Yobu 20:1-29

  • Mawu achiwiri a Zofari (1-29)

    • Anaona kuti Yobu wamunyoza (2, 3)

    • Ananena kuti Yobu ndi woipa (5)

    • Ananena kuti Yobu amasangalala kuchita machimo (12, 13)

20  Zofari+ wa ku Naama anayankha kuti:   “Maganizo anga akundivutitsa ndipo achititsa kuti ndiyankheChifukwa mumtima mwanga muli mkwiyo.   Ndamva zimene wanena pondinyoza,Ndipo ndikuyankha chifukwa ndine womvetsa zinthu.*   Uyenera kuti wakhala ukudziwa zimenezi,Chifukwa zakhala zili choncho kuchokera pamene munthu* anaikidwa padziko lapansi,+   Kuti kufuula kwa chisangalalo kwa munthu woipa sikukhalitsa,Ndiponso kuti kusangalala kwa woipa* kumakhala kwa kanthawi.+   Ngakhale kuti ulemerero wake umafika kumwamba,Ndipo mutu wake umafika mʼmitambo,   Adzatheratu mofanana ndi ndowe zake.Anthu amene ankamuona adzati, ‘Kodi munthu uja ali kuti?’   Iye adzauluka ngati maloto ndipo sadzamupeza.Adzathamangitsidwa ngati masomphenya a usiku.   Diso limene linamuona silidzamuonanso,Ndipo malo ake sadzamuonanso.+ 10  Ana ake adzapempha anthu osauka kuti awathandize,Ndipo iye adzabweza chuma chimene analanda kwa anthu ena.+ 11  Iye anali wamphamvu* ngati mmene analili ali mnyamata,Koma adzagona nazo* limodzi mʼfumbi. 12  Ngati zoipa zimatsekemera mʼkamwa mwake,Ngati amazibisa pansi pa lilime lake, 13  Ngati amazisunga ndipo safuna kuzilavula,Koma amapitiriza kuzivumata mʼkamwa mwake, 14  Chakudya chake chidzasasa mʼmatumbo mwake.Chidzakhala ngati poizoni wa mamba* mʼthupi mwake. 15  Wameza chuma, koma adzachisanza.Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwake. 16  Adzayamwa poizoni wa mamba,Mano a mphiri adzamupha.* 17  Sadzaona ngalande za madzi,Mitsinje yosefukira ndi uchi komanso mafuta amumkaka. 18  Adzabweza chuma chake ndipo sadzachidya.*Sadzadyerera chuma chimene anachipeza pamalonda ake.+ 19  Chifukwa waphwanya osauka nʼkuwasiya,Walanda nyumba imene sanamange. 20  Koma sadzapeza mtendere mumtima mwake.Chuma chake sichidzamupulumutsa. 21  Palibe chimene chatsala choti alande,Nʼchifukwa chake zinthu sizidzapitiriza kumuyendera bwino. 22  Chuma chake chikadzafika pachimake, adzakhala ndi nkhawa,Tsoka lalikulu lidzamugwera. 23  Pamene akudzazitsa mimba yake,Mulungu adzamutumizira mkwiyo wake woyaka moto,Adzauvumbitsa pa iye mpaka udzafika mʼmatumbo mwake. 24  Akamadzathawa zida zachitsulo,Mivi yoponyedwa ndi uta wakopa idzamulasa. 25  Adzazula muvi kumsana kwake,Komanso chida chonyezimira pandulu yake,Ndipo mantha adzamugwira.+ 26  Chuma chake chidzasowa mumdima wandiweyani.Moto umene palibe amene waukupizira udzamupsereza.Munthu amene adzapulumuke mutenti yake adzakumana ndi tsoka. 27  Kumwamba kudzaulula zolakwa zake,Ndipo dziko lapansi lidzamuukira. 28  Madzi osefukira adzakokolola nyumba yake.Adzakhala mtsinje wamphamvu pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu. 29  Ili ndi gawo la munthu woipa lochokera kwa Mulungu,Cholowa chimene Mulungu walamula kuti alandire.”

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “chifukwa ndili ndi mzimu womvetsa zinthu.”
Kapena kuti, “mtundu wa anthu; Adamu.”
Kapena kuti, “wampatuko.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Mafupa ake anali amphamvu.”
Apa akunena mphamvu zake.
Kapena kuti, “ndulu ya mamba.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Lilime la mphiri lidzamupha.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “ndipo sadzachimeza.”