NYIMBO 11

Chilengedwe Chimatamanda Mulungu

Chilengedwe Chimatamanda Mulungu

(Salimo 19)

  1. 1. Yehova ntchito zanu n’zambiri,

    Zakumwamba zitamanda inu.

    Chilengedwe chinena za inu;

    Ngakhale sichitulutsa mawu.

    Chilengedwe chinena za inu;

    Ngakhale sichitulutsa mawu.

  2. 2. Nzeru yeniyeni ndi yabwino,

    Imateteza okuopani.

    Mfundo zanu zoposa golide​—

    N’zothandiza ana ndi akulu.

    Mfundo zanu zoposa golide​—

    N’zothandiza ana ndi akulu.

  3. 3. Kudziwa inu n’kothandizadi,

    Mawu anu, amapatsa moyo.

    Oyeretsa dzina lanu onse,

    Mudzawapatsatu madalitso.

    Oyeretsa dzina lanu onse,

    Mudzawapatsatu madalitso.