Kubwereza Gawo 4

Kubwereza Gawo 4

Kambiranani mafunsowa ndi mphunzitsi wanu:

  1. Werengani Miyambo 13:20.

    • N’chifukwa chiyani muyenera kusankha mwanzeru anthu ocheza nawo?

      (Onani Phunziro 48.)

  2. Kodi ndi malangizo a m’Baibulo ati omwe angakuthandizeni ngati ndinu . . .

    • mwamuna kapena mkazi wapabanja?

    • kholo kapena mwana?

      (Onani Phunziro 49 ndi 50.)

  3. Kodi timasangalatsa Yehova tikamalankhula zinthu zotani? Nanga Yehova sasangalala tikamalankhula zinthu zotani?

    (Onani Phunziro 51.)

  4. Kodi ndi mfundo za m’Baibulo ziti zomwe zingakuthandizeni kuti muzisankha mwanzeru zovala komanso mmene mungadzikongoletsere?

    (Onani Phunziro 52.)

  5. Kodi mungatani kuti muzisankha zosangalatsa zomwe sizingakhumudwitse Yehova?

    (Onani Phunziro 53.)

  6. Werengani Mateyu 24:​45-47.

    • Kodi “kapolo wokhulupirika ndi wanzeru” ndi ndani?

      (Onani Phunziro 54.)

  7. Kodi tingagwiritse ntchito bwanji nthawi, mphamvu, ndalama ndi zinthu zathu zina pothandiza mpingo?

    (Onani Phunziro 55.)

  8. Werengani Salimo 133:1.

    • Kodi ndi zinthu ziti zomwe mungachite pothandiza kuti mpingo ukhale wogwirizana?

      (Onani Phunziro 56.)

  9. Kodi tingatani kuti Yehova atithandize tikachita tchimo lalikulu?

    (Onani Phunziro 57.)

  10. Werengani 1 Mbiri 28:9.

    • Kodi tingasonyeze bwanji kuti timatumikira Yehova “ndi mtima wathunthu” pamene anthu ena akutitsutsa kapena ngati asiya kutumikira Yehova?

    • Kodi pali zinthu zomwe mukufunikira kusintha kuti mukhalebe okhulupirika kwa Yehova komanso kuti mutuluke m’chipembedzo chonyenga?

      (Onani Phunziro 58.)

  11. Kodi mungakonzekere bwanji kuzunzidwa?

    (Onani Phunziro 59.)

  12. Kodi ndi zinthu ziti zomwe mukufuna kumachita kuti mupitirize kutumikira Yehova?

    (Onani Phunziro 60.)