NYIMBO 113

Yehova Amatipatsa Mtendere

Yehova Amatipatsa Mtendere

(Yohane 14:27)

  1. 1. Tamandani Yehova,

    Wamtendereyo.

    Nkhondo adzazithetsa,

    Mwa Mwana wake.

    Adzapambana nkhondo,

    Yachilungamo.

    Mtendere udzabwera,

    Padziko lonse.

  2. 2. Tasiya kulankhula

    Zokhumudwitsa.

    Malupanga, mikondo,

    Zonse tataya.

    Tisungabe mtendere

    Tikhululuke.

    Monga nkhosa za Yesu,

    Zamtenderedi.

  3. 3. Mtendere ndi umboni

    wa madalitso.

    Tasunga malamulo

    a M’lungu wathu.

    Timakonda mtendere,

    Tiusonyeza

    Mpaka M’paradaiso

    Wamtendereyo.