NYIMBO 95

Kuwala Kukuwonjezerekabe

Kuwala Kukuwonjezerekabe

(Miyambo 4:18)

  1. 1. Aneneri akale ankafuna,

    Kudziwa za Yesu Mesiya.

    Mzimu wa M’lungu unaneneratu,

    Kuti adzatipulumutsa.

    Nthawi yakwana, akulamulira,

    Umboni wake ulipo.

    Kudziwa zimenezi ndi mwayi

    Waukulu womwe tili nawo.

    (KOLASI)

    Kuwala kwa panjira yathu;

    Kukuwonjezerekadi.

    Zomwe M’lungu akuulula;

    Zimatitsogoleradi.

  2. 2. Ambuye wathu wasankha kapolo,

    Ndi mmene amatidyetsera.

    Ndipo kuwala kwa cho’nadi pano

    Kukungowonjezerekabe.

    Pano tikuyenda molimba mtima,

    Mowala ngati masana.

    Tikuthokoza Yehova chifukwa,

    Cho’nadi chake watipatsa.

    (KOLASI)

    Kuwala kwa panjira yathu;

    Kukuwonjezerekadi.

    Zomwe M’lungu akuulula;

    Zimatitsogoleradi.