NYIMBO 40

Kodi Ndife a Ndani?

Kodi Ndife a Ndani?

(Aroma 14:8)

  1. 1. Iwe ndi wandani?

    Umvera m’lungu uti?

    Amene umam’gwadirayo.

    Iye ndiye m’lungu wako.

    Milungu iwiri;

    Sungaitumikire.

    Sungalambire iwiri yonse,

    Sankhapo mmodzi yekha.

  2. 2. Iwe ndi wandani?

    Umvera m’lungu uti?

    Zilitu ndi iwe kusankha,

    Woona kaya wonama.

    Kodi Kaisara

    Udakamukondabe?

    Kapena udzamvera Yehova

    N’kugwira ntchito yake?

  3. 3. Ine ndi wandani?

    Ndidzamvera Yehova.

    Atate wanga wakumwamba;

    Ine ndidzam’sangalatsa.

    Anandigulatu;

    Ndidzamutumikira.

    Ndizim’lambira, dzina lakenso

    Ndizililemekeza.