Yeremiya 37:1-21

  • Akasidi anabwerera kwa kanthawi kochepa (1-10)

  • Yeremiya anaikidwa mʼndende (11-16)

  • Zedekiya anakumana ndi Yeremiya (17-21)

    • Yeremiya ankapatsidwa mkate (21)

37  Ndiyeno Mfumu Zedekiya+ mwana wa Yosiya inayamba kulamulira mʼmalo mwa Koniya+ mwana wa Yehoyakimu chifukwa Mfumu Nebukadinezara* ya Babulo inamuika kuti akhale mfumu mʼdziko la Yuda.+  Koma Zedekiyayo, atumiki ake ndi anthu amʼdzikolo sanamvere mawu amene Yehova ananena kudzera mwa mneneri Yeremiya.  Ndiyeno Mfumu Zedekiya inatuma Yehukali+ mwana wa Selemiya ndi Zefaniya+ mwana wa Maaseya wansembe kwa mneneri Yeremiya kukamuuza kuti: “Chonde, tipempherere kwa Yehova Mulungu wathu.”  Yeremiya ankakhala mwaufulu pakati pa anthuwo chifukwa anali asanamutsekere mʼndende.+  Ndiyeno asilikali a Farao anabwera kuchokera ku Iguputo+ ndipo Akasidi amene anali atazungulira mzinda wa Yerusalemu atamva zimenezi anachoka ku Yerusalemu.+  Kenako Yehova anauza mneneri Yeremiya kuti:  “Yehova Mulungu wa Isiraeli wanena kuti, ‘Mfumu ya Yuda imene yakutumani kudzafunsira kwa ine mukaiuze kuti: “Taonani! Asilikali a Farao amene akubwera kudzakuthandizani adzabwerera kwawo ku Iguputo.+  Ndipo Akasidi adzabweranso kudzamenyana ndi mzinda uno, adzaulanda nʼkuuwotcha ndi moto.”+  Yehova wanena kuti: “Musadzipusitse ponena kuti, ‘Akasidi samenyana nafe, ndithu abwerera,’ chifukwa sachoka ayi. 10  Ngakhale mutapha pafupifupi asilikali onse a Akasidi amene akumenyana nanu nʼkungotsala ovulala kwambiri okha, iwo angadzukebe mʼmatenti awo nʼkuwotcha mzindawu ndi moto.”’”+ 11  Asilikali a Akasidi atabwerera kuchoka ku Yerusalemu chifukwa cha asilikali a Farao,+ 12  Yeremiya ananyamuka kuchoka ku Yerusalemu kupita kudziko la Benjamini+ kuti akalandire cholowa chake pakati pa anthu ake. 13  Koma mneneri Yeremiya atafika pa Geti la Benjamini, mkulu wa alonda amene dzina lake linali Iriya mwana wa Selemiya, mwana wa Hananiya, anamugwira nʼkunena kuti: “Ukuthawira kwa Akasidi iwe!” 14  Yeremiya anamuyankha kuti: “Zabodza zimenezo! Ine sindikuthawira kwa Akasidi.” Koma Iriya sanamumvere. Choncho Iriya anagwira Yeremiya nʼkumupititsa kwa akalonga. 15  Akalongawo anakwiyira kwambiri Yeremiya+ ndipo anamumenya nʼkumutsekera*+ mʼnyumba ya Yehonatani mlembi, imene anaisandutsa ndende. 16  Yeremiya anamuika mʼndende yapansi,* muselo ndipo anakhala mmenemo kwa masiku ambiri. 17  Kenako Mfumu Zedekiya inatuma anthu kuti akatenge Yeremiya.+ Atabwera naye, mfumuyo inamufunsa mafunso mwachinsinsi mʼnyumba mwake. Mfumuyo inamufunsa kuti: “Kodi pali mawu aliwonse ochokera kwa Yehova?” Yeremiya anayankha kuti: “Eya alipo!” Ndipo anapitiriza kuti: “Inuyo mudzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya Babulo!”+ 18  Yeremiya anafunsanso Mfumu Zedekiya kuti: “Kodi ineyo ndakulakwirani chiyani pamodzi ndi atumiki anu ndiponso anthuwa, kuti munditsekere mʼndende? 19  Tsopano ali kuti aneneri anu amene ankalosera kwa inu kuti, ‘Mfumu ya Babulo sidzabwera kudzamenyana ndi inu ndiponso dzikoliʼ?+ 20  Ndiye ndimvereni chonde, mbuyanga mfumu. Chonde, imvani pempho langa lakuti mundikomere mtima. Musandibwezere kunyumba ya Yehonatani+ mlembi, chifukwa ndingakafere kumeneko.”+ 21  Choncho Mfumu Zedekiya inalamula kuti Yeremiya atsekeredwe mʼBwalo la Alonda+ ndipo tsiku lililonse ankamupatsa mtanda wozungulira wa mkate.+ Mkate umenewu unkachokera kumsewu wa ophika mkate ndipo anapitiriza kumʼpatsa mkatewo mpaka mkate wonse utatha mumzindamo.+ Choncho Yeremiya anapitiriza kukhala mʼBwalo la Alonda.

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
Mʼchilankhulo choyambirira, “anamuika mʼnyumba yamatangadza.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “anamuika mʼnyumba yachitsime.”