Pali Mulungu woona mmodzi yekha ndipo dzina lake ndi Yehova. (Salimo 83:18) Iye ndi Mzimu ndipo sitingathe kumuona. Iye amatikonda ndipo amafuna kuti ifenso tizimukonda komanso tizikonda anthu anzathu. (Mateyu 22:35-40) Iye ndi Wamkulukulu ndiponso ndi Mlengi wa zinthu zonse.