Zefaniya 3:1-20

  • Yerusalemu, mzinda wogalukira ndiponso wachinyengo (1-7)

  • Kuweruza ndiponso kubwezeretsa (8-20)

    • Kusintha nʼkuyamba kulankhula chilankhulo choyera (9)

    • Anthu odzichepetsa komanso ooneka onyozeka adzapulumutsidwa (12)

    • Yehova adzakondwera ndi Ziyoni (17)

3  Tsoka kwa mzinda wogalukira, woipitsidwa komanso wopondereza anthu ake.+   Mzindawo sunamvere+ ndipo sunalole kulangizidwa,+ Sunakhulupirire Yehova+ komanso sunayandikire Mulungu wake.+   Akalonga ake ali ngati mikango yobangula.+ Oweruza ake ali ngati mimbulu imene ikuyenda usiku.Imene pofika mʼmawa imadya chilichonse osasiya ngakhale fupa.   Aneneri ake ndi amwano ndiponso achinyengo.+ Ansembe ake amaipitsa zinthu zopatulika,+Ndipo amaphwanya malamulo.+   Yehova ndi wolungama mumzindawo+ ndipo salakwitsa. Mʼmawa uliwonse iye amadziwitsa anthu chilungamo chake,+Moti mofanana ndi kuwala, chilungamocho sichisowa. Koma wosalungama sachita manyazi.+   “Ine ndinawononga mitundu ya anthu ndi kusakaza nsanja zawo zamʼmakona. Ndinawononga misewu yawo moti simunkayendanso anthu. Mizinda yawo inakhala mabwinja ndipo simunatsale munthu aliyense.+   Ndiyeno ndinati, ‘Mosakayikira udzandiopa ndipo udzalola kulangizidwa,’+ Kuti iye* asawonongedwe.+Ndidzamuimba mlandu wa zonsezi.* Koma mʼpamene ankafunitsitsa kwambiri kuchita zoipa.+   Yehova wanena kuti: ‘Choncho pitirizani kundiyembekezera,*+Mpaka tsiku limene ndidzanyamuke kuti ndikatenge zinthu za anthu omwe ndawagonjetsa.*Chiweruzo changa ndi choti ndisonkhanitse mitundu ya anthu, ndisonkhanitse maufumu,Kuti ndiwasonyeze mkwiyo wanga, ndithu mkwiyo wanga wonse woyaka moto,+Chifukwa moto wa mkwiyo wanga udzawotcheratu dziko lonse lapansi.+   Pa nthawiyo ndidzasintha chilankhulo cha anthu kuti chikhale chilankhulo choyera,Kuti onse aziitanira pa dzina la Yehova,Nʼkumamutumikira mogwirizana.’*+ 10  Kuchokera kuchigawo cha mitsinje ya ku Itiyopiya,Anthu amene akundichonderera, anthu anga obalalitsidwa, adzandibweretsera mphatso.+ 11  Pa tsiku limenelo, sudzachita manyaziChifukwa cha zinthu zonse zimene unachita pondigalukira,+Popeza ndidzachotsa anthu odzikweza pakati panu.Ndipo sudzakhalanso wodzikweza mʼphiri langa lopatulika.+ 12  Ndidzasiya anthu odzichepetsa ndi ofatsa kuti akhalebe pakati panu,+Ndipo iwo adzapeza chitetezo mʼdzina la Yehova. 13  Aisiraeli otsala+ sadzachita zinthu zosalungama.+Sadzalankhula bodza kapena kukhala ndi lilime lachinyengo.Iwo adzadya ndi kugona ndipo sipadzakhala wowaopseza.”+ 14  Fuula mosangalala, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni!* Fuula chifukwa chopambana, iwe Isiraeli!+ Sangalala ndiponso kondwera ndi mtima wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!*+ 15  Yehova wakuchotsera ziweruzo zake.+ Wabweza mdani wako.+ Yehova, Mfumu ya Isiraeli, ali pakati panu.+ Ndipo sudzaopanso kuti tsoka likugwera.+ 16  Tsiku limenelo Yerusalemu adzauzidwa kuti: “Usaope iwe Ziyoni,+ Ndipo manja ako asafooke. 17  Yehova Mulungu wako ali pakati panu+ Ndipo adzakupulumutsa chifukwa ndi wamphamvu. Iye adzakondwera nawe.+ Adzakhala phee chifukwa chokhutira ndi chikondi chimene akukusonyeza, Ndipo adzafuula mosangalala chifukwa chokondwera nawe. 18  Ndidzasonkhanitsa anthu amene akumva chisoni chifukwa chosapezeka pazikondwerero zako.+Iwo sanali ndi iwe chifukwa anali ku ukapolo kumene ankanyozedwa.+ 19  Pa nthawiyo ndidzalanga onse amene akukupondereza,+Ndipo ndidzapulumutsa wotsimphina.+Ndidzasonkhanitsa anthu amene anabalalitsidwa.+ Ndidzachititsa kuti akhale otchuka* komanso azitamandidwa,Mʼdziko lonse limene anachititsidwa manyazi. 20  Pa nthawiyo ndidzakubweretsani,Ndidzachita zimenezi pa nthawi imene ndidzakusonkhanitseni. Ndikadzabwezeretsa iwe ukuona, anthu a mtundu wako amene anatengedwa kupita ku ukapolo,+Ndidzachititsa kuti ukhale wotchuka* komanso uzitamandidwa,+ pakati pa anthu a mitundu yonse yapadziko lapansi,” watero Yehova.

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “Ndidzamulanga chifukwa cha zonsezi.”
Kutanthauza Yerusalemu.
Kapena kuti, “kundidikirira moleza mtima.”
Mabaibulo ena amati, “ndidzanyamuke ngati mboni.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “phewa ndi phewa.”
Mawu akuti “mwana wamkazi wa Ziyoni” ndi mawu andakatulo ndipo nthawi zambiri amanena za mzinda wa Yerusalemu kapena anthu amene ankakhala mumzindawo.
Mawu akuti “mwana wamkazi wa Yerusalemu” ndi mawu andakatulo ndipo nthawi zambiri amanena za mzinda wa Yerusalemu kapena anthu amene ankakhala mumzindawo.
Mʼchilankhulo choyambirira, “ndi dzina.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “ndi dzina.”