NYIMBO 2

Dzina Lanu Ndinu Yehova

Dzina Lanu Ndinu Yehova

(Salimo 83:18)

  1. 1. Mulungu woona—

    Mlengi wa zinthu zonse

    Mulungu wamuyaya—

    Ndinudi Yehova.

    Ndifetu amwayi

    Kukhala anthu anu.

    Tilengeza za inu,

    Ku mitundu yonse.

    (KOLASI)

    Yehova, Yehova,

    M’lungu ndinu nokha.

    Kumwambako ndi padziko

    Palibenso wina.

    Ndinudi Wamphamvuyonse

    Onsetu adziwe.

    Yehova, Yehova,

    M’lungu wathu ndinu nokha.

  2. 2. Tingathe kukhala

    Chilichonse mwafuna.

    Tigwire ntchito yanu—

    Ndinudi Yehova.

    Mwatipatsa dzina

    Tikhale Mboni zanu.

    Uwu ndi mwayi wathu—

    Tikutamandani.

    (KOLASI)

    Yehova, Yehova,

    M’lungu ndinu nokha.

    Kumwambako ndi padziko

    Palibenso wina.

    Ndinudi Wamphamvuyonse

    Onsetu adziwe.

    Yehova, Yehova,

    M’lungu wathu ndinu nokha.