CHIGAWO 13 Kodi Tiyenera Kuchita Chiyani Kuti Tikondweretse Mulungu? YAMBANI Kodi Tiyenera Kuchita Chiyani Kuti Tikondweretse Mulungu? Pepani, zalephereka. Koperani Vidiyoyi Onetsani Kaonekedwe ka Mawu Bisani Kaonekedwe ka Mawu Muzipewa kuchita zinthu zoipa. 1 Akorinto 6:9, 10 Ngati timakonda Yehova, tiyenera kupewa kuchita zinthu zimene iye amadana nazo. Yehova safuna kuti tiziba, tiziledzera kapena tizigwiritsa ntchito mankhwala osokoneza bongo. Mulungu amadana ndi aliyense wopha munthu kapena wochotsa mimba, ndiponso amadana n’zoti anthu azigonana amuna kapena akazi okhaokha. Iye safuna kuti tikhale adyera kapena andewu. Sitiyenera kulambira mafano kapena kuchita zinthu zogwirizana ndi kukhulupirira mizimu. M’dziko lapansi la Paradaiso limene likubweralo, simudzakhala anthu ochita zoipa. Muzichita zinthu zabwino. Mateyu 7:12 Kuti tikondweretse Mulungu, tiyenera kuyesetsa kumutsanzira. Muzikonda anthu ena powakomera mtima ndi kuwathandiza. Mukhale oona mtima. Mukhale achifundo ndipo muzikhululukira ena. Muziuza ena za Yehova ndiponso zochita zake.—Yesaya 43:10. Yam'mbuyo Yotsatira Mwina Mungakondenso Kudziwa Izi ESSENTIAL BIBLE TEACHINGS Kodi Mulungu Amavomereza Zipembedzo Zonse? Anthu amaganiza kuti palibe vuto ngati munthu atalowa m’chipembedzo chilichonse. ZOKHUDZA IFEYO N’chifukwa Chiyani Tiyenera Kuphunzira Baibulo—Vidiyo Yathunthu Baibulo likuthandiza anthu ambirimbiri padziko lonse lapansi kupeza mayankho a mafunso ofunika kwambiri. Kodi inunso mungakonde? Sindikizani Patsani ena Patsani ena Kodi Tiyenera Kuchita Chiyani Kuti Tikondweretse Mulungu? MVERANI MULUNGU KUTI MUDZAPEZE MOYO WOSATHA Kodi Tiyenera Kuchita Chiyani Kuti Tikondweretse Mulungu? Chinenero Chamanja cha ku Malawi Kodi Tiyenera Kuchita Chiyani Kuti Tikondweretse Mulungu? https://assetsnffrgf-a.akamaihd.net/assets/ct/f62df3bf2a/images/syn_placeholder_sqr.png