Yesaya 12:1-6
12 Pa tsiku limenelo ndithu udzanena kuti:
“Ndikukuthokozani, inu YehovaChifukwa ngakhale munandikwiyira,Mkwiyo wanu unachepa pangʼonopangʼono ndipo munanditonthoza.+
2 Taonani! Mulungu ndi chipulumutso changa.+
Ndidzamukhulupirira ndipo sindidzaopa chilichonse,+Chifukwa Ya,* Yehova, ndi mphamvu zanga komanso nyonga zanga,Ndipo iye wakhala chipulumutso changa.”+
3 Mudzatunga madzi mosangalalaPa akasupe achipulumutso.+
4 Pa tsiku limenelo mudzanena kuti:
“Yamikani Yehova, itanani pa dzina lake,Dziwitsani mitundu ya anthu ntchito zake.+
Lengezani kuti dzina lake ndi lokwezeka.+
5 Imbani nyimbo zotamanda Yehova,+ chifukwa wachita zinthu zodabwitsa.+
Lengezani zimenezi padziko lonse lapansi.
6 Fuulani mwachisangalalo inu okhala mu Ziyoni,*Chifukwa Woyera wa Isiraeli amene ali pakati panu ndi wamkulu.”