Yobu 23:1-17

  • Yankho la Yobu (1-17)

    • Ankafuna kupititsa mlandu wake kwa Mulungu (1-7)

    • Ananena kuti Mulungu sakupezeka (8, 9)

    • “Ndapitiriza kuyenda mʼnjira yake ndipo sindinapatuke” (11)

23  Yobu anayankha kuti:   “Leronso ndipitiriza kudandaula.*+Mphamvu zanga zatha chifukwa chakuti ndikuusa moyo.   Ndikanadziwa kumene ndingapeze Mulungu,+ Ndikanapita kumalo kumene iye amakhala.+   Bwenzi nditapititsa mlandu wanga kwa iyeNdipo ndikanafotokoza mfundo zodziikira kumbuyo.   Ndikanamvetsera zimene akanandiyankha,Ndipo ndikanasunga zimene wandiuza.   Kodi akanalimbana nane pogwiritsa ntchito mphamvu zake zazikulu? Ayi ndithu, iye akanandimvetsera.+   Kumeneko, mlandu wa munthu wowongoka mtima udzaweruzidwa pamaso pake,Ndipo Woweruza wanga adzagamula kuti ndilibe mlandu mpaka kalekale.   Koma ndikapita kumʼmawa, iye kulibe.Ndipo ndikabwerako, sindimupeza.   Iye akamagwira ntchito kumanzere, sindingamuyangʼane.Kenako amatembenukira kumanja, koma sindimuonabe. 10  Koma akudziwa njira imene ine ndikudutsa.+ Akamaliza kundiyesa, ndidzakhala ngati golide woyenga bwino.+ 11  Mapazi anga akuponda mmene mapazi ake akuponda.Ndapitiriza kuyenda mʼnjira yake ndipo sindinapatuke.+ 12  Sindinasiye kutsatira malamulo otuluka pakamwa pake. Ndasunga mosamala mawu ake+ kuposa zimene amafuna kuti ndichite.* 13  Akatsimikiza kuti achite zinthu, ndi ndani angamuletse?+ Akafuna kuchita chinthu, amachitadi.+ 14  Iye adzachita zonse zimene wakonza kuti andichitire,Ndipo pali zinthu zambiri zoterezi zimene akuganiza kuti andichitire. 15  Nʼchifukwa chake ndikuda nkhawa ndi zimene Mulungu angandichitire.Ndikaganizira za iye, ndikumachita mantha kwambiri. 16  Mulungu wachititsa kuti nditaye mtima,Ndipo Wamphamvuyonse wachititsa kuti ndikhale ndi mantha. 17  Koma mdima sunapangitse kuti ndisiye kulankhula,Kapenanso mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.”

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “ndidandaula moukira.”
Kapena kuti, “kuposa zimene anandiuza kuti ndichite.”