Yobu 18:1-21

  • Mawu achiwiri a Bilidadi (1-21)

    • Anafotokoza zimene zimachitikira anthu ochimwa (5-20)

    • Ananena kuti Yobu sadziwa Mulungu (21)

18  Bilidadi+ wa ku Shuwa anayankha kuti:   “Kodi usiya nthawi yanji kulankhula choncho? Sonyeza kuti ndiwe wozindikira kuti nafenso tilankhule.   Nʼchifukwa chiyani ukutiona ngati zinyama+Ndiponso ngati anthu opusa?*   Ngakhale utadzikhadzulakhadzula chifukwa choti wakwiya,Kodi dziko lapansi lingasiyidwe chifukwa cha iwe?Kapena kodi thanthwe lingasunthe pamalo ake?   Inde, kuwala kwa woipa kudzazimitsidwa,Ndipo malawi a moto wake sadzawala.+   Kuwala kwa mutenti yake kudzazima,Ndipo nyale imene ili mutenti yake idzazimitsidwa.   Adzakhala alibe mphamvu zoti nʼkuyendera,Ndipo mapulani ake adzamubweretsera mavuto.+   Mapazi ake adzamugwetsera mu ukonde,Ndipo adzayenda mʼzingwe za ukondewo.   Msampha udzamugwira chidendene.Khwekhwe lidzamukola.+ 10  Chingwe chabisidwa pansi kuti chimukole,Ndipo msampha uli panjira yake. 11  Zoopsa zimamuchititsa mantha paliponse,+Ndipo zimamuthamangitsa zili naye pafupi kwambiri. 12  Mphamvu zake zimachepa,Ndipo tsoka+ lidzamuchititsa kuti ayende modzandira.* 13  Khungu lake ladyeka.Matenda oopsa kwambiri agwira* manja ndi miyendo yake. 14  Iye adzachotsedwa mʼmalo otetezeka amutenti yake,+Ndipo adzamupititsa kwa mfumu ya zinthu zoopsa.* 15  Anthu achilendo adzakhala* mutenti yake.Sulufule adzamwazidwa panyumba yake.+ 16  Pansi, mizu yake idzauma,Ndipo pamwamba, nthambi zake zidzafota. 17  Anthu sadzamukumbukiranso padziko lapansi,Ndipo mumsewu dzina lake silidzadziwika.* 18  Adzamuchotsa powala nʼkumupititsa kumdimaNdipo adzamuthamangitsa padziko lapansi. 19  Iye sadzasiya ana kapena mbadwa pakati pa anthu ake,Ndipo sipadzakhala wopulumuka pamalo amene iye akukhala.* 20  Tsiku la tsoka lake likadzafika, anthu a Kumadzulo adzachita mantha kwambiri,Ndipo anthu a Kumʼmawa adzagwidwa ndi mantha aakulu. 21  Izi nʼzimene zimachitikira matenti a munthu wochita zoipa,Komanso malo a munthu amene sadziwa Mulungu.”

Mawu a M'munsi

Mabaibulo ena amati, “anthu odetsedwa.”
Kapena kuti, “motsimphina.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Mwana woyamba kubadwa wa imfa wagwira.”
Kapena kuti, “adzamupititsa ku imfa yowawa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Chinthu chomwe si chake chidzakhala.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “sadzakhala ndi dzina.”
Kapena kuti, “pamalo amene akukhala monga mlendo.”