Yobu 17:1-16

  • Yankho la Yobu likupitirira (1-16)

    • “Anthu onyoza andizungulira” (2)

    • “Iye wachititsa kuti anthu azindinyoza” (6)

    • “Ku Manda kudzakhala kunyumba kwanga” (13)

17  “Mzimu wanga wasweka, masiku anga atha.Kumanda kukundidikirira.+   Anthu onyoza andizungulira,+Ndipo diso langa likuyenera kuyangʼanitsitsa* khalidwe lawo lopanduka.   Chonde, landilani chikole changa ndipo muchisunge. Kodi pali winanso amene angagwirane nane chanza nʼkulonjeza kuti andithandiza?+   Mwawapangitsa kuti akhale osazindikira,+Nʼchifukwa chake simunawalemekeze.   Anthu amenewa amauza anzawo kuti agawana nawo chuma chawo,Pamene ana awo akulephera kuona bwinobwino chifukwa cha njala.   Iye wachititsa kuti anthu azindinyoza,+Mwakuti ndakhala munthu amene anthu akumulavulira kumaso.+   Chifukwa cha kuzunzika, maso anga ayamba kuchita mdima.+Manja ndi miyendo yanga zakhala ngati mthunzi.   Anthu owongoka mtima akuyangʼana zimenezi modabwa,Ndipo munthu wosalakwa wakhumudwa chifukwa cha anthu oipa.*   Wolungama akuyendabe panjira yake,+Ndipo amene ali ndi manja oyera, mphamvu zake zikuwonjezereka.+ 10  Komabe, nonsenu mungathe kubwera nʼkuyambiranso kundinena,Chifukwa sindikuonapo aliyense wanzeru pakati panu.+ 11  Masiku anga atha,+Zolinga zanga, zolakalaka za mtima wanga, zasokonezeka.+ 12  Anzanga akumasintha usiku kuti ukhale masana.Iwo akunena kuti, ‘Chifukwa choti kuli mdima, kuwala kuyenera kuti kwayandikira.’ 13  Ngati nditadikira, ku Manda* kudzakhala kunyumba kwanga.+Ndidzayala bedi langa mumdima.+ 14  Ndidzaitana dzenje*+ kuti, ‘Ndinu bambo anga!’ Kwa mphutsi ndidzati, ‘Mayi anga ndi mlongo wanga!’ 15  Ndiye chiyembekezo changa chili kuti?+ Kodi pali amene akuona kuti ndili ndi chiyembekezo? 16  Chidzapita* ku Manda* otsekedwa ndi zitsulo,Pa nthawi imene tonsefe tidzapitira limodzi kufumbi.”+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “likuyenera kukhala pa.”
Kapena kuti, “ampatuko.”
Amenewa ndi manda a anthu onse. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Kapena kuti, “manda.”
Apa akunena chiyembekezo.
Amenewa ndi manda a anthu onse. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.