NYIMBO 119

Tiyenera Kukhala Ndi Chikhulupiriro

Tiyenera Kukhala Ndi Chikhulupiriro

(Aheberi 10:38, 39)

  1. 1. Kale Mulungu ankalankhula

    Kudzera mwa aneneri.

    Lero kudzera mwa Mwana wake,

    Akuti, ‘lapanitu.’

    (KOLASI)

    Kodi chikhulupiriro

    Chathu ndi cholimba ndithu?

    Chikakhala chenicheni,

    M’pamene tingadzapulumuke.

  2. 2. Mosangalala timvera Yesu,

    Tilalikira Ufumu.

    Tilengezabe molimba mtima;

    Anthu amve uthenga.

    (KOLASI)

    Kodi chikhulupiriro

    Chathu ndi cholimba ndithu?

    Chikakhala chenicheni,

    M’pamene tingadzapulumuke.

  3. 3. Talimbatu m’chikhulupiriro;

    Sitidzabwerera m’mbuyo.

    Tidziwa Yehova M’lungu wathu

    Adzatipulumutsa.

    (KOLASI)

    Kodi chikhulupiriro

    Chathu ndi cholimba ndithu?

    Chikakhala chenicheni,

    M’pamene tingadzapulumuke.