Yeremiya 49:1-39

  • Ulosi wokhudza Aamoni (1-6)

  • Ulosi wokhudza Edomu (7-22)

    • Mtundu wa Edomu sudzakhalaponso (17, 18)

  • Ulosi wokhudza Damasiko (23-27)

  • Ulosi wokhudza Kedara ndi Hazori (28-33)

  • Ulosi wokhudza Elamu (34-39)

49  Ponena za Aamoni+ Yehova wanena kuti: “Kodi Isiraeli alibe ana aamuna? Kodi alibe wolandira cholowa? Nʼchifukwa chiyani Malikamu+ watenga Gadi+ kuti akhale cholowa chake? Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Isiraeli?”   “‘Choncho taonani! Masiku akubwera,’ akutero Yehova,‘Amene ndidzachititsa kuti ku Raba,+ umene ndi mzinda wa Aamoni,+ kumveke chizindikiro chakuti kukubwera nkhondo.* Mzindawu udzasanduka bwinja ndi mulu wadothi.Midzi yake yozungulira idzawotchedwa ndi moto.’ ‘Ndipo Isiraeli adzatenga dziko la anthu amene analanda dziko lake,’+ akutero Yehova.   ‘Fuula iwe Hesiboni chifukwa mzinda wa Ai wawonongedwa! Lirani inu midzi yozungulira Raba. Valani ziguduli. Lirani mokuwa nʼkumayendayenda mʼmakola amiyala,*Chifukwa Malikamu adzatengedwa kupita kudziko lina,Limodzi ndi ansembe komanso akalonga ake.+   Bwanji ukudzitama chifukwa cha zigwa zako,Zigwa zoyenda madzi, iwe mwana wamkazi wosakhulupirika,Amene ukudalira chuma chakoNʼkumanena kuti: “Ndi ndani angabwere kudzandiukira?”’”   “Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Ambuye Wamkulu Koposa wanena kuti, ‘Ine ndikukubweretserani chinthu chochititsa mantha,Kuchokera kwa anthu onse amene akuzungulirani. Mudzabalalitsidwa kulowera mbali zonse,Ndipo palibe amene adzasonkhanitse anthu amene athawa.’”   “‘Koma pambuyo pake ndidzasonkhanitsa Aamoni amene anatengedwa kupita kudziko lina,’ akutero Yehova.”  Ponena za Edomu, Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti: “Kodi nzeru zinatha ku Temani?+ Kodi anthu ozindikira sakuperekanso malangizo anzeru? Kodi nzeru zawo zinawola?   Thawani! Bwererani! Pitani kumalo otsika kuti mukakhale kumeneko, inu amene mukukhala ku Dedani!+ Chifukwa Esau ndidzamugwetsera tsokaNthawi yoti ndimupatse chilango ikadzafika.   Kodi okolola mphesa atabwera kwa iwe,Sangasiye zina kuti anthu akunkhe? Ngati akuba atabwera usiku,Angawononge zokhazo zimene akufuna.+ 10  Koma ine ndidzawononga zinthu zonse za Esau nʼkumusiya alibe chilichonse. Ndidzavundukula malo ake amene amabisalako,Moti sadzathanso kubisala. Ana ake, abale ake ndi anthu oyandikana naye, onse adzawonongedwa,+Ndipo Esau sadzakhalaponso.+ 11  Ana anu amasiye asiyeni mʼmanja mwanga,Ndipo ine ndidzawasiya amoyo,Akazi anu amasiye adzandikhulupirira.” 12  Yehova wanena kuti: “Taonani! Ngati amene sanapatsidwe chiweruzo kuti amwe zamʼkapu akuyenera kumwa, kodi iweyo ukuyenera kusiyidwa osapatsidwa chilango? Ayi, sudzasiyidwa osapatsidwa chilango chifukwa ukuyenera kumwa zamʼkapumo.”+ 13  “Chifukwa ine ndalumbira pa dzina langa kuti Bozira adzakhala chinthu chochititsa mantha,+ adzanyozedwa, adzawonongedwa ndi kutembereredwa ndipo mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka kalekale,” akutero Yehova.+ 14  Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova,Nthumwi yatumidwa kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti: “Sonkhanani pamodzi nʼkubwera kudzamuukira,Konzekerani kumenya nkhondo.”+ 15  “Taona! Ndakuchititsa kukhala wosafunika pakati pa mitundu ina,Ndakuchititsa kukhala wonyozeka pakati pa anthu.+ 16  Iwe unachititsa kuti anthu azinjenjemera ndipo zimenezi zakupusitsa,Mtima wako wodzikuza wakupusitsa,Iwe amene ukukhala mʼmalo obisika amʼthanthwe,Amene ukukhala paphiri lalitali kwambiri. Ngakhale kuti unamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga,Ine ndidzakugwetsa kuchoka pamenepo,” akutero Yehova. 17  “Edomu adzakhala chinthu chochititsa mantha.+ Aliyense wodutsa pafupi naye adzamuyangʼanitsitsa mwamantha nʼkumuimbira mluzu chifukwa cha miliri yonse imene idzamugwere. 18  Mofanana ndi mmene Sodomu ndi Gomora komanso midzi imene anali nayo pafupi inawonongedwera, ndi mmenenso zidzakhalire ndi Edomu.+ Palibe aliyense amene adzakhalenso mʼdzikolo,” akutero Yehova.