Yobu 12:1-25

  • Yankho la Yobu (1-25)

    • “Si ine munthu wamba poyerekezera ndi inu” (3)

    • “Ine ndakhala chinthu choseketsa” (4)

    • ‘Nzeru zili ndi Mulungu’ (13)

    • Mulungu ndi wapamwamba kuposa oweruza ndi mafumu (17, 18)

12  Kenako Yobu anayankha kuti:   “Zoonadi, anthu inu mukudziwa zinthu zambiri,*Ndipo nzeru zidzathera limodzi ndi inu.   Koma inenso ndine wozindikira* ngati inuyo. Si ine munthu wamba poyerekezera ndi inu. Ndi ndani amene sakudziwa zimenezi?   Ine ndakhala chinthu choseketsa kwa anzanga,+Ndakhala munthu amene akuitana Mulungu kuti amuyankhe.+ Munthu wolungama komanso wosalakwa wakhala choseketsa.   Amene zinthu zikuwayendera bwino amanyoza amene akumana ndi tsoka,Iwo amaganiza kuti limagwera anthu okhawo amene akukumana kale ndi mavuto.*   Anthu akuba amakhala mwamtendere mʼmatenti awo,+Amene amakwiyitsa Mulungu amakhala otetezeka,+Anthu amene mulungu wawo ali mʼmanja mwawo.   Koma funsa nyama ndipo zidzakuphunzitsa.Komanso mbalame zamumlengalenga, ndipo zidzakuuza.   Kapena chita chidwi* ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa,Komanso nsomba zamʼnyanja ndipo zidzakuuza.   Kodi ndi ndani pa zonsezi amene sakudziwaKuti dzanja la Yehova ndi limene lachita zimenezi? 10  Moyo wa chilichonse uli mʼdzanja lake,Ndiponso mzimu* wa munthu aliyense.+ 11  Kodi si paja khutu limasiyanitsa mawuNgati mmene lilime limasiyanitsira* kakomedwe ka chakudya?+ 12  Kodi si paja okalamba amakhala ndi nzeru,+Ndipo amene akhala moyo wautali si paja amamvetsa zinthu? 13  Mulungu ali ndi nzeru komanso mphamvu.+Iye amamvetsa zinthu ndipo adzakwaniritsa cholinga chake.+ 14  Iye akagwetsa chinthu, sichingamangidwenso,+Zimene iye watseka, palibe munthu amene angatsegule. 15  Akaletsa mvula, chilichonse chimauma,+Akalola kuti ibwere, madzi amasefukira padziko lapansi.+ 16  Iye ali ndi mphamvu komanso nzeru zopindulitsa.+Ali ndi mphamvu pa munthu amene akusochera ndi amene akusocheretsa ena. 17  Iye amachititsa kuti alangizi ayende opanda nsapato,*Ndipo amapusitsa oweruza.+ 18  Amamasula zingwe zimene mafumu amangira anthu,+Ndipo amawamanga lamba mʼchiuno mwawo. 19  Amachititsa kuti ansembe ayende opanda nsapato,+Ndipo amachotsa paudindo olamulira amphamvu.+ 20  Alangizi okhulupirika amawasowetsa chonena,Ndipo amachotsa kuzindikira kwa amuna achikulire,* 21  Iye amachititsa manyazi anthu olemekezeka,+Ndipo amachititsa anthu amphamvu kuti akhale ofooka.* 22  Amaulula zinthu zozama zimene zili mumdima,+Ndipo amabweretsa kuwala mumdima wandiweyani. 23  Amachititsa mitundu kuti ikhale yamphamvu nʼcholinga choti aiwononge.Amakulitsa mitundu kuti aipititse ku ukapolo. 24  Amachotsa nzeru za atsogoleri* a anthuwo,Ndipo amawachititsa kuti azingoyendayenda mʼchipululu mmene mulibe njira.+ 25  Iwo amafufuza mumdima+ mmene mulibe kuwala,Iye amawachititsa kuti aziyendayenda ngati anthu oledzera.”+

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “anthu inu ndinu anthu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “inenso ndili ndi mtima.”
Kapena kuti, “anthu okhawo amene mapazi awo aterereka.”
Mabaibulo ena amati, “lankhula.”
Kapena kuti, “mpweya.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼkamwa mumasiyanitsira.”
Kapena kuti, “ayende atavulidwa chilichonse.”
Kapena kuti, “kwa akulu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndipo amakhwepetsa lamba wa anthu amphamvu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Amachotsa mtima wa atsogoleri.”