Yoswa 5:1-15

  • Mdulidwe ku Giligala (1-9)

  • Chikondwerero cha Pasika; mana anasiya (10-12)

  • Kalonga wa gulu lankhondo la ­Yehova (13-15)

5  Mafumu onse a Aamori+ amene anali kutsidya la kumadzulo kwa mtsinje wa Yorodano, ndi mafumu onse a Akanani+ amene anali mʼmbali mwa nyanja, anamva kuti Yehova anaphwetsa madzi a mtsinje wa Yorodano mpaka Aisiraeli onse atawoloka. Atangomva zimenezo, anachita mantha kwambiri,*+ moti analibenso mphamvu chifukwa choopa Aisiraeli.+  Pa nthawi imeneyo, Yehova anauza Yoswa kuti: “Panga timipeni tamiyala ndipo udule khungu+ amuna a Chiisiraeli kachiwiri.”  Choncho Yoswa anapanga timipeni tamiyala nʼkudula amuna a Chiisiraeli. Zimenezi zinachitikira ku Gibeyati-haaraloti.*+  Yoswa anawadula chifukwa chakuti amuna onse amene anatuluka mu Iguputo, onse otha kupita kunkhondo,* anali atafera mʼchipululu pa ulendo wochokera ku Iguputo.+  Anthu onse amene anachoka ku Iguputo anali odulidwa. Koma onse amene anabadwira mʼchipululu pa ulendo wochokera ku Iguputo, anali asanadulidwe.  Aisiraeliwo anayenda mʼchipululu zaka 40,+ mpaka anthu onse amene anatuluka mu Iguputo, amene sanamvere mawu a Yehova+ atatha kuphatikizapo amuna onse otha kupita kunkhondo. Amenewo Yehova anawalumbirira kuti sadzawalola kuona dziko+ limene Yehova analumbirira makolo awo kuti adzalipereka kwa anthu ake,*+ dziko loyenda mkaka ndi uchi.+  Iye analowetsa mʼdzikomo ana awo mʼmalo mwa iwowo.+ Ana amenewa Yoswa anawadula, chifukwa sanadulidwe pa nthawi imene anali pa ulendo.  Atamaliza kudula amuna onse, aliyense anakhalabe muhema wake pamsasapo mpaka atachira.  Kenako Yehova anauza Yoswa kuti: “Lero ndachititsa kuti Aiguputo asamakunyozeninso.”* Choncho malowo amawatchula kuti Giligala,*+ mpaka lero. 10  Aisiraeliwo anakhalabe ku Giligala ndipo anachita Pasika madzulo pa tsiku la 14 la mweziwo,+ mʼchipululu cha Yeriko. 11  Tsiku lotsatira, iwo anayamba kudya zokolola za mʼdzikomo. Pa tsikuli anayamba kudya mikate yopanda zofufumitsa+ ndiponso tirigu wokazinga. 12  Mana analeka kugwa pa tsikuli, pamene Aisiraeli anadya zokolola za mʼdzikomo. Kuyambira pamenepo, sipankakhalanso mana oti Aisiraeli azidya.+ Choncho chaka chimenechi nʼchimene iwo anayamba kudya zokolola za mʼdziko la Kanani.+ 13  Yoswa ali pafupi ndi Yeriko, anakweza maso ake ndipo anaona mwamuna wina+ ataima patsogolo pake, atanyamula lupanga mʼmanja.+ Yoswa anamuyandikira nʼkumufunsa kuti: “Kodi uli kumbali yathu kapena kumbali ya adani athu?” 14  Munthuyo anayankha kuti: “Ayi, ndabwera chifukwa ndine kalonga* wa gulu lankhondo la Yehova.”+ Atatero, Yoswa anagwada nʼkuwerama mpaka nkhope yake pansi, ndipo anamuuza kuti: “Lankhulani mbuyanga kwa kapolo wanu.” 15  Ndiyeno kalonga wa gulu lankhondo la Yehovayo anauza Yoswa kuti: “Vula nsapato zako, chifukwa malo amene waimawo ndi oyera.” Nthawi yomweyo, Yoswa anavula nsapato zake.+

Mawu a M'munsi

Mʼchilankhulo choyambirira, “mitima yawo inasungunuka.”
Kutanthauza “Phiri la Makungu Akunsonga.”
Kapena kuti, “onse azaka zoyenera kukhala asilikali.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “kwa ife.”
Kapena kuti, “Ndachotsa chitonzo cha Iguputo pa inu.”
Kutanthauza “Kuchotsa.”
Kapena kuti, “ndine mtsogoleri.”