Yeremiya 51:1-64

  • Ulosi wokhudza Babulo (1-64)

    • Babulo adzawonongedwa mwadzidzidzi ndi Amedi (8-12)

    • Buku linaponyedwa mumtsinje wa Firate (59-64)

51  Yehova wanena kuti: “Babulo+ komanso anthu amene akukhala ku Lebi-kamai*Ndikuwabweretsera chimphepo chowononga.   Ine ndidzatumiza anthu opeta ku Babulo,Ndipo adzamupeta nʼkusiya dziko lake lili lopanda kanthu.Pa tsiku la tsoka lake, anthuwo adzamuukira kuchokera kumbali zonse.+   Munthu wodziwa kuponya mivi musamulole kukunga uta wake. Musalole kuti aliyense aimirire atavala chovala chamamba achitsulo. Anyamata ake musawamvere chisoni.+ Wonongani gulu lake lonse la asilikali.   Iwo adzaphedwa mʼdziko la Akasidi,Adzabayidwa mʼmisewu ya ku Babulo.+   Chifukwa Mulungu, Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, sanasiye Isiraeli ndi Yuda kuti akhale akazi amasiye.+ Koma dziko la Akasidi lili ndi mlandu waukulu pamaso pa Woyera wa Isiraeli.   Tulukani mʼBabulo nʼkuthawa,Ndipo pulumutsani moyo wanu.+ Musawonongeke chifukwa cha zolakwa zake. Ino ndi nthawi yoti Yehova amubwezere. Mulungu akubwezera Babulo chifukwa cha zimene anachita.+   Babulo anali ngati kapu yagolide mʼdzanja la Yehova.Anachititsa kuti dziko lonse lapansi liledzere. Mitundu ya anthu yaledzera ndi vinyo wake.+Nʼchifukwa chake mitundu ya anthu ikuchita zinthu ngati anthu amisala.+   Babulo wagwa mwadzidzidzi ndipo wasweka.+ Mulirireni mofuula.+ Mʼpatseni mafuta a basamu kuti ululu wake uthe, mwina angachire.”   “Tinayesetsa kuti tichiritse Babulo koma sanachiritsike. Musiyeni, tiyeni tizipita. Aliyense apite kudziko lakwawo.+ Chifukwa zolakwa zake zafika kumwamba,Zafika pamwamba kwambiri ngati mitambo.+ 10  Yehova watichitira zinthu zachilungamo.+ Bwerani, tiyeni tinene mu Ziyoni ntchito za Yehova Mulungu wathu.”+ 11  “Nolani mivi yanu.*+ Tengani zishango zozungulira. Yehova walimbikitsa* mafumu a Amedi kuti akamenye nkhondo,+Chifukwa akufuna kuwononga Babulo. Yehova akubwezera Babulo, akumubwezera chifukwa cha kachisi wake. 12  Kwezani chizindikiro+ kuti muukire mpanda wa Babulo. Wonjezerani alonda ndipo ikani alondawo pamalo awo. Uzani omenya nkhondo mobisalira anzawo kuti akonzeke. Chifukwa Yehova waganiza zoti achite,Ndipo adzachitira anthu amene akukhala ku Babulo zimene ananena.”+ 13  “Iwe mkazi amene ukukhala pamadzi ambiri,+Amene uli ndi chuma chambiri,+Mapeto ako afika ndipo nthawi yako yopanga phindu yatha.+ 14  Yehova wa magulu ankhondo akumwamba walumbira mʼdzina lake kuti,‘Mʼdziko lako ndidzadzazamo amuna ochuluka ngati dzombe,Ndipo amunawo adzafuula mosangalala chifukwa chakuti akugonjetsa.’+ 15  Iye ndi Mulungu amene anapanga dziko lapansi pogwiritsa ntchito mphamvu zake,Amene anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru zake+Amenenso anatambasula kumwamba chifukwa cha kuzindikira kwake.+ 16  Mawu ake akamveka,Madzi akumwamba amachita mkokomo,Ndipo amachititsa mitambo* kukwera kuchokera kumalekezero a dziko lapansi. Iye amachititsa kuti kukamagwa mvula mphezi zizingʼanimaNdipo amatulutsa mphepo mʼnyumba zake zosungira.