NYIMBO 24

Bwerani Kuphiri la Yehova

Bwerani Kuphiri la Yehova

(Yesaya 2:2-4)

  1. 1. Phiri la Yehova,

    Tangoliyang’anani.

    Latalika kuposa

    Ena onse lero.

    Anthu akubwera,

    Kuchokera kutali,

    Akuitanizana,

    ‘Bwerani kwa M’lungu.’

    Tsopano wamng’ono

    Wakhala mtundu waukulu,

    Tikuona kuti,

    Tikudalitsidwa ndi M’lungu.

    Ambiri tsopano

    Akuvomerezadi.

    Ulamuliro wake

    Mokhulupirika.

  2. 2. Yesu walamula

    Kuti tipite ndithu.

    Tikalalikire

    Uthenga wa Ufumu.

    Khristu wayambano

    Ulamuliro wake.

    Iye akuti tikhale

    Kumbali yake.

    Ndi zosangalatsa,

    Kuona khamu lalikulu.

    Likukulirabe,

    Ndipo tonse tikuthandiza.

    Tonse tifuule,

    Tiitanetu anthu,

    ‘Bwerani kuphiri

    la Yehova Mulungu.’