NYIMBO 76

Kodi Mumamva Bwanji?

Kodi Mumamva Bwanji?

(Aheberi 13:15)

  1. 1. Kodi m’mamva bwanji

    m’kazindikira kuti,

    mwasonyezadi khama

    pophunzitsa ena?

    Inde m’kayesetsa,

    M’lungu adzadalitsa.

    Mudzathandiza anthu

    kudziwa Mulungu.

    (KOLASI)

    Timasangalala ndithu

    kupereka mtima wathu.

    Choncho tim’tumikirebe

    tsiku lililonse.

  2. 2. Kodi m’mamva bwanji

    m’kazindikira kuti,

    mwawafika pamtima

    akamva uthenga?

    Ena amakana,

    ena kunamizidwa.

    Koma timanyadira

    tikalalikira.

    (KOLASI)

    Timasangalala ndithu

    kupereka mtima wathu.

    Choncho tim’tumikirebe

    tsiku lililonse.

  3. 3. Kodi m’mamva bwanji

    m’kakumbukira kuti,

    mwa chikondi Yehova

    amatsogolera?

    Timalalikira,

    anthu timaphunzitsa,

    akhale ndi tsogolo

    adzapeze moyo.

    (KOLASI)

    Timasangalala ndithu

    kupereka mtima wathu.

    Choncho tim’tumikirebe

    tsiku lililonse.