+ 17  Munthu aliyense akuchita zinthu mopanda nzeru komanso mosazindikira. Mmisiri wa zitsulo aliyense adzachita manyazi chifukwa cha chifaniziro chake chosula.+Chifukwa chifaniziro chake chopangidwa ndi chitsulo chosungunula ndi mulungu wonamaNdipo mafano amenewa alibe mzimu.*+ 18  Iwo ndi achabechabe,+ oyenera kunyozedwa. Tsiku loti aweruzidwe likadzafika adzawonongedwa. 19  Koma Mulungu, amene ndi cholowa cha Yakobo, sali ngati mafano amenewa,Chifukwa iye ndi amene anapanga chilichonse,Ngakhalenso ndodo ya cholowa chake.+ Dzina lake ndi Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.”+ 20  “Iwe ndiwe chibonga changa, chida changa chomenyera nkhondo,Ndipo ndidzakugwiritsa ntchito pophwanya mitundu ya anthu. Ndidzakugwiritsa ntchito powononga maufumu. 21  Ndidzakugwiritsa ntchito pophwanya hatchi ndi wokwerapo wake. Ndidzakugwiritsa ntchito pophwanya magaleta ankhondo ndi okweramo ake. 22  Ndidzakugwiritsa ntchito pophwanya mwamuna ndi mkazi. Ndidzakugwiritsa ntchito pophwanya mwamuna wachikulire ndi kamnyamata. Ndidzakugwiritsa ntchito pophwanya mnyamata ndi mtsikana. 23  Ndidzakugwiritsa ntchito pophwanya mʼbusa ndi ziweto zake. Ndidzakugwiritsa ntchito pophwanya mlimi ndi ziweto zimene amazigwiritsa ntchito polima. Ndidzakugwiritsa ntchito pophwanya abwanamkubwa ndi achiwiri kwa olamulira. 24  Ndidzabwezera Babulo ndi anthu onse amene akukhala mʼdziko la KasidiChifukwa cha zoipa zonse zimene anachita ku Ziyoni inu mukuona,”+ akutero Yehova. 25  “Ine ndidzachita nawe nkhondo,+ iwe phiri lowonongaAmene wawononga dziko lonse lapansi,” akutero Yehova.+ “Ndidzatambasula dzanja langa nʼkukupatsa chilango moti ndidzakugubuduza kuchokera pamatanthweNdipo ndidzakusandutsa phiri limene lawotchedwa ndi moto.” 26  “Anthu sadzatenga kwa iwe mwala wapakona kapena mwala wapamaziko,Chifukwa udzakhala bwinja mpaka kalekale,”+ akutero Yehova. 27  “Kwezani chizindikiro mʼdzikoli.+ Imbani lipenga pakati pa mitundu ya anthu. Sankhani* mitundu ya anthu kuti ichite naye nkhondo. Muitanireni maufumu a ku Ararati,+ ku Mini ndi ku Asikenazi+ kuti adzamuukire. Muikireni wolemba anthu usilikali. Mubweretsereni mahatchi ambiri ngati dzombe lingʼonolingʼono. 28  Sankhani* mitundu ya anthu kuti ichite naye nkhondo.Sankhani mafumu a ku Mediya,+ abwanamkubwa ake ndi achiwiri kwa olamulira awo onseKomanso mayiko onse amene iwo amawalamulira. 29  Dziko lidzagwedezeka ndi kunjenjemera,Chifukwa Yehova adzachitira Babulo zimene akuganizaKuti dziko la Babulo likhale chinthu chochititsa mantha, lopanda munthu wokhalamo.+ 30  Asilikali a ku Babulo asiya kumenya nkhondo. Iwo akhala pansi mʼmalo awo otetezeka. Mphamvu zawo zatha.+ Akhala ngati akazi.+ Nyumba za mʼBabulo zawotchedwa. Mipiringidzo yake yathyoledwa.+ 31  Munthu amene watumidwa kukanena uthenga wakumana ndi mnzake,Ndipo mthenga wina wakumana ndi mnzake.Onsewa akukanena kwa mfumu ya Babulo kuti mzinda wake walandidwa kumbali zonse.+ 32  Akukanena kuti malo owolokera mtsinje alandidwa,+Ngalawa zagumbwa* zawotchedwaKomanso kuti asilikali akuchita mantha kwambiri.” 