NYIMBO 134

Ana Ndi Mphatso Yochokera kwa Mulungu

Ana Ndi Mphatso Yochokera kwa Mulungu

(Salimo 127:3-5)

  1. 1. Mwamuna ’kakhala bambo

    Mkazinso akakhala ndi mwana,

    Ayenera kukumbukira,

    Mwanayo si wawo okha.

    Ndi mphatso yochoka kwa M’lungu;

    Amapatsa chikondi ndi moyo.

    Amapereka malangizo

    Othandizadi kwa makolo.

    (KOLASI)

    Mphatsoyi ndi yopatulika;

    Ndipo muisamalire.

    M’phunzitseni mwana cho’nadi;

    Ndipo mudzamuthandiza.

  2. 2. Mawu onse a Mulungu​—

    Azikhalatu pamtima panu.

    Muziuzanso ana anu,

    Uwu ndi udindo wanu.

    Muziwaphunzitsa poyenda,

    Podzuka ndi pa nthawi yopuma.

    Akamakula saiwala,

    Adzalandira madalitso.

    (KOLASI)

    Mphatsoyi ndi yopatulika;

    Ndipo muisamalire.

    M’phunzitseni mwana cho’nadi;

    Ndipo mudzamuthandiza.