NYIMBO 108

Chikondi Chosatha cha Mulungu

Chikondi Chosatha cha Mulungu

(Yesaya 55:1-3)

  1. 1. M’lungu ndi chikondi.

    Amatikonda kwambiri.

    Anaperekatu Yesu

    N’kuwombola anthu tonse,

    Timayembekezeranso

    Moyo wosangalatsadi.

    (KOLASI)

    Inu nonse a ludzu,

    Dzamweni kwaulere.

    Madzi opatsa moyo;

    Mulungu n’chikondi.

  2. 2. M’lungu ndi chikondi.

    Ntchito zake ndi umboni.

    Wasonyezanso chikondi,

    Popatsa Yesu Ufumu.

    Ufumu wa Yesu pano.

    Wayamba kulamulira.

    (KOLASI)

    Inu nonse a ludzu,

    Dzamweni kwaulere.

    Madzi opatsa moyo;

    Mulungu n’chikondi.

  3. 3. M’lungu ndi chikondi.

    Nafenso tichisonyeze.

    Pothandiza ’nthu ofatsa,

    Kusungatu malamulo.

    Timamvera M’lungu wathu,

    Tilalikira konseko.

    (KOLASI)

    Inu nonse a ludzu,

    Dzamweni kwaulere.

    Madzi opatsa moyo;

    Mulungu n’chikondi.