NYIMBO 139

Yerekezerani Kuti Muli M’dziko Latsopano

Yerekezerani Kuti Muli M’dziko Latsopano

(Chivumbulutso 21:1-5)

  1. 1. Yerekeza ukuona;

    Iwe ndi ’ne m’dziko latsopano.

    Ona mmene udzamvere

    Kukhala m’dziko lamtendere.

    Oipa onse achoka.

    M’lungu wathu sadzalephera.

    Kusintha zonse padziko lapansi,

    Tidzamuimbira nyimbo

    tikumati:

    (KOLASI)

    “Tikuthokoza mwachita bwino.

    Zonse zakhaladi zatsopano.

    Tikuimba nyimbo mwachisangalalo

    Ndinudi woyenera ulemerero.”

  2. 2. Taganizira m’tsogolo;

    Iwe ndi ’ne m’dziko latsopano.

    Sitidzamva ndi kuona

    Zinthu zotichititsa mantha.

    Mmene analonjezera;

    Zinthu zonse zachitikadi.

    Tsopano aku’kitsanso akufa;

    Iwo ndi ife

    tidzamuyamikira:

    (KOLASI)

    “Tikuthokoza mwachita bwino.

    Zonse zakhaladi zatsopano.

    Tikuimba nyimbo mwachisangalalo

    Ndinudi woyenera ulemerero.”