Yobu 9:1-35

  • Yankho la Yobu (1-35)

    • Munthu sangalimbane ndi Mulungu (2-4)

    • ‘Mulungu amachita zinthu zosatheka kuzifufuza’ (10)

    • Palibe amene angatsutsane ndi Mulungu (32)

9  Yobu anayankha kuti:   “Ndikudziwa ndithu kuti zili choncho. Koma kodi munthu anganene bwanji kuti ndi wosalakwa pamaso pa Mulungu?+   Ngati munthu akufuna kutsutsana ndi Mulungu,*+Munthuyo sangathe kuyankha funso ndi limodzi lomwe pamafunso ake 1,000.   Iye ali ndi mtima wanzeru ndiponso mphamvu zambiri.+ Ndani angatsutsane naye koma osavulala?+   Iye amasuntha* mapiri popanda aliyense kudziwa.Amawagubuduza atakwiya.   Amagwedeza dziko lapansi nʼkulisuntha pamalo ake,Moti zipilala zake zimagwedera.+   Amalamula dzuwa kuti lisawaleNdipo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.+   Iye amatambasula kumwamba yekha,+Ndipo amayenda pamafunde ataliatali a mʼnyanja.+   Anapanga gulu la nyenyezi la Asi, la Kesili ndi la Kima,+Komanso gulu la nyenyezi za kumʼmwera. 10  Amachita zinthu zazikulu ndi zosatheka kuzifufuza,+Zinthu zodabwitsa zimene ndi zosatheka kuziwerenga.+ 11  Iye amadutsa pafupi ndi ine koma sinditha kumuona,Amandidutsa koma ine osamuzindikira. 12  Iye akalanda chinthu, ndani angalimbane naye? Ndani angamufunse kuti, ‘Mukuchita chiyani?’+ 13  Mulungu sadzabweza mkwiyo wake.+Ngakhale anthu othandiza Rahabi*+ adzamugwadira. 14  Nʼchifukwa chake ndikamamuyankha,Ndiyenera kusankha bwino mawu anga. 15  Ngakhale nditakhala kuti ndikunena zoona, sindingamuyankhe.+ Koma ndingachonderere woweruza wanga kuti andichitire chifundo. 16  Kodi nditamuitana, angandiyankhe? Sindikukhulupirira kuti angandimvetsere. 17  Chifukwa iye wandivulaza ndi mavuto angati mphepo yamkuntho,Ndipo wachulukitsa mabala anga popanda chifukwa.+ 18  Sakulola kuti ndikokeko mpweya,Ndipo akungopitiriza kuwonjezera mavuto anga. 19  Pa nkhani yokhala ndi mphamvu, iye ndi wamphamvu kwambiri.+ Pa nkhani yochita zinthu mwachilungamo, iye amanena kuti: ‘Ndi ndani angandiimbe mlandu?’* 20  Ngakhale ndikanapezeka kuti ndine wosalakwa, pakamwa panga pakanandiweruza kuti ndine wolakwa.Ngakhale nditakhala wokhulupirika,* adzandipezabe ndi mlandu.* 21  Ngakhale nditakhala wokhulupirika,* sindikudziwa zimene zingandichitikire,Moyo wangawu sindikuufunanso.* 22  Zonsezi mfundo yake ndi imodzi. Nʼchifukwa chake ndikunena kuti,‘Iye amawononga onse, osalakwa* komanso oipa.’ 23  Anthu atafa mwadzidzidzi ndi madzi osefukira,Iye angaseke anthu osalakwa akuvutika. 24  Dziko lapansi laperekedwa mʼmanja mwa anthu oipa.+Iye amaphimba maso a oweruza* a dzikolo. Ngati si iyeyo, ndiye ndi ndani? 25  Panopa masiku anga akufulumira kwambiri kuposa munthu wothamanga.+Iwo akuthawa asanaone zabwino. 26  Amayenda mofulumira ngati ngalawa za bango,Ngati ziwombankhanga zimene zimambwandira nyama yoti zidye. 27  Ngati nditanena kuti, ‘Ndiiwala kudandaula kwanga,Ndisintha maonekedwe a nkhope yanga nʼkukhala wosangalala,’ 28  Ndingachitebe mantha chifukwa cha zopweteka zanga zonse,+Ndipo ndikudziwa kuti simungandipeze kuti ndine wosalakwa. 29  Ndingapezekebe kuti ndine wolakwa.* Ndiye ndivutikirenji pachabe?+ 30  Nditati ndisambe mʼmadzi oyera,*Komanso kusamba mʼmanja ndi sopo,+ 31  Inuyo mungandiviike mʼdzenje la matope,Moti ngakhale zovala zanga zomwe zinganyansidwe nane. 32  Chifukwa iye si munthu ngati ine kuti ndingamuyankhe,Kapena kuti titengerane kukhoti.+ 33  Palibe munthu woti agamule mlandu wathu,*Amene angakhale woweruza wathu.* 34  Ngati iye akanasiya kundimenya,*Komanso kundiopseza ndi zinthu zake zochititsa mantha,+ 35  Ndikanalankhula naye mopanda mantha,Chifukwa ine sindiopa kulankhula.”

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “akufuna kutengera Mulungu kukhoti.”
Kapena kuti, “Iye amachotsa.”
Nʼkutheka kuti chimenechi ndi chilombo choopsa cha mʼnyanja.
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ndi ndani angandisumire?”
Kapena kuti, “Ngakhale nditakhala wosalakwa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “adzapezabe kuti ndine wokhotakhota.”
Kapena kuti, “Ngakhale nditakhala wosalakwa.”
Kapena kuti, “ndikuunyoza; ndikuukana.”
Kapena kuti, “okhulupirika.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “nkhope za oweruza.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “woipa.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼmadzi achipale chofewa.”
Kapena kuti, “Palibe mʼkhalapakati pa mlandu wathu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Amene angaike dzanja lake patonsefe.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “Ngati iye akanachotsa ndodo yake pa ine.”