Yesaya 5:1-30

  • Nyimbo yonena za munda wa mpesa wa Yehova (1-7)

  • Masoka amene anagwera munda wa mpesa wa Yehova (8-24)

  • Mulungu anakwiyira anthu ake (25-30)

5  Ndikufuna ndimuimbire nyimbo wokondedwa wangaNyimbo yonena za munthu amene ndimamukonda ndiponso munda wake wa mpesa.+ Wokondedwa wanga anali ndi munda wa mpesa pamalo achonde mʼmbali mwa phiri.   Iye analima mundawo nʼkuchotsamo miyala. Anadzalamo mphesa zofiira zabwino kwambiri,Anamanga nsanja pakati pa mundawo,Komanso anasemamo choponderamo mphesa.+ Kenako ankayembekezera kuti mundawo ubereka mphesa zabwino,Koma unangobereka mphesa zamʼtchire.+   “Tsopano inu anthu okhala mu Yerusalemu ndiponso inu amuna a mu Yuda,Weruzani pakati pa ine ndi munda wanga wa mpesawu.+   Nʼchiyaninso china chimene ndikanachita mʼmunda wanga wa mpesawuChimene sindinachitemo kale?+ Ine ndinkayembekezera kuti ubereka mphesa zabwino,Koma nʼchifukwa chiyani unabereka mphesa zamʼtchire zokha?   Tsopano ndikuuzaniZimene ndichite ndi munda wanga wa mpesawu: Ndichotsa zomera zimene zinali ngati mpanda wa mundawo,Ndipo uwotchedwa.+ Ndigumula mpanda wake wamiyalaNdipo mundawo udzapondedwapondedwa.   Ndidzangousiya kuti ukhale munda wosalimidwa.+Sindidzatengulira mitengo yake kapena kuulima. Mʼmundamo mudzamera zitsamba zaminga komanso tchire,+Ndipo ndidzalamula mitambo kuti isagwetse mvula pamundawo.+   Chifukwa nyumba ya Isiraeli ndi munda wa mpesa wa Yehova wa magulu ankhondo akumwamba.+Amuna a ku Yuda ndi mitengo ya mpesa imene ankaikonda kwambiri. Iye ankayembekezera chilungamo,+Koma pankachitika zinthu zopanda chilungamo.Ankayembekezera zinthu zolungamaKoma ankangomva anthu akulira chifukwa chozunzidwa.”+   Tsoka kwa anthu amene akuwonjezera nyumba zina panyumba zawo,+Ndiponso amene akuwonjezera minda ina kuminda yawo,+Mpaka malo onse kutha,Ndipo iwo ayamba kukhala okhaokha mʼdzikoli.   Yehova wa magulu ankhondo akumwamba walumbira ine ndikumvaKuti nyumba zambiri, ngakhale kuti ndi zikuluzikulu komanso zokongola,Zidzakhala chinthu chodabwitsa kwambiriNdipo simudzakhala aliyense.+ 10  Chifukwa maekala 10* a munda wa mpesa adzatulutsa mtsuko* umodzi wokha wa vinyo,Ndipo mbewu zokwana muyezo umodzi wa homeri* zidzatulutsa zokolola zokwana muyezo umodzi wokha wa efa.*+ 11  Tsoka kwa anthu amene amadzuka mʼmamawa kwambiri kuti amwe mowa,+Amene amakhala akumwabe mpaka madzulo kutada, moti vinyo amawaledzeretsa. 12  Pa zikondwerero zawo amaimbapo azeze, zoimbira za zingwe,Maseche ndi zitoliro ndipo amamwapo vinyo.Koma saganizira zochita za Yehova,Ndipo saona ntchito ya manja ake. 13  Choncho anthu anga adzapita ku ukapolo kudziko linaChifukwa chosadziwa zinthu.+Anthu awo olemekezeka adzakhala ndi njala,+Ndipo anthu awo onse adzakhala ndi ludzu. 14  Choncho Manda* akulitsa malo akeNdipo atsegula kwambiri pakamwa pake kupitirira malire.+Anthu olemekezeka a mumzindawo, khamu lake limene limachita phokoso komanso zikondwerero zakeAdzatsikira mʼmandamo. 15  Munthu adzawerama,Munthu adzatsitsidwa,Ndipo maso a anthu odzikuza adzatsitsidwa. 