NYIMBO 114

“Khalani Oleza Mtima”

“Khalani Oleza Mtima”

(Yakobo 5:8)

  1. 1. Mbuye wathu Yehova,

    Dzina lake ndi loyera.

    Amafunitsitsatu

    Kuliyeretsa dzinali.

    Mumibadwo yambiri,

    Iye ndi wopirira;

    Amalezanso mtima,

    Ndipo sakutopa.

    Cholinga chake n’choti

    Anthu adzapulumuke.

    Adzapitirizabe

    Kukhala woleza mtima.

  2. 2. Tikamaleza mtima

    Tidzamvera M’lungu wathu.

    Khalidweli n’labwino,

    Timatha kupewa mkwiyo.

    Timaona zabwino

    Mwa ena nthawi zonse.

    Limatithandizanso

    Pa mavuto onse.

    Makhalidwe enanso

    Omwe n’zipatso zamzimu,

    Adzatithandizadi

    Kutsanzira M’lungu wathu.