33  Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli wanena kuti: “Mwana wamkazi wa Babulo* ali ngati malo opunthira mbewu. Ino ndi nthawi yomupondaponda. Posachedwapa nthawi yokolola imufikira.” 34  “Nebukadinezara* mfumu ya Babulo wandidya.+Wandisokoneza. Wandisandutsa chiwiya chopanda kanthu. Wandimeza ngati chinjoka chachikulu.+Wakhuta zinthu zanga zabwino. Wanditsukuluza. 35  Anthu amene akukhala mu Ziyoni akunena kuti, ‘Chiwawa chimene anachitira ine ndi thupi langa chigwerenso Babulo.’+ Ndipo Yerusalemu akunena kuti, ‘Magazi anga akhale pa anthu amene akukhala mʼdziko la Kasidi.’” 36  Choncho Yehova wanena kuti: “Ine ndikuteteza pa mlandu wako,+Ndipo ndidzakubwezerera adani ako.+ Ndidzaphwetsa nyanja yake ndi zitsime zake.+ 37  Babulo adzakhala milu yamiyala,+Malo obisalamo mimbulu,+Chinthu chochititsa mantha komanso chimene anthu azidzachiimbira mluzuNdipo simudzapezeka munthu wokhalamo.+ 38  Anthu onse pamodzi adzabangula ngati mikango yamphamvu.* Adzalira ngati ana a mikango.” 39  “Akadzakhala ndi chilakolako champhamvu chofuna kudya, ndidzawakonzera phwando ndipo ndidzawaledzeretsaNʼcholinga choti asangalale.+Kenako adzagona tulo tosathaNdipo sadzadzukanso,”+ akutero Yehova. 40  “Ndidzapita nawo kumalo okawaphera ngati ana a nkhosa,Ngati nkhosa zamphongo pamodzi ndi mbuzi.” 41  “Taonani! Sesaki* walandidwa,+Dziko limene anthu amalitamanda padziko lonse lapansi latengedwa.+ Babulo wakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ya anthu. 42  Nyanja yasefukira nʼkumiza Babulo. Mzinda wa Babulo wamizidwa ndi mafunde ambiri a nyanjayo. 43  Mizinda yake yakhala chinthu chochititsa mantha, dziko lopanda madzi komanso chipululu. Mizindayo yakhala dziko limene simudzakhalanso munthu aliyense ndipo palibe munthu amene adzadutsemo.+ 44  Ndidzalanga Beli+ ku Babulo,Ndipo ndidzamulavulitsa zimene wameza.+ Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye,Ndipo mpanda wa Babulo udzagwa.+ 45  Tulukani mʼBabulo anthu anga.+ Thawani mkwiyo wa Yehova+ woyaka moto kuti mupulumutse moyo wanu.+ 46  Musataye mtima kapena kuchita mantha ndi uthenga umene udzamveke mʼdzikoli. Mʼchaka chimodzi uthenga udzafika,Kenako mʼchaka chotsatira kudzabweranso uthenga wina,Wonena za chiwawa chimene chidzachitike mʼdzikoli komanso wonena kuti wolamulira akuukira wolamulira mnzake. 47  Choncho masiku adzafikaPamene ndidzawononge zifaniziro zogoba za ku Babulo. Dziko lake lonse lidzachititsidwa manyazi,Ndipo mitembo ya anthu ake onse amene adzaphedwe idzakhala paliponse mumzindawo.+ 48  Kumwamba ndi dziko lapansi komanso chilichonse cha mmenemoZidzafuula mosangalala poona kuti Babulo wagwa,+Chifukwa owononga adzabwera kwa iye kuchokera kumpoto,”+ akutero Yehova. 49  “Babulo sanaphetse anthu a mu Isiraeli okha+Koma anaphetsanso anthu apadziko lonse lapansi ku Babuloko. 50  Inu amene mwathawa lupanga, pitirizani kuthawa, musaime.+ Kumbukirani Yehova pamene muli kutali kwambiri,Ndipo muziganizira Yerusalemu mumtima mwanu.”+ 51  “Tachititsidwa manyazi chifukwa tamva mawu onyoza. Manyazi aphimba nkhope zathu,Chifukwa anthu achilendo* abwera kudzaukira malo oyera a mʼnyumba ya Yehova.”