NYIMBO 88

Ndidziwitseni Njira Zanu

Ndidziwitseni Njira Zanu

(Salimo 25:4)

  1. 1. Yehova tasonkhanatu pamodzi,

    Pomvera kuitana kwanu.

    Mawu anu ndi nyale m’njira yathu,

    Amatiphunzitsa za inu.

    (KOLASI)

    Ndiphunzitseni njira zanuzo;

    Ndikhale womvera malamulo.

    Ndiyendetseni m’njira yoona,

    Malamulo anu ndizikonda.

  2. 2. Nzeru zanu Yehova ndi zakuya,

    Mfundo zanu n’zolimbikitsa.

    Mawu anu adzakhala kosatha,

    Timapezamo zodabwitsa.

    (KOLASI)

    Ndiphunzitseni njira zanuzo;

    Ndikhale womvera malamulo.

    Ndiyendetseni m’njira yoona,

    Malamulo anu ndizikonda.