadinezara* mfumu ya Babulo, asilikali ake onse, maufumu onse apadziko lapansi amene anali pansi pa ulamuliro wake ndiponso mitundu yonse ya anthu ankamenyana ndi Yerusalemu komanso mizinda yake yonse. Iye anati:+  “Yehova Mulungu wa Isiraeli wanena kuti, ‘Pita ukauze Mfumu Zedekiya+ ya Yuda kuti: “Yehova wanena kuti, ‘Ine ndikupereka mzindawu mʼmanja mwa mfumu ya Babulo ndipo idzauwotcha ndi moto.+  Iweyo adzakugwira ndithu nʼkukupereka kwa iye ndipo sudzathawa mʼmanja mwake.+ Udzaonana ndi mfumu ya Babulo maso ndi maso ndipo idzalankhula nawe. Iweyo udzapita ku Babulo.’+  Koma iwe Zedekiya mfumu ya Yuda, imva mawu a Yehova akuti, ‘Ponena za iwe, Yehova wanena kuti: “Sudzafa ndi lupanga.  Udzafa mu mtendere.+ Anthu adzakuchitira mwambo wowotcha zinthu zonunkhira ngati mmene anachitira ndi makolo ako, mafumu amene analipo iwe usanabadwe. Polira maliro ako adzanena kuti, ‘Mayo ine mbuyanga!’ chifukwa ‘Ine ndalankhula mawu amenewa,’ akutero Yehova.”’”’”  Kenako mneneri Yeremiya anauza Mfumu Zedekiya ya Yuda mawu onsewa ku Yerusalemu,  pamene asilikali a mfumu ya Babulo ankamenyana ndi Yerusalemu komanso mizinda yonse ya mu Yuda imene inatsala,+ kuphatikizapo Lakisi+ ndi Azeka.+ Imeneyi ndi mizinda yokhayo ya mipanda yolimba kwambiri imene inatsala mu Yuda.  Yehova analankhula ndi Yeremiya pambuyo poti Mfumu Zedekiya yachita pangano ndi anthu onse a mu Yerusalemu kuti alengeze ufulu,+  kuti aliyense amasule akapolo ake a Chiheberi, aamuna ndi aakazi, kuti pasapezeke munthu amene akusunga Myuda mnzake ngati kapolo wake. 10  Choncho akalonga onse ndi anthu onse anamvera. Iwo anachita pangano kuti aliyense amasule akapolo ake aamuna ndi aakazi kuti asakhalenso akapolo. Iwo anamvera nʼkuwalola kuti achoke. 11  Koma patapita nthawi, iwo anakatenganso akapolo aamuna ndi aakazi amene anawamasula aja ndipo anawakakamiza kuti akhalenso akapolo awo. 12  Choncho Yehova anauza Yeremiya mawu ndipo Yehova anati: 13  “Yehova Mulungu wa Isiraeli wanena kuti, ‘Ine ndinachita pangano ndi makolo anu+ pa tsiku limene ndinawatulutsa mʼdziko la Iguputo, kumene anali akapolo.+ Ndinapangana nawo kuti: 14  “Kumapeto kwa zaka 7, aliyense wa inu azimasula mʼbale wake yemwe ndi Mheberi amene anagulitsidwa kwa inu ndipo wakutumikirani kwa zaka 6. Muzimulola kuti achoke.”+ Koma makolo anu sanandimvere ndipo sanatchere khutu lawo. 15  Ndipo inuyo posachedwapa* munasintha nʼkuchita zabwino pamaso panga polengeza ufulu kwa abale anu. Munachita pangano pamaso panga, mʼnyumba imene imatchulidwa ndi dzina langa. 16  Koma kenako munasinthanso nʼkuipitsa dzina langa+ potenganso akapolo anu aamuna ndi aakazi amene munawalola kuti achoke nʼkupita kulikonse kumene anafuna. Inu munawakakamiza kuti akhalenso akapolo anu.’ 17  Choncho Yehova wanena kuti, ‘Inu simunamvere mawu anga oti mulengeze ufulu, aliyense kwa mʼbale wake ndi kwa mnzake.+ Tsopano ine ndikulengeza ufulu kwa inu,’ akutero Yehova. ‘Inu mudzafa ndi lupanga, mliri* ndi njala.+ Ndidzakusandutsani chinthu chimene maufumu onse apadziko lapansi adzachita nacho mantha.+ 18  Ndipo izi ndi zimene zidzachitikire anthu amene anaphwanya pangano langa posatsatira mawu a mʼpangano limene iwo anachita pamaso panga. Iwo anachita pangano limeneli podula mwana wa ngʼombe pakati nʼkudutsa pakati pa mbali ziwirizo.+ 19  Anthuwa ndi akalonga a Yuda, akalonga a Yerusalemu, nduna zapanyumba ya mfumu, ansembe ndi anthu onse amʼdzikoli amene anadutsa pakati pa mwana wa ngʼombe yemwe anamudula pakati. 20  Ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo ndi mʼmanja mwa onse amene akufuna moyo wawo. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zouluka mumlengalenga ndi zilombo zakutchire.+ 21  Ndipo Mfumu Zedekiya ya Yuda ndi akalonga ake ndidzawapereka mʼmanja mwa adani awo, mʼmanja mwa anthu amene akufuna moyo wawo ndiponso mʼmanja mwa asilikali a mfumu ya ku Babulo+ amene akubwerera osamenyana nanu.’+ 22  Yehova wanena kuti, ‘Ndidzapereka lamulo ndipo ndidzachititsa kuti adaniwo abwererenso mumzinda uno. Iwo adzamenyana ndi mzindawu ndipo adzaulanda nʼkuuwotcha ndi moto.+ Mizinda ya Yuda ndidzaisandutsa bwinja ndipo simudzapezeka wokhalamo.’”+

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
Mʼchilankhulo choyambirira, “lero.”
Kapena kuti, “matenda.”