+ 19  “Taona! Wina adzabwera ngati mkango+ kuchokera munkhalango zowirira zamʼmphepete mwa Yorodano. Adzabwera kudzaukira malo otetezeka odyetserako ziweto, koma mʼkanthawi kochepa ndidzamuthamangitsa pamalowo. Ndidzaika pamalopo mtsogoleri amene ndamusankha. Chifukwa ndi ndani amene angafanane ndi ine ndipo ndi ndani angatsutsane nane? Kodi pali mʼbusa amene angakane kuchita zimene ine ndikufuna?+ 20  Tsopano amuna inu, tamverani zimene Yehova wasankha* kuchitira Edomu ndiponso zimene waganiza kuti achitire anthu amene akukhala ku Temani:+ Ndithudi, chilombo chidzakokera kutali ana a nkhosa. Adzachititsa kuti malo awo okhala asanduke bwinja chifukwa cha zimene anthuwo anachita.+ 21  Dziko lapansi lagwedezeka chifukwa cha mkokomo wa kugwa kwawo. Kukumveka kulira! Kulirako kwamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.+ 22  Taonani! Mofanana ndi chiwombankhanga mdani adzatsika nʼkugwira chakudya chake,+Ndipo adzatambasula mapiko ake pa Bozira.+ Pa tsiku limenelo mtima wa asilikali a ku EdomuUdzakhala ngati mtima wa mkazi amene akubereka.” 23  Uthenga wokhudza Damasiko ndi wakuti:+ “Hamati+ ndi Aripadi achititsidwa manyaziChifukwa chakuti amva uthenga woipa. Iwo agwidwa ndi mantha aakulu. Nyanja yachita mafunde ndipo singathe kukhala bata. 24  Damasiko sanathenso kulimba mtima. Watembenuka kuti athawe koma wagwidwa ndi mantha aakulu. Iye wagwidwa ndi nkhawa ndiponso zowawa,Ngati mkazi amene akubereka. 25  Kodi zatheka bwanji kuti anthu asachoke mumzinda wotamandika,Mudzi wobweretsa chisangalalo? 26  Chifukwa anyamata ake adzaphedwa mʼmabwalo ake,Ndipo asilikali onse adzaphedwa tsiku limenelo,” akutero Yehova wa magulu ankhondo akumwamba. 27  “Mpanda wa Damasiko ndidzauyatsa moto,Ndipo motowo udzawotcha nsanja zokhala ndi mipanda yolimba za Beni-hadadi.”+ 28  Ponena za Kedara+ ndi maufumu a ku Hazori amene Mfumu Nebukadinezara* ya Babulo inawagonjetsa, Yehova wanena kuti: “Nyamukani, pitani ku Kedara,Ndipo mukawononge ana a Kumʼmawa. 29  Matenti awo, nkhosa zawo, nsalu za matenti awoNdi katundu wawo yense zidzatengedwa. Ngamila zawo zidzalandidwa,Ndipo anthu adzawalirira kuti, ‘Zochititsa mantha zili paliponse!’” 30  “Thawani, pitani kutali. Pitani ndipo mukakhale mʼmalo otsika, inu anthu amene mukukhala ku Hazori,” akutero Yehova. “Chifukwa Nebukadinezara* mfumu ya Babulo wakonza njira yoti akuukireni,Ndipo wakonza pulani kuti akugonjetseni.” 31  “Nyamukani, pitani mukaukire mtundu wa anthu umene ukukhala mwamtendere,Umene ukukhala popanda chosokoneza!” akutero Yehova. “Kumeneko kulibe zitseko ndi mipiringidzo. Anthu ake amakhala kwaokhaokha. 32  Ngamila zawo zidzalandidwa,Ndipo ziweto zawo zochulukazo zidzatengedwa ndi adani. Anthu amene amadulira ndevu zawo zamʼmbali,Ndidzawabalalitsira kumbali zonse,*+Ndipo ndizawagwetsera tsoka kuchokera kumadera onse,” akutero Yehova. 33  “Hazori adzakhala malo obisalamo mimbulu,Adzakhala bwinja mpaka kalekale. Palibe munthu amene adzakhale kumeneko,Ndipo palibe aliyense amene adzakhazikike kumeneko.” 34  Yehova anauza Yeremiya mawu okhudza Elamu+ kumayambiriro kwa ulamuliro wa Mfumu Zedekiya+ ya Yuda kuti: 35  “Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti, ‘Ine ndikuthyola uta wa Aelamu,+ umene umachititsa kuti akhale amphamvu.* 36  Anthu a ku Elamu ndidzawabweretsera mphepo 4 kuchokera kumalekezero 4 akumwamba, ndipo ndidzawabalalitsira kumphepo zonsezi. Sipadzapezeka mtundu wa anthu kumene anthu a ku Elamu amene abalalitsidwa sadzapitako.’” 37  “Aelamu ndidzawachititsa mantha pamaso pa adani awo ndi pamaso pa anthu amene akufunafuna moyo wawo. Ndidzawabweretsera tsoka, mkwiyo wanga woyaka moto,” akutero Yehova. “Ndidzawatumizira lupanga mpaka nditawawononga onse.” 38  “Ndidzaika mpando wanga wachifumu ku Elamu+ ndipo kumeneko ndidzawononga mfumu ndi akalonga ake,” akutero Yehova. 39  “Ndiyeno mʼmasiku otsiriza ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu a ku Elamu amene anatengedwa kupita kudziko lina,” akutero Yehova.

Mawu a M'munsi

Mabaibulo ena amati, “kumveke mfuwu ya nkhondo.”
Kapena kuti, “mʼmakola a nkhosa.”
Kapena kuti, “akufuna.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
Mʼchilankhulo choyambirira, “kumphepo zonse.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “umene ndi chiyambi cha mphamvu zawo.”