16  Yehova wa magulu ankhondo akumwamba adzakwezeka chifukwa cha chiweruzo chake.*Mulungu woona, Woyera,+ adzadziyeretsa kudzera mʼchilungamo.+ 17  Kumeneko, ana a nkhosa amphongo adzadyako msipu ngati kuti ali pamalo odyetserapo ziweto.Alendo adzadyera mʼmabwinja mmene kale munali nyama zodyetsedwa bwino. 18  Tsoka kwa amene amakoka zolakwa zawo ndi zingwe zachinyengoKomanso amene amakoka machimo awo ndi zingwe zokokera ngolo. 19  Tsoka kwa amene amanena kuti: “Agwire ntchito yake mofulumira.Ibwere mwamsanga kuti tiione. Cholinga* cha Woyera wa Isiraeli chichitikeKuti tichidziwe.”+ 20  Tsoka kwa amene akunena kuti chabwino nʼchoipa ndipo choipa nʼchabwino,+Amene akuika mdima mʼmalo mwa kuwala ndi kuwala mʼmalo mwa mdima,Amene akuika zowawa mʼmalo mwa zotsekemera ndi zotsekemera mʼmalo mwa zowawa. 21  Tsoka kwa amene amadziona ngati anzeruKomanso amene amadziona ngati ochenjera.+ 22  Tsoka kwa anthu amene amatchuka ndi kumwa vinyo kwambiri,Komanso kwa anthu amene ndi akatswiri odziwa kusakaniza mowa.+ 23  Tsoka kwa anthu amene amaweruza kuti woipa alibe mlandu chifukwa choti alandira chiphuphu,+Ndiponso kwa amene amalephera kuweruza anthu olungama mwachilungamo.+ 24  Choncho, mofanana ndi mmene lawi la moto limapserezera mapesiKomanso mmene udzu wouma umayakira mʼmalawi a moto,Mizu yawo idzawola,Ndipo maluwa awo adzauluzika ngati fumbi,Chifukwa akana malamulo* a Yehova wa magulu ankhondo akumwambaNdipo anyoza mawu a Woyera wa Isiraeli.+ 25  Nʼchifukwa chake mkwiyo wa Yehova wayakira anthu ake,Ndipo adzatambasula dzanja lake nʼkuwalanga.+ Mapiri adzagwedezeka,Ndipo mitembo yawo idzakhala ngati zinyalala mʼmisewu.+ Chifukwa cha zonsezi, mkwiyo wake sunabwerere,Koma dzanja lake lidakali lotambasula kuti awalange. 26  Iye waikira chizindikiro mtundu wakutali.+Wauimbira likhweru kuti ubwere kuchokera kumapeto kwa dziko lapansi.+Ndipotu mtunduwo ukubwera mofulumira kwambiri.+ 27  Pakati pawo palibe aliyense amene watopa kapena amene akupunthwa. Palibe amene akuwodzera kapena amene akugona. Lamba wa mʼchiuno mwawo sanamasulidwe,Ndipo zingwe za nsapato zawo sizinaduke. 28  Mivi yawo ndi yakuthwa,Ndipo mauta awo onse ndi okungika.* Ziboda za mahatchi awo nʼzolimba ngati mwala wa nsangalabwi,Ndipo mawilo a magaleta awo ali ngati mphepo yamkuntho.+ 29  Kubangula kwawo kuli ngati kwa mkango,Amabangula ngati mikango yamphamvu.*+ Iwo adzabangula nʼkugwira nyamaNdipo adzainyamula popanda woipulumutsa. 30  Pa tsiku limenelo, iwo adzabangulira nyamayoNgati mkokomo wa nyanja.+ Munthu aliyense amene adzayangʼane dzikolo adzaona mdima wodetsa nkhawa.Ngakhale kuwala kudzasanduka mdima chifukwa cha mitambo.+

Mawu a M'munsi

Zikuoneka kuti amenewa anali malo aakulu pafupifupi mahekitala 4.
Amenewa ndi manda a anthu onse. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Kapena kuti, “chilungamo chake.”
Kapena kuti, “Chosankha.”
Kapena kuti, “malangizo.”
Kapena kuti, “ndi okonzekera kuponya mivi.”
Kapena kuti, “mikango yamphamvu yamanyenje.”