Yobu 35:1-16
35 Elihu anapitiriza kulankhula kuti:
2 “Kodi mukutsimikiza kuti zimene mukunena nʼzoona moti munganene kuti,‘Ndine wolungama kuposa Mulunguʼ?+
3 Inu mwanena kuti, ‘Kodi ndikachita zabwino, inu* muli nazo ntchito yanji?
Kodi ndikapanda kuchimwa ndimapindula chiyani?’+
4 Ine ndikuyankhani inuyoLimodzi ndi anzanu+ amene muli nawowo.
5 Yangʼanani kumwamba muone,Muonetsetse mitambo+ imene ili kutali ndi inu.
6 Mukachimwa, kodi Mulungu zimamupweteka bwanji?+
Zolakwa zanu zikachuluka, kodi zimamukhudza bwanji Mulungu?+
7 Ngati muli wolungama, kodi mumamʼpatsa chiyani?Kodi amalandira chiyani kuchokera kwa inu?+
8 Zoipa zimene mumachita zimangopweteka munthu ngati inu nomwe,Ndipo chilungamo chanu chimangothandiza mwana wa munthu.
9 Ngati anthu akuponderezedwa kwambiri, amalira kuti athandizidwe.Amalira kuti apulumutsidwe mʼmanja mwa anthu amphamvu amene akuwapondereza.+
10 Koma palibe amene amanena kuti, ‘Kodi Mulungu Wamkulu amene anandipanga+ ali kuti,Amene amachititsa kuti tiziimba nyimbo usiku?’+
11 Iye amatiphunzitsa+ zinthu zambiri kuposa nyama zakutchire,+Ndipo amatipatsa nzeru kuposa mbalame zamumlengalenga.
12 Iwo amalira kuti athandizidwe, koma iye sawayankha,+Chifukwa cha kunyada kwa anthu oipa.+
13 Ndithudi Mulungu samvetsera kulira kwachinyengo,*+Wamphamvuyonse samvetsera zinthu zabodza.
14 Ndiye kodi iye angamvetsere mukamadandaula kuti simukumuona?+
Iye ndi amene angaweruze mlandu wanu, choncho muzimuyembekezera.+
15 Pajatu iye sanakukwiyireni nʼkukupatsani chilango,Komanso sanaone kudzitukumula kwanu.+
16 Choncho Yobu watsegula pakamwa pake mopanda phindu.Ngakhale kuti sakudziwa zoona, iye akulankhula zambirimbiri.”+