Yesaya 11:1-16

  • Ulamuliro wolungama wa nthambi ya Jese (1-10)

    • Mmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wa nkhosa (6)

    • Dziko lapansi lidzadzaza ndi anthu odziwa Yehova (9)

  • Otsala adzabwerera kwawo (11-16)

11  Nthambi+ idzaphuka pachitsa cha Jese,+Ndipo mphukira+ yotuluka pamizu yake idzabereka zipatso.   Mzimu wa Yehova udzakhazikika pa iye,+Mzimu wanzeru+ ndi womvetsa zinthu,Mzimu wopereka malangizo abwino ndi wamphamvu,+Mzimu wodziwa zinthu ndi woopa Yehova.   Iye adzasangalala ndi kuopa Yehova.+ Sadzaweruza potengera zimene wangoona ndi maso ake,Kapena kudzudzula potengera zimene wangomva ndi makutu ake.+   Adzaweruza mwachilungamo anthu onyozeka,Ndipo adzadzudzula anthu mowongoka mtima, pothandiza ofatsa apadziko lapansi. Adzakwapula dziko lapansi ndi ndodo ya pakamwa pake+Ndipo adzapha anthu oipa pogwiritsa ntchito mpweya* wamʼkamwa mwake.+   Chilungamo ndi kukhulupirikaZidzakhala lamba wamʼchiuno mwake.+   Mmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wa nkhosa kwa kanthawi,+Ndipo kambuku adzagona pansi ndi mbuzi yaingʼono,Mwana wa ngʼombe, mkango wamphamvu ndi nyama yonenepa zidzakhala pamodzi,*+Ndipo kamnyamata kakangʼono kadzazitsogolera.   Ngʼombe ndi chimbalangondo zidzadyera pamodziNdipo ana awo adzagona pansi pamodzi. Mkango udzadya udzu ngati ngʼombe yamphongo.+   Mwana woyamwa adzasewera pa una wa mamba,Ndipo mwana amene anasiya kuyamwa adzapisa dzanja lake kudzenje la njoka yapoizoni.   Sizidzavulazana+Kapena kuwonongana mʼphiri langa lonse loyera,+Chifukwa dziko lapansi lidzadzaza ndi anthu odziwa YehovaNgati mmene madzi amadzazira mʼnyanja.+ 10  Pa tsiku limenelo muzu wa Jese+ udzaimirira ngati chizindikiro kwa anthu.+ Anthu a mitundu ina adzatembenukira kwa iye kuti awapatse malangizo,*+Ndipo malo ake okhalapo adzakhala aulemerero. 11  Pa tsiku limenelo Yehova adzaperekanso dzanja lake kachiwiri kuti atenge anthu ake otsala kuchokera ku Asuri,+ ku Iguputo,+ ku Patirosi,+ ku Kusi,+ ku Elamu,+ ku Sinara,* ku Hamati ndi mʼzilumba zamʼnyanja.+ 12  Iye adzakwezera chizindikiro mitundu ya anthu nʼkusonkhanitsa Aisiraeli omwe anamwazikana.+ Ndipo adzasonkhanitsa pamodzi Ayuda omwe anabalalika, kuchokera kumakona 4 a dziko lapansi.+ 13  Nsanje ya Efuraimu idzatha,+Ndipo anthu amene amadana ndi Yuda adzaphedwa. Efuraimu sadzachitira nsanje Yuda,Ndiponso Yuda sadzadana ndi Efuraimu.+ 14  Iwo adzatsika zitunda za* Afilisiti kumadzulo.Onsewa pamodzi, adzalanda katundu wa anthu a Kumʼmawa. Adzatambasula dzanja lawo nʼkugonjetsa* Edomu+ ndi Mowabu,+Ndipo Aamoni adzawagonjera.+ 15  Yehova adzagawa pakati* chigawo cha* nyanja ya Iguputo,+Ndipo adzayendetsa dzanja lake moopseza Mtsinje.*+ Pogwiritsa ntchito mpweya* wake wotentha, adzamenya timitsinje 7 tamtsinjewo,*Ndipo adzachititsa anthu kuwoloka atavala nsapato zawo. 16  Padzakhala msewu waukulu+ wochokera kudziko la Asuri woti mudzadutse anthu ake amene adzatsale,+Ngati mmene zinalili kwa Aisiraeli pamene ankatuluka mʼdziko la Iguputo.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “mzimu.”
Mabaibulo ena amati, “zidzadyera limodzi.”
Kapena kuti, “Anthu a mitundu ina adzamufunafuna.”
Ameneyu ndi Babeloniya.
Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼmapewa a.”
Kapena kuti, “adzasonyeza mphamvu zawo pa.”
Mabaibulo ena amati, “adzaphwetsa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “lilime la.”
Umenewu ndi mtsinje wa Firate.
Kapena kuti, “mzimu.”
Mabaibulo ena amati, “adzaugawa mtsinjewo kukhala timitsinje tisanu ndi tiwiri.”