Yeremiya 35:1-19

  • Arekabu anasonyeza chitsanzo chabwino pa nkhani yomvera (1-19)

35  Mʼmasiku a Yehoyakimu+ mwana wa Yosiya, mfumu ya Yuda, Yehova anauza Yeremiya kuti:  “Pita kunyumba ya Arekabu,+ ukalankhule nawo ndipo ukabwere nawo kunyumba ya Yehova. Ukalowe nawo mʼchimodzi mwa zipinda zodyera ndipo ukawapatse vinyo kuti amwe.”  Choncho ndinatenga Yaazaniya, mwana wa Yeremiya mwana wa Habaziniya, azibale ake, ana ake onse aamuna ndi banja lonse la Arekabu  nʼkuwabweretsa mʼnyumba ya Yehova. Ndinalowa nawo mʼchipinda chodyera cha ana a Hanani mwana wa Igadaliya, munthu wa Mulungu woona. Chipinda chimenechi chinali pafupi ndi chipinda chodyera cha akalonga chimene chinali pamwamba pa chipinda chodyera cha Maaseya mwana wa Salumu, amene anali mlonda wapakhomo.  Kenako ndinaika makapu ndi zipanda zodzaza ndi vinyo pamaso pa Arekabu nʼkuwauza kuti: “Imwani vinyoyu.”  Koma iwo anati: “Sitingamwe vinyo, chifukwa Yehonadabu*+ mwana wa Rekabu, kholo lathu, anatilamula kuti, ‘Inuyo kapena ana anu musamamwe vinyo mpaka kalekale.  Musamamange nyumba, musamafese mbewu komanso musamadzale kapena kukhala ndi minda ya mpesa. Koma nthawi zonse muzikhala mʼmatenti kuti mukhale ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukhala ngati alendo.’  Choncho ife tikupitiriza kumvera mawu a Yehonadabu mwana wa Rekabu kholo lathu, pa chilichonse chimene anatilamula. Timachita zimenezi popewa kumwa vinyo aliyense, ifeyo, akazi athu, ana athu aamuna ndi ana athu aakazi.  Sitimanga nyumba kuti tizikhalamo ndipo tilibe minda ya mpesa. Sitilima minda kapena kudzala mbewu. 10  Tikupitiriza kukhala mʼmatenti ndipo timamvera zonse zimene Yehonadabu* kholo lathu anatilamula. 11  Koma pamene Mfumu Nebukadinezara* ya Babulo inabwera kudzaukira dzikoli+ tinati, ‘Tiyeni tipite ku Yerusalemu kuti tithawe asilikali a Akasidi ndi asilikali a ku Siriya,’ ndipo pano tikukhala ku Yerusalemu.” 12  Yehova analankhula ndi Yeremiya kuti: 13  “Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti, ‘Pita ukauze anthu a ku Yuda komanso anthu amene akukhala mu Yerusalemu kuti: “Kodi inu simunkalimbikitsidwa nthawi zonse kuti muzimvera mawu anga?”+ akutero Yehova. 14  “Yehonadabu mwana wa Rekabu analamula ana ake kuti asamamwe vinyo ndipo iwo akhala akutsatira mawu ake moti samwa vinyo mpaka lero pomvera lamulo la kholo lawo.+ Koma ine ndakhala ndikulankhula nanu mobwerezabwereza,* koma simunandimvere.+ 15  Ndinkakutumizirani mobwerezabwereza*+ atumiki anga onse omwe anali aneneri. Ndinkawauza uthenga wakuti, ‘Chonde bwererani ndipo aliyense asiye njira zake zoipa.+ Muzichita zinthu zabwino. Musatsatire milungu ina nʼkumaitumikira. Mukatero mudzapitiriza kukhala mʼdziko limene ndinapatsa inuyo ndi makolo anu.’+ Koma inu simunatchere khutu kapena kundimvera. 16  Ana a Yehonadabu mwana wa Rekabu akhala akutsatira lamulo limene kholo lawo linawapatsa,+ koma anthu awa sanandimvere.”’” 17  “Choncho Yehova, Mulungu wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti, ‘Tsopano Yuda ndi anthu onse amene akukhala mu Yerusalemu ndiwagwetsera masoka onse amene ndinawachenjeza kuti ndidzawagwetsera.+ Ndichita zimenezi chifukwa ndakhala ndikulankhula nawo koma sanandimvere. Ndinkawaitana koma sanandiyankhe.’”+ 18  Ndiyeno Yeremiya anauza anthu a mʼnyumba ya Rekabu kuti: “Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli wanena kuti, ‘Chifukwa chakuti mwamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu ndipo mukupitiriza kusunga malamulo ake onse komanso kuchita zonse zimene anakulamulani, 19  Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli wanena kuti: “Sipadzalephera kukhala munthu wa mʼbanja la Yehonadabu* mwana wa Rekabu woti azitumikira pamaso panga nthawi zonse.”’”

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “Yonadabu,” chidule cha dzina lakuti Yehonadabu.
Mʼchilankhulo choyambirira, “Yonadabu,” chidule cha dzina lakuti Yehonadabu.
Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
Mʼchilankhulo choyambirira, “ndakhala ndikudzuka mʼmamawa nʼkumalankhula nanu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndinkadzuka mʼmamawa nʼkuwatumiza.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Yonadabu,” chidule cha dzina lakuti Yehonadabu.