Zekariya 11:1-17

  • Zotsatira za kukana mʼbusa weniweni wa Mulungu (1-17)

    • “Weta nkhosa zimene zinayenera kuphedwa” (4)

    • Ndodo ziwiri: Wosangalatsa komanso Mgwirizano (7)

    • Malipiro a mʼbusa: Ndalama 30 zasiliva (12)

    • Ndalama zinaponyedwa mosungira chuma (13)

11  “Iwe Lebanoni, tsegula zitseko zako,Kuti moto uwotcheretu mitengo yako ya mkungudza.   Lira mofuula, iwe mtengo wa junipa,* chifukwa mtengo wa mkungudza wagwa.Mitengo ikuluikulu yawonongedwa. Lirani mofuula, inu mitengo ya thundu* ya ku Basana,Chifukwa nkhalango yowirira kwambiri ija yawonongedwa.   Tamverani! Abusa akulira mofuula,Chifukwa ulemerero wawo watha. Tamverani! Mikango yamphamvu ikubangula,Chifukwa nkhalango zowirira za mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodano zawonongedwa.  Yehova Mulungu wanga wanena kuti, ‘Weta nkhosa zimene zinayenera kuphedwa.+  Amene anazigula amazipha,+ koma saimbidwa mlandu. Amene akuzigulitsa+ akunena kuti: “Yehova atamandike chifukwa ndilemera.” Ndipo abusa ake sazichitira chifundo.’+  ‘Sindidzachitiranso chifundo anthu okhala mʼdzikoli,’ watero Yehova. ‘Choncho ine ndidzachititsa kuti aliyense aziponderezedwa ndi mnzake ndiponso mfumu yake. Iwo adzawononga dzikoli, ndipo ine sindidzawapulumutsa mʼmanja mwawo.’”  Ine ndinayamba kuweta nkhosa zimene zinayenera kuphedwa+ ndipo ndinachita zimenezi chifukwa cha inu, anthu ovutika a mʼgulu la nkhosali. Choncho ndinatenga ndodo ziwiri. Ina ndinaipatsa dzina lakuti Wosangalatsa ndipo inayo ndinaipatsa dzina lakuti Mgwirizano.+ Ndiyeno ndinayamba kuweta gulu la nkhosalo.  Ndinachotsa abusa atatu mʼmwezi umodzi chifukwa sindinathenso kuwalezera mtima ndipo iwonso ananyansidwa nane.  Ndipo ndinanena kuti: “Sindikuwetaninso. Amene akufa afe ndipo amene akuwonongeka, awonongeke. Otsalawo adyane.” 10  Choncho ndinatenga ndodo yanga yotchedwa Wosangalatsa+ ija nʼkuiduladula. Ndinachita izi kuti ndithetse pangano limene ndinachita ndi anthu a mtundu wanga. 11  Panganolo linaswedwa tsiku limenelo ndipo nkhosa zovutika zimene zinaona ndikuchita zimenezi, zinadziwa kuti zimene ndachitazo nʼzimene Yehova ananena. 12  Kenako ndinawauza kuti: “Ngati mukuona kuti nʼzoyenera, ndipatseni malipiro anga. Koma ngati mukuona kuti nʼzosayenera musandipatse.” Iwo anandilipira* ndalama 30 zasiliva.+ 13  Kenako Yehova anandiuza kuti: “Kaziponye mosungiramo chuma. Zimenezi ndi ndalama zochepa zimene aona kuti angandilipire.”+ Choncho ndinatenga ndalama 30 zasilivazo nʼkukaziponya mosungiramo chuma panyumba ya Yehova.+ 14  Kenako ndinathyola ndodo yanga yachiwiri ija yotchedwa Mgwirizano,+ pothetsa ubale wa Yuda ndi Isiraeli.+ 15  Ndiyeno Yehova anandiuza kuti: “Tenga zida za mʼbusa wopanda pake.+ 16  Chifukwa ndilola kuti mʼdzikoli mukhale mʼbusa wina. Mʼbusa ameneyu sadzasamalira nkhosa zimene zikuwonongeka.+ Iye sadzafunafuna nkhosa yaingʼono, sadzachiritsa yovulala+ komanso sadzapatsa chakudya nkhosa zimene zikadali zamphamvu. Mʼmalomwake adzadya nyama ya nkhosa yonenepa+ ndipo adzakupula* ziboda za nkhosazo.+ 17  Tsoka kwa mʼbusa wanga wopanda pake+ amene akusiya nkhosa.+ Lupanga lidzamutema padzanja ndi diso lake lakumanja. Dzanja lake lidzalumala kwambiri,Ndipo diso lake lamanja lidzachita khungu.”*

Mawu a M'munsi

Mtengo wa junipa ndi wofanana ndi mtengo wa mkungudza.
Ena amati, “nthundu.”
Mʼchilankhulo choyambirira, “anandiyezera.”
Ena amati, “kusupula.”
Kapena kuti, “lidzachita mdima.”