+ 52  “Choncho masiku adzafika,” akutero Yehova,“Pamene ndidzawononge zifaniziro zake zogoba,Ndipo mʼdziko lake lonse anthu ovulazidwa adzakhala akubuula.”+ 53  “Ngakhale Babulo atakwera kukafika kumwamba,+Ngakhale atalimbitsa kwambiri mpanda wake wautaliwo,Anthu amene adzamuwononge adzabwera kuchokera kwa ine,”+ akutero Yehova. 54  “Tamverani! Ku Babulo kukumveka kulira kofuula,+Mʼdziko la Akasidi mukumveka phokoso la chiwonongeko chachikulu,+ 55  Chifukwa Yehova akuwononga Babulo,Adzachititsa kuti mawu ake aakuluwo asamvekenso,Ndipo phokoso la adani ake lidzakhala ngati la mafunde amphamvu. Phokoso la mawu awo lidzamveka. 56  Wowononga adzafikira Babulo.+Asilikali ake adzagwidwa,+Mauta awo adzathyoledwa,Chifukwa Yehova ndi Mulungu amene amapereka chilango choyenera.+ Iye adzabwezera ndithu.+ 57  Ndidzaledzeretsa akalonga ake, anthu ake anzeru,+Abwanamkubwa ake, achiwiri kwa olamulira ake ndi asilikali ake,Ndipo adzagona tulo tosatha,Moti sadzadzukanso,”+ ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova wa magulu ankhondo akumwamba. 58  Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti: “Ngakhale kuti mpanda wa Babulo ndi waukulu, wonse udzagwetsedwa,+Ndipo ngakhale kuti mageti ake ndi ataliatali, adzawotchedwa. Anthu adzagwira ntchito yotopetsa pachabe.Mitundu ya anthu idzadzitopetsa ndi ntchito, koma ntchito yawoyo idzawonongedwa ndi moto.”+ 59  Mneneri Yeremiya anapereka malangizo kwa Seraya mwana wa Neriya+ mwana wa Maseya. Anapereka malangizowo pamene Seraya anapita ndi Zedekiya mfumu ya Yuda ku Babulo mʼchaka cha 4 cha ufumu wake. Seraya anali woyangʼanira zinthu za mfumu. 60  Yeremiya analemba mʼbuku limodzi masoka onse amene adzagwere Babulo. Iye analemba mawu onsewa okhudza zimene zidzachitikire Babulo. 61  Choncho Yeremiya anauza Seraya kuti: “Ukakafika ku Babulo nʼkuona mzindawo, ukawerenge mokweza mawu onsewa. 62  Kenako ukanene kuti, ‘Inu Yehova! Inu mwanena kuti malo ano adzawonongedwa ndipo simudzapezeka aliyense wokhalamo, munthu kapena nyama, komanso kuti mzindawu udzakhala bwinja mpaka kalekale.’+ 63  Ndiye ukakamaliza kuwerenga bukuli, ukalimangirire mwala nʼkuliponya pakati pa mtsinje wa Firate. 64  Ndiyeno ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene Babulo adzamirire ndipo sadzatulukanso+ chifukwa cha tsoka limene ndikumugwetsera. Ndipo anthu amene akukhala mumzindawo adzatopa.’”+ Mawu a Yeremiya athera pamenepa.

Mawu a M'munsi

Zikuoneka kuti limeneli ndi dzina lina la Kasidi.
Mabaibulo ena amati, “Dzazani tizikwama toikamo mivi.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “wadzutsa mitima ya.”
Kapena kuti, “nthunzi.”
Kapena kuti, “mpweya.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Yeretsani.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Yeretsani.”
Mawu akuti “mwana wamkazi wa Babulo” ndi mawu a ndakatulo ndipo nthawi zambiri amanena za mzinda wa Babulo kapena anthu amene ankakhala mumzindawo.
Mʼchilankhulo choyambirira, “Nebukadirezara.” Kameneka ndi kalembedwe kena ka dzinali.
Kapena kuti, “mikango yaingʼono yamanyenje.”
Zikuoneka kuti limeneli ndi dzina lina la Babele (Babulo).
Kapena kuti, “anthu ochokera kudziko lina.”