Yobu 26:1-14

  • Yankho la Yobu (1-14)

    • “Komatu ndiye wathandiza munthu wopanda mphamvu!” (1-4)

    • ‘Mulungu anaika dziko lapansi mʼmalere’ (7)

    • ‘Kambali kakangʼono chabe ka zochita za Mulungu’ (14)

26  Yobu anayankha kuti:   “Komatu ndiye wathandiza munthu wopanda mphamvu! Wapulumutsa munthu wa manja ofooka.+   Waperekadi malangizo othandiza kwa munthu wopanda nzeru.+ Komanso wachititsa kuti anthu ambiri adziwe nzeru zothandiza.   Kodi ukuuza ndani,Ndipo ndi ndani amene wakuuzira zimene ukunenazi?*   Akufa alibe mphamvu ndipo amanjenjemera pamaso pa Mulungu.Iwo ali pansi kwambiri kuposa madzi ndi zonse zimene zimakhala mmenemo.   Manda* ali maliseche pamaso pa Mulungu,+Ndipo malo achiwonongeko* amakhala osavundikira.   Iye anatambasula thambo lakumpoto* pamwamba pa malo opanda kanthu,+Ndipo dziko lapansi analiika mʼmalere.   Iye anakulunga madzi mʼmitambo yake,+Mʼnjira yoti mitamboyo isaphulike chifukwa cha kulemera kwa madziwo.   Anaphimba mpando wake wachifumu kuti usamaoneke,Anauphimba ndi mtambo wake.+ 10  Anaika malire pakati pa thambo ndi nyanja,+Anaika malire pakati pa kuwala ndi mdima. 11  Zipilala zakumwamba zimanjenjemera,Zimachita mantha ndi kudzudzula kwa Mulungu. 12  Ndi mphamvu zake amavundula nyanja,+Ndipo ndi kuzindikira kwake amaduladula chilombo cha mʼnyanja.*+ 13  Ndi mpweya umene wapuma,* amapangitsa kuti kumwamba kukhale koyera.Dzanja lake limabaya njoka yothamanga. 14  Komatu zimenezi ndi kambali kakangʼono chabe ka zochita zake,+Ndipo tangomva kunongʼona kwapansipansi kwa mphamvu zake. Ndiye ndi ndani amene angamvetse mabingu ake amphamvu?”+

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “Kodi mpweya (mzimu) umene watuluka mwa iwe ndi wandani?”
Amenewa ndi manda a anthu onse. Onani Matanthauzo a Mawu Ena.
Kapena kuti, “Ndipo Abadoni.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “anatambasula kumpoto.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “amaduladula Rahabi.”
Kapena kuti, “mphepo.”