Yeremiya 9:1-26

  • Yeremiya anali ndi chisoni chachikulu (1-3a)

  • Yehova anaimba mlandu Yuda (3b-16)

  • Kulirira Yuda (17-22)

  • Adzitame chifukwa chodziwa Yehova (23-26)

9  Ndikanakonda mʼmutu mwanga mukanakhala madzi ambiri,Ndiponso maso anga akanakhala kasupe wa misozi.+ Zikanatero, ndikanalira masana ndi usikuChifukwa cha anthu a mtundu wanga amene aphedwa.   Ndikanakonda ndikanakhala ndi malo ogona anthu apaulendo mʼchipululu. Zikanatero, ndikanasiya anthu a mtundu wanga nʼkuwachokera,Chifukwa onse ndi achigololo,+Gulu la anthu ochita zachinyengo.   Iwo ndi okonzeka kunama ngati uta umene wakungidwa.Dzikolo ladzaza ndi chinyengo ndipo palibe amene ali wokhulupirika.+ “Iwo akuchita zoipa motsatizanatsatizana,Ndipo akundinyalanyaza,”+ akutero Yehova.   “Aliyense asamale ndi mnzake,Ndipo musamakhulupirire ngakhale mʼbale wanu. Chifukwa munthu aliyense ndi wachinyengo,+Ndipo munthu aliyense akunenera mnzake zoipa.+   Aliyense amapusitsa mnzake,Ndipo palibe amene amalankhula zoona. Aphunzitsa lilime lawo kulankhula chinyengo.+ Iwo amadzitopetsa okha pochita zinthu zoipa.   Iwe ukukhala pakati pa anthu achinyengo. Iwo anakana kundidziwa chifukwa cha chinyengo chawo,” akutero Yehova.   Choncho, Yehova wa magulu ankhondo akumwamba akuti: “Ine ndidzawayenga komanso kuwayesa,+Nanga mwana wamkazi wa anthu anga ndingamuchitirenso chiyani?   Lilime lawo ndi muvi wakupha umene umalankhula zachinyengo. Munthu amalankhula mwamtendere ndi mnzake,Koma mumtima mwake amakonza chiwembu.”   “Kodi sindikuyenera kuwalanga chifukwa cha zinthu zimenezi?” akutero Yehova. “Kodi sindikuyenera kubwezera mtundu wa anthu oterewa?+ 10  Ndidzalirira mapiri mokweza komanso modandaulaNdipo ndidzaimba nyimbo yoimba polira, polirira malo odyetserako ziweto amʼchipululu,Chifukwa awotchedwa moti palibe munthu amene angadutsemo,Ndipo kulira kwa ziweto sikukumveka. Mbalame zouluka mumlengalenga komanso nyama zakutchire zathawamo ndipo zachoka.+ 11  Yerusalemu ndidzamusandutsa milu ya miyala+ ndiponso malo obisalamo mimbulu,+Ndipo mizinda ya Yuda ndidzaisandutsa mabwinja, popanda wokhalamo.+ 12  Kodi wanzeru ndi ndani kuti amvetse zimenezi, Kodi Yehova walankhula ndi ndani kuti anene zimenezi? Nʼchifukwa chiyani dzikoli lawonongedwa? Nʼchifukwa chiyani lawotchedwa nʼkukhala ngati chipululuChimene palibe munthu amene akudutsamo?” 13  Yehova anayankha kuti: “Nʼchifukwa chakuti iwo asiya chilamulo changa chimene ndinawapatsa.* Komanso chifukwa chakuti sanatsatire chilamulocho ndiponso kumvera mawu anga. 14  Mʼmalo mwake, anatsatira zofuna za mitima yawo mouma khosi+ ndipo anatsatira mafano a Baala, mogwirizana ndi zimene makolo awo anawaphunzitsa.+ 15  Choncho Yehova wa magulu ankhondo akumwamba, Mulungu wa Isiraeli, wanena kuti, ‘Ine ndidzadyetsa anthu amenewa chitsamba chowawa ndipo ndidzawamwetsa madzi apoizoni.+ 16  Ndidzawamwaza pakati pa mitundu ya anthu imene iwo kapena makolo awo sanaidziwe.+ Ndipo ndidzawatumizira adani awo kuti awathamangitse ndi lupanga mpaka nditawawononga onse.’+ 17  Yehova wa magulu ankhondo akumwamba wanena kuti,‘Chitani zinthu mozindikira. Itanani akazi oimba nyimbo zoimba polira kuti abwere.+Ndipo tumizani anthu kuti akaitane akazi odziwa kulira maliro, 18  Kuti abwere mofulumira nʼkudzatiimbira nyimbo zoimba polira,Kuti maso athu atuluke misoziNdipo madzi atuluke mʼzikope zathu.+ 19  Chifukwa ku Ziyoni kwamveka anthu akulira mofuula kuti:+ “Tawonongedwa kwambiri! Tachita manyazi kwambiri! Chifukwa tasiya dziko lathu ndipo atigwetsera nyumba zathu.”+ 20  Akazi inu, tamverani mawu a Yehova. Tcherani khutu kuti mumve mawu otuluka mʼkamwa mwake. Phunzitsani ana anu aakazi kulira maliroNdipo aliyense aphunzitse mnzake nyimbo yoimba polirayi.+ 21  Chifukwa imfa yatilowera mʼnyumba kudzera mʼmawindo.Yalowa munsanja zathu zokhala ndi makoma olimbaKuti mumsewu musapezeke mwana aliyenseNdiponso kuti anyamata asapezeke mʼmabwalo a mzinda.’+ 22  Unene kuti, ‘Yehova wanena kuti: “Mitembo ya anthu idzangoti mbwee panthaka ngati manyowa.Idzakhala ngati tirigu amene angomumweta kumeneKoma popanda munthu womusonkhanitsa pamodzi.”’”+ 23  Yehova wanena kuti: “Munthu wanzeru asadzitame chifukwa cha nzeru zake.+Munthu wamphamvu asadzitame chifukwa cha mphamvu zake.Ndipo munthu wachuma asadzitame chifukwa cha chuma chake.”+ 24  “Koma amene akudzitama adzitame pa chifukwa chakuti: Amamvetsa bwino njira zanga ndipo amandidziwa,+Kuti ine ndine Yehova, amene ndimasonyeza chikondi chokhulupirika ndipo ndimachita zinthu zachilungamo komanso zolungama padziko lapansi,+Chifukwa zinthu zimenezi zimandisangalatsa,”+ akutero Yehova. 25  Yehova wanena kuti, “Taona masiku akubwera ndipo ndidzaimba mlandu aliyense wodulidwa koma amene sanachite mdulidwe wa mtima wake.+ 26  Ndidzaimba mlandu Iguputo,+ Yuda,+ Edomu,+ Aamoni+ ndi Mowabu+ komanso onse odulira ndevu zawo zamʼmbali amene amakhala mʼchipululu.+ Chifukwa mitundu yonse ndi yosadulidwa ndipo anthu onse a mʼnyumba ya Isiraeli sanachite mdulidwe wa mitima yawo.”+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “malangizo anga amene ndinawapatsa.”