Patapita nthawi, Yehova anatumiza mngelo ameneyu kudzabadwa ngati mwana ku Betelehemu kwa namwali wina dzina lake Mariya. Mwana ameneyo anam’patsa dzina lakuti Yesu.—Yohane 6:38.
Ali padziko lapansi, Yesu anasonyeza bwino kwambiri makhalidwe a Mulungu. Iye anali wachifundo, wachikondi ndiponso anthu ankafika kwa iye momasuka. Ankaphunzitsa anthu choonadi chonena za Yehova mopanda mantha.
Yesu ankachita zinthu zabwino koma anthu ankadana naye. 1 Petulo 2:21-24
Yesu anachiritsanso odwala ndi kuukitsa anthu ena amene anafa.
Atsogoleri a chipembedzo ankadana ndi Yesu chifukwa iye ankaulula zochita zawo zoipa ndipo ankaululanso kuti iwo ankaphunzitsa zinthu zabodza.
Atsogoleri a chipembedzo anachititsa Aroma kuti amenye ndi kupha